< Deuteronomo 4 >

1 Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
And now, thou Israel, here the comaundementis and domes whiche Y teche thee, that thou do tho, and lyue, and that thow entre and welde the lond which the Lord God of youre fadris schal yyue to you.
2 Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
Ye schulen not adde to the word which Y speke to you, nether ye schulen take awei `fro it; kepe ye the comaundementis of youre Lord God, which Y comaunde to you.
3 Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
Youre iyen sien alle thingis whiche the Lord dide ayens Belphegor; how he alto brak alle the worschiperis `of hym fro the myddis of you.
4 Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
Forsothe ye that cleuen to youre Lord God lyuen alle `til in to present day.
5 Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
Ye witen that Y tauyte you the comaundementis and riytfulnessis, as my Lord God comaundide to me; so ye schulen do tho in the lond whiche ye schulen welde,
6 Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
and ye schulen kepe, and schulen fille in werk. For this is youre wisdom and vndurstondyng bifor puplis, that alle men here these comaundementis, and seie, Lo! a wise puple and vnderstondynge! a greet folk!
7 Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
Noon other nacioun is so greet, `not in noumbre ether in bodili quantite, but in dignite, that hath Goddis neiyynge to it silf, as oure God is redi to alle oure bisechyngis.
8 Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
For whi what other folk is so noble, that it hath cerymonyes and iust domes, and al the lawe which Y schal `sette forth to dai bifor youre iyen?
9 Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
Therfor kepe thi silf, and thi soule bisili; foryete thou not the wordis whiche thin iyen sien, and falle tho not doun fro thin herte, in alle the daies of thi lijf. Thou schalt teche tho thi sones and thi sones sones.
10 Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
Telle thou the day in which thou stodist bifor thi Lord God in Oreb, whanne the Lord spak to me, and seide, Gadere thou the puple to me, that it here my wordis, and lerne for to drede me in al tyme in which it lyueth in erthe, and teche hise sones.
11 Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
And ye neiyiden to the `roote of the hille, that brente `til to heuene; and derknessis, and cloude, and myist weren therynne.
12 Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
And the Lord spak to you fro the myddis of fier; ye herden the vois of hise wordis, and outirli ye sien no fourme.
13 Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
And he schewide to you his couenaunt, which he comaundide, that ye schulden do, and `he schewide ten wordis, whiche he wroot in two tablis of stoon.
14 Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
And he comaundide to me in that tyme, that Y schulde teche you cerymonyes and domes, whiche ye owen to do in the lond whiche ye schulen welde.
15 Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
Therfor kepe ye bisili youre soulis; ye sien not ony licnesse in the dai in which the Lord spak to you in Oreb, fro the myddis of the fier;
16 kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
lest perauenture ye be disseyued and make to you a grauun licnesse, ether an ymage of male, ether of female;
17 kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
a licnesse of alle beestis that ben on erthe, ether of bridis fleynge vndur heuene,
18 Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
and of crepynge beestis that ben moued in erthe, ether of fischis that dwellen vndur the erthe in watris; lest perauenture,
19 Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
whanne thin iyen ben reisid to heuene, thou se the sonne, and moone, and alle the sterris of heuene, and be disseyued bi errour, and worschipe tho, `bi outermer reuerence, and onour, `bi ynner reuerence, `tho thingis whiche thi Lord God made of nouyt, in to seruyce to alle folkis that ben vndur heuene.
20 Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
Forsothe the Lord took you, and ledde out of the yrun furneys of Egipt, that he schulde haue a puple of eritage, as it is in `present dai.
21 Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
And the Lord was wrooth ayens me for youre wordis, and swoor that Y schulde not passe Jordan, and schulde not entre in to the beeste lond, which he schal yyue to you.
22 Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
Lo! Y die in this erthe; Y schal not passe Jordan; ye schulen passe, and schulen welde the noble lond.
23 Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
Be thou war, lest ony tyme thou foryete the couenaunt of thi Lord God, which he made with thee, and lest thou make to thee a grauun licness of tho thingis whiche the Lord forbeed to make.
24 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
For thi Lord God is fier wastynge; `God, a feruent louyere.
25 Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
If ye gendren sones, and sones of sones, and ye dwellen in the lond, and ye be disceyued, and make to you ony licnesse, and doen yuel bifor youre Lord God, that ye terren hym to greet wrathe,
26 ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
Y clepe witnesses to dai heuene and erthe, `that is, ech resonable creature beynge in heuene and in erthe, that ye schulen perische soone fro the lond, which ye schulen welde, whanne ye han passid Jordan; ye schulen not dwelle long tyme therynne, but the Lord schal do awey you,
27 Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
and schal scatere `in to alle hethen men, and ye schulen leeue fewe among naciouns, to whiche the Lord schal lede you.
28 Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
And there ye schulen serue to goddis, that ben maad bi `the hond of men, to a tre and a stoon, that `seen not, nether heren, nether eten, nether smellen.
29 Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
And whanne thou hast souyt there thi Lord God, thou schalt fynde hym; if netheles thou sekist with al the herte, and with al the tribulacioun of thi soule.
30 Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
Aftir that alle thingis han founde thee, that ben biforseid, forsothe in the laste tyme, thou schalt turne ayen to thi Lord God, and thou schalt here his vois.
31 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
For thi Lord God is merciful God; he schal not forsake thee, nethir he schal do awey outirli, nethir he schal foryete the couenaunt, in which he swoor to thi fadris.
32 Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
Axe thou of elde daies that weren bifor thee, fro the day in which thi Lord God made of nouyt man on erthe, axe thou fro that oon ende of heuene `til to the tother ende therof, if sich a thing was doon ony tyme, ether if it was euere knowun,
33 Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
that a puple herde the vois of God spekynge fro the myddis of the fier, as thou herdist, and siest;
34 Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
if God `dide, that he entride, and took to him silf a folc fro the middis of naciouns, bi temptaciouns, myraclis, and grete wondris, bi batel, and strong hond, and arm holdun forth, and orrible siytis, bi alle thingis whiche youre Lord God dide for you in Egipt, `while thin iyen sien;
35 Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
that thou schuldist wite, that the Lord hym silf is God, and noon other is, outakun oon.
36 Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
Fro heuene he made thee to here his vois, that he schulde teche thee; and in erthe he schewide to thee his grettiste fier, and thou herdist the wordis `of hym fro the myddis of the fier;
37 Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
for he louyde thi fadris, and chees her seed aftir hem. And he ledde thee out of Egipt, and yede bifore in his greet vertu,
38 kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
that he schulde do awei grettiste naciouns, and strongere than thou, in thin entryng, and that he schulde lede thee ynne, and schulde yyue to thee the lond `of hem in to possessioun, as thou seest in `present day.
39 Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
Therfor wite thou to dai, and thenke in thin herte, that the Lord him silfe is God in heuene aboue, and in erthe bynethe, and noon other is.
40 Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
Kepe thou hise heestis, and comaundementis, whiche Y comaunde to thee, that it be wel to thee, and to thi sones after thee, and that thou dwelle mych tyme on the lond, which thi Lord God schal yyue to thee.
41 Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
Thanne Moises departide thre citees biyende Jordan at the eest coost,
42 kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
that he fle to tho, that sleeth his neighbore not wilfuli, and was not enemy bifore oon and `the tother dai, and that he mai fle to summe of these citees;
43 Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
Bosor in the wildirnesse, which is set in the feeldi lond, of the lynage of Ruben; and Ramoth in Galaad, which is in the lynage of Gad; and Golan in Basan, which is in the lynage of Manasses.
44 Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
This is the lawe which Moises `settide forth bifor the sones of Israel,
45 Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
and these ben the witnessyngis, and cerymonyes, and domes, whiche he spak to the sones of Israel, whanne thei yeden out of Egipt,
46 Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
biyende Jordan, in the valey ayens the temple of Phegor, in the lond of Seon, kyng of Ammorreis, that dwellide in Esebon, whom Moises killide. And the sones of Israel yeden out of Egipt, and weldiden `the lond of him,
47 Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
and the lond of Og, kyng of Basan, twei kyngis of Ammoreis, that weren biyende Jordan, at the rysyng of the sunne;
48 Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
fro Aroer which is set on the brenke of the stronde of Arnon, `til to the hil of Seon, which is Hermon;
49 ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.
thei weldiden al the pleyn biyende Jordan, at the eest coost, `til to the see of wildirnesse, and `til to the rootis of the hil of Phasga.

< Deuteronomo 4 >