< Deuteronomo 4 >

1 Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
“Zwana-ke khathesi, Oh Israyeli, izimiso lemithetho engizalifundisa yona. Ilandeleni ukuze liphile njalo libe lakho ukuyalithatha lelolizwe uThixo uNkulunkulu wabokhokho benu alinika lona.
2 Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
Lingangezeleli kulokho engililaya khona njalo lingaphunguli loba yikuphi kwakhona, kodwa gcinani imilayo kaThixo uNkulunkulu wenu engilinika yona.
3 Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
Lazibonela ngawenu amehlo okwenziwa nguThixo eBhali-Pheyori. UThixo uNkulunkulu wenu wabatshabalalisa bonke ababekhonza uBhali wasePheyori,
4 Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
kodwa lina lonke elabambelela kuThixo uNkulunkulu wenu lilokhu lisaphila lalamuhla lokhu.
5 Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
Liyabona sengalifundisa izimiso lemithetho uThixo wami angilaya ngazo, ukuze liyigcine elizweni elingena kulo ukuba lilithathe.
6 Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
Lizigcine ngonanzelelo ngoba lokhu kuzaveza obala ukuhlakanipha lokuzwisisa kwenu ezizweni ezizakuzwa ngalezizimiso njalo zitsho zithi, ‘Ngeqiniso lesisizwe esilodumo yisizwe sabantu abahlakaniphileyo njalo abazwisisayo.’
7 Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
Yisiphi esinye isizwe esilodumo esilabonkulunkulu baso ababaseduze laso njengoThixo uNkulunkulu wethu oba lathi nxa sikhuleka kuye?
8 Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
Yisiphi esinye isizwe esilezimiso eziqondileyo lemithetho enjengale imithetho engiyethula phambi kwenu lamuhla na?
9 Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
Kodwa linanzelele, liqaphelisise ukuze lingakhohlwa izinto elizibonileyo loba zilibaleke ezinhliziyweni zenu ekuphileni kwenu konke. Fundisani abantwabenu ngalezizinto njalo labo babofundisa abantwababo labantwana babantwana abalandela emva kwabo.
10 Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
Khumbulani usuku elema ngalo phambi kukaThixo uNkulunkulu wenu eHorebhi, lapho athi khona kimi, ‘Buthanisa abantu ukuze bezwe amazwi ami ukuze bakwazi ukungidumisa nxa belokhu besahlala elizweni njalo bafundise abantwababo.’
11 Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
Lasondela lema ngaphansi kwentaba ilavuka amalangabi eqonga phezulu, kulamayezi amnyama lomnyama owesabekayo.
12 Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
Ngakho uThixo wakhuluma lani ephakathi komlilo. Lezwa umdumo welizwi kodwa alizange libone lutho; kwaba yilizwi lodwa nje.
13 Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
Wakhupha ilizwi lokubuyisana lesivumelwano sakhe, imiThetho eliTshumi, waselilaya ukuba liyilandele njalo wayiloba ezibhebhedwini zamatshe ezimbili.
14 Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
Kungalesosikhathi lapho uThixo angiqondisa ukuba ngilifundise izimiso lemilayo okuzamele liyilandele ekuchapheni kwenu uJodani lisiya elizweni elizalithumba libe ngelenu.”
15 Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
“Akulalutho loba yisimo bani elasibonayo mhla uThixo ekhuluma lani eHorebhi ephakathi kwelangabi lomlilo. Kunjalo-nje kumele lizinanzelele okuqinileyo,
16 kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
ukuze lingaxhwali libe selizenzela isithombe, loba umfanekiso olesimo bani, loba ngesilesimo sesilisa loba esesifazane,
17 kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
loba yiphi inyamazana emhlabeni loba inyoni endizayo emkhathini,
18 Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
loba yisiphi isinanakazana esihuquzelayo emhlabathini loba yinhlanzi ngaphansi kwamanzi.
19 Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
Njalo nxa likhangela phezulu esibhakabhakeni libona ilanga, inyanga kanye lezinkanyezi, zonke ezihlobise zacecisa isibhakabhaka, lingalingeki lizikhothamele beselikhonza izinto uThixo uNkulunkulu wenu azibekela izizwe zonke ngaphansi kwezulu.
20 Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
Kodwa-ke lina, uThixo walithatha walenyula eziko lokuncibilikisa insimbi, walikhipha eGibhithe, ukuze libe ngabantu belifa lakhe, njengoba linje lamuhla.
21 Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
UThixo wangithukuthelela ngenxa yenu, wafunga waphelela wathi angiyikuchapha uJodani ngingene elizweni uThixo uNkulunkulu wenu alinika lona ukuba libe yilifa lenu.
22 Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
Mina ngizafela kulelilizwe; angiyikuchapha uJodani, kodwa lina seliseduze ukuba lichaphe liyelithumba lelolizwe elihle.
23 Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
Nanzelelani ukuthi lingalibali isivumelwano sikaNkulunkulu wenu asenza lani; lingazenzeli isithombe loba singesesimo bani salokho uThixo uNkulunkulu wenu akwalileyo.
24 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
Ngoba uThixo uNkulunkulu wenu ungumlilo oqothulayo, uNkulunkulu olobukhwele.
25 Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
Ngemva kokuba selike laba labantwana, lesizukulwane njalo selihlale ezweni okwesikhathi eside, lingasuka libe selixhwala beselizenzela loba yisiphi isithombe, lisenza okubi emehlweni kaThixo uNkulunkulu wenu limthukuthelisa,
26 ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
ngibiza izulu lomhlaba ukuthi libe ngufakazi wami ukuze libhujiswe masinyazana lingangeni elizweni elizachapha uJodani ukuze lilithumbe. Aliyikuhlala kulo isikhathi eside kodwa iqiniso yikuthi lizatshabalaliswa.
27 Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
UThixo uzalihlakaza ezizweni, njalo abalutshwana benu yibo abazasinda ezizweni uThixo azalifuqela khona.
28 Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
Khonale lizakhonza onkulunkulu ababunjwe ngabantu ngezigodo langamatshe, abangeke babone loba bezwe loba badle loba bezwe ukunuka.
29 Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Kodwa nxa likhonale lingadinga uThixo uNkulunkulu wenu, lizamfumana nxa limdinga ngezinhliziyo zenu ezipheleleyo langemiphefumulo yenu yonke.
30 Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
Nxa selisosizini zonke lezizinto sezilehlela, lapho-ke ngezinsuku ezizayo lizabuyela kuThixo uNkulunkulu wenu limlalele.
31 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
Phela uThixo uNkulunkulu wenu nguNkulunkulu olomusa; kayikulidela loba alibhubhise loba alibale isivumelwano sakhe asenza labokhokho benu, leso asiqinisa kubo ngesifungo.”
32 Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
“Buzani khathesi ngezinsuku ezedlulayo, kudala lingakabi khona, kusukela ngosuku uNkulunkulu adala ngalo umuntu emhlabeni; buzani kusukela ngapha kwamazulu kusiya ngale kwamazulu. Kambe kukhona yini okukhulu kangaka okwedlula lokhu osekuke kwenzakala loba kwezwakala na?
33 Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
Sikhona na esinye isizwe esake sezwa uNkulunkulu ekhuluma ephakathi kwelangabi lomlilo, njengalokhu eselikuzwile, saphila na?
34 Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
Kukhona na unkulunkulu oseke wazama ukuzithathela esinye isizwe phakathi kwesinye, ngokuhlola, ngemilingo yezibonakaliso, lezimangaliso, lezimpi, ngesandla esilamandla langokwelula ingalo, loba izenzo ezinkulu ezesabekayo, njengakho konke uThixo uNkulunkulu wenu alenzela khona eGibhithe lizibonela ngamehlo enu?
35 Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
Lakutshengiswa konke lokhu ukuze lazi ukuthi uThixo unguNkulunkulu; ngaphandle kwakhe kakho omunye futhi.
36 Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
Esemazulwini wakwenza ukuthi lilizwe ilizwi lakhe ukuze libe lobuntu. Emhlabeni walitshengisa amalangabi omlilo akhe omkhulu, njalo lawezwa amazwi akhe ephuma emlilweni.
37 Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
Ngenxa yokuthi wabathanda okhokho benu wakhetha izizukulwane zabo ezalandela ngemva kwabo, walikhipha eGibhithe ngoBukhona bakhe kanye langamandla akhe amakhulu,
38 kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
ukuxotsha zonke izizwe phambi kwenu, izizwe ezilamandla kulezenu lokulingenisa elizweni lazo ukuze aliphe lona libe yilifa lenu, njengoba kunjalo lamuhla.
39 Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
Yamukelani njalo likugcine ezinhliziyweni zenu lamuhla ukuthi uThixo unguNkulunkulu ezulwini phezulu lasemhlabeni phansi. Kakho omunye.
40 Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
Gcinani izimiso zakhe lemilayo yakhe, engilinika yona lamuhla, ukuze kulihambele kahle lina kanye labantwabenu lokuthi liphile isikhathi eside elizweni eliliphiwa nguThixo uNkulunkulu wenu ukuze libe ngelenu kokuphela.”
41 Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
Ngakho uMosi wasekhetha amadolobho amathathu empumalanga yeJodani,
42 kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
ukuze kuthi wonke oyabe ebulele omunye abalekele khona nxa eyabe ebulele umakhelwane kungekho mona kodwa kube yingozi. Bangabalekela kwelinye lala amadolobho ukuze baphephise impilo zabo.
43 Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
Amadolobho lawo kwakuyila: iBhezeri emagcekeni asenkangala, lingelabakoRubheni; iRamothi eGiliyadi, lingelabakoGadi; kanye lelaseGolani eBhashani lona lingelabakoManase.
44 Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
Lo ngumthetho owethulwa nguMosi kwabako-Israyeli.
45 Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
Lezi kwakuyizilinganiso, izimiso lemithetho eyethulwa nguMosi kubo ekuphumeni kwabo eGibhithe
46 Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
njalo babesesigodini esiseduzane leBhethi-Pheyori empumalanga yeJodani elizweni likaSihoni inkosi yama-Amori, yena owabusa eHeshibhoni njalo wehlulwa nguMosi labako-Israyeli bephuma eGibhithe.
47 Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
Bathatha ilizwe lakhe kanye lelizwe lika-Ogi inkosi yaseBhashani, amakhosi ama-Amori womabili empumalanga yeJodani.
48 Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
Ilizwe leli lalisuka e-Aroweri emaphethelweni ezindonga zase-Arinoni kusiya entabeni yaseSiyoni (khona kuyiHemoni),
49 ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.
kuhlanganisa layo yonke i-Arabha empumalanga yeJodani kuze kuyefika oLwandle lwe-Arabha, ngaphansi komthezuko wasePhisiga.

< Deuteronomo 4 >