< Deuteronomo 4 >
1 Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
Now, Israel [God prevails], sh'ma ·hear obey· the statutes and to the judgments, which I teach you, to do them; that you may live, and go in and possess the land which Adonai, the God of your fathers, gives you.
2 Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
You shall not add to the word which I enjoin you, neither shall you take away from it, that you may keep the mitzvot ·instructions· of Adonai your God which I enjoin you.
3 Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
Your eyes have seen what Adonai did because of Baal Peor; for all the men who followed Baal Peor, Adonai your God has destroyed them from among you.
4 Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
But you who were faithful to Adonai your God are all alive today.
5 Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
Behold, I have taught you statutes and judgments, even as Adonai my God enjoined me, that you should do so in the middle of the land where you go in to possess it.
6 Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
Keep therefore and do them; for this is your wisdom and your understanding in the sight of the peoples, who shall sh'ma ·hear obey· all these statutes, and say, “Surely this great nation is a wise and understanding people.”
7 Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
For what great nation is there, that has a deity so near to them, as Yahweh Eloheikhem [Yahweh our God] is whenever we call on him?
8 Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
What great nation is there, that has statutes and judgement so upright as all this Torah ·Teaching·, which I set before you today?
9 Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
Only be careful, and keep your soul diligently, lest you forget the things which your eyes saw, and lest they depart from your heart all the days of your life; but make them known to your children and your children’s children;
10 Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
the day that you stood before Adonai your God in Horeb [Desert], when Adonai said to me, “Assemble the people to me, and I will make them sh'ma ·hear obey· my words, that they may learn to fear me all the days that they live on the earth, and that they may teach their children.”
11 Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
You came near and stood under the mountain. The mountain burned with fire to the heart of the sky, with darkness, cloud, and thick darkness.
12 Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
Adonai spoke to you out of the middle of the fire: you sh'ma ·hear obey· the voice of words, but you saw no form; you only heard a voice.
13 Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
He declared to you his covenant ·binding contract between two or more parties·, which he enjoined you to perform, even the Ten Words. He wrote them on two stone tablets.
14 Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
Adonai enjoined me at that time to teach you statutes and judgments, that you might do them in the land where you go over to possess it.
15 Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
Be very careful, for you saw no kind of form on the day that Adonai spoke to you in Horeb [Desert] out of the middle of the fire,
16 kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
lest you corrupt yourselves, and make yourself an engraved image in the form of any figure, the likeness of male or female,
17 kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
the likeness of any animal that is on the earth, the likeness of any winged bird that flies in the sky,
18 Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
the likeness of anything that creeps on the ground, the likeness of any fish that is in the water under the earth;
19 Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
and lest you lift up your eyes to the sky, and when you see the sun and the moon and the stars, even all the army of the sky, you are drawn away and worship them, and abad ·serve· them, which Adonai your God has allotted to all the peoples under the whole sky.
20 Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
But Adonai has taken you, and brought you out of the iron furnace, out of Egypt [Abode of slavery], to be to him a people of inheritance, as it is today.
21 Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
Furthermore Adonai was angry with me for your sakes, and swore that I should not go over the Jordan [Descender], and that I should not go in to that good land, which Adonai your God gives you for an inheritance;
22 Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
but I must die in this land. I must not go over the Jordan [Descender]; but you shall go over, and possess that good land.
23 Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
Be careful, lest you forget the covenant ·binding contract between two or more parties· of Adonai your God, which he made with you, and make yourselves an engraved image in the form of anything which Adonai your God has enjoined forbidden for you.
24 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
For Yahweh [He sustains breathing] your God is 'Akal 'Esh [Consuming Fire], El Kana' [Jealous God].
25 Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
When you shall father children, and children’s children, and you shall have been long in the land, and shall corrupt yourselves, and make an engraved image in the form of anything, and shall do that which is evil in Adonai your God’s sight, to provoke him to anger;
26 ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
I call heaven and earth to witness against you today, that you will soon utterly perish from off the land which you go over the Jordan [Descender] to possess it. You will not prolong your days on it, but will utterly be destroyed.
27 Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
Adonai will scatter you among the peoples, and you will be left few in number among the nations, where Adonai will lead you away.
28 Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
There you shall abad ·serve· deities, the work of men’s hands, wood and stone, which neither see, nor sh'ma ·hear obey·, nor eat, nor smell.
29 Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
But from there you shall seek Adonai your God, and you shall find him, when you search after him with all your heart and with all your soul.
30 Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
When you are in oppression, and all these things have come on you, in the latter days you shall teshuvah ·completely return· to Adonai your God, and sh'ma ·hear obey· to his voice.
31 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
For Adonai your God is a merciful God. He will not fail you, neither destroy you, nor forget the covenant ·binding contract between two or more parties· of your fathers which he swore to them.
32 Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
For ask now of the days that are past, which were before you, since the day that God created man on the earth, and from the one end of the sky to the other, whether there has been anything as this great thing is, or has been sh'ma ·heard obeyed· like it?
33 Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
Did a people ever sh'ma ·hear obey· the voice of God speaking out of the middle of the fire, as you have sh'ma ·heard obeyed·, and live?
34 Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
Or has God tried to go and take a nation for himself from among another nation, by trials, by signs, by wonders, by war, by a mighty hand, by an outstretched arm, and by great terrors, according to all that Adonai your God did for you in Egypt [Abode of slavery] before your eyes?
35 Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
It was shown to you so that you might know that Yahweh [He sustains breathing] is God. There is no one else besides him,
36 Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
Out of heaven he made you to sh'ma ·hear obey· his voice, that he might instruct you. On earth he made you to see his great fire; and you sh'ma ·heard obeyed· his words out of the middle of the fire.
37 Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
Because he 'ahav ·affectionately loved· your fathers, therefore he chose their offspring after them, and brought you out with his presence, with his great power, out of Egypt [Abode of slavery];
38 kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
to drive out nations from before you greater and mightier than you, to bring you in, to give you their land for an inheritance, as it is today.
39 Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
Know therefore today, and take it to heart, that Yahweh [He sustains breathing] himself is God in heaven above and on the earth beneath. There is no one else.
40 Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
You shall keep his statutes, and his mitzvot ·instructions·, which I enjoin you today, that it may go well with you, and with your children after you, and that you may prolong your days in the land, which Adonai your God gives you, forever.
41 Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
Then Moses [Drawn out] set apart three cities beyond the Jordan [Descender] toward the sunrise;
42 kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
that the man slayer might flee there, who kills his neighbor unawares, and didn’t hate him in time past; and that fleeing to one of these cities he might live:
43 Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
Bezer in the wilderness, in the plain country, for the Reubenites; and Ramoth in Gilead, for the Gadites; and Golan in Bashan, for the Manassites.
44 Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
This is the Torah ·Teaching· which Moses [Drawn out] set before the children of Israel [God prevails].
45 Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
These are the testimonies, and the statutes, and the judgments, which Moses [Drawn out] spoke to the children of Israel [God prevails], when they came out of Egypt [Abode of slavery],
46 Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
beyond the Jordan [Descender], in the valley over against Beth Peor, in the land of Sihon king of the Amorites [Descendants of Talkers], who lived at Heshbon, whom Moses [Drawn out] and the children of Israel [God prevails] struck, when they came out of Egypt [Abode of slavery].
47 Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
They took his land in possession, and the land of Og king of Bashan, the two kings of the Amorites [Descendants of Talkers], who were beyond the Jordan [Descender] toward the sunrise;
48 Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
from Aroer, which is on the edge of the valley of the Arnon, even to Mount Sion (also called Hermon [Devoted to destruction]),
49 ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.
and all the Arabah beyond the Jordan [Descender] eastward, even to the sea of the Arabah, under the slopes of Pisgah.