< Deuteronomo 34 >
1 Ndipo Mose anakwera Phiri la Nebo kuchokera ku chigwa cha Mowabu ndi kukafika pamwamba pa Phiri la Pisiga, kummawa kwa Yeriko. Kumeneko Yehova anamuonetsa dziko lonse; kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani.
Mojzes se je iz moábskih ravnin dvignil na goro Nebó, k vrhu Pisge, ki je nasproti Jerihe. In Gospod mu je pokazal vso deželo Gileád, do Dana
2 Dera lonse la Nafutali, dziko lonse la Efereimu ndi Manase, dziko lonse la Yuda mpaka kukafika kumadzulo kwa nyanja,
in ves Neftáli, Efrájimovo in Manásejevo deželo in vso Judovo deželo, do skrajnega morja,
3 Negevi ndi chigawo chonse kuchokera ku Chigwa cha Yeriko, Mzinda wa mitengo ya migwalangwa, mpaka ku Zowari.
in jug in ravnino jerihonske doline, mesto palmovih dreves, do Coarja.
4 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti, “Limenelo ndi dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo pamene ndinanena kuti, ‘Ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’ Ndakulola kuti ulione, koma sudzawoloka kuti ukalowemo.”
Gospod mu je rekel: »To je dežela, ki sem jo prisegel Abrahamu, Izaku in Jakobu, rekoč: ›Dal jo bom tvojemu semenu.‹ Dal sem ti, da jo vidiš s svojimi očmi, toda ne boš šel tja preko.«
5 Choncho Mose mtumiki wa Yehova anamwalira kumeneko ku Mowabu, monga momwe ananenera Yehova.
Tako je Gospodov služabnik Mojzes umrl tam v moábski deželi, glede na Gospodovo besedo.
6 Yehova anamuyika mʼmanda ku Mowabu, mʼchigwa choyangʼanana ndi Beti-Peori, koma mpaka lero palibe amene amadziwa pamene pali manda ake.
Pokopal ga je v dolini, v moábski deželi nasproti Bet Peórja, toda noben človek ne pozna njegovega mavzoleja do današnjega dne.
7 Mose anamwalira ali ndi zaka 120, koma maso ake ankaonabe ndipo anali amphamvu.
Mojzes je bil star sto dvajset let, ko je umrl. Njegovo oko ni bilo zatemnjeno niti se njegova naravna sila ni zmanjšala.
8 Aisraeli analira maliro a Mose mʼchikhwawa cha Mowabu kwa masiku makumi atatu mpaka nthawi ya kulira maliro ndi kukhuza inatha.
Izraelovi otroci so na moábskih ravninah trideset dni jokali za Mojzesom; tako so bili dnevi jokanja in žalovanja za Mojzesom končani.
9 Tsono Yoswa, mwana wa Nuni anadzazidwa ndi mzimu wanzeru chifukwa nʼkuti Mose atamusanjika manja. Choncho Aisraeli anamumvera ndipo anachita zomwe Yehova analamula Mose.
Nunov sin Józue pa je bil poln duha modrosti, kajti Mojzes je nanj položil svoji roki in Izraelovi otroci so mu prisluhnili in storili, kakor je Gospod zapovedal Mojzesu.
10 Kuyambira nthawi imeneyi, mu Israeli simunakhalepo mneneri wina aliyense wofanana ndi Mose, amene Yehova amayankhula naye maso ndi maso.
In od takrat v Izraelu ni vstal prerok, podoben Mojzesu, ki ga je Gospod poznal iz obličja v obličje,
11 Amene anachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi ndi zozizwitsa zimene Yehova anamutuma kuti achite mu Igupto, kwa Farao ndi kwa nduna zake zonse ndiponso mʼdziko lake lonse.
v vseh znamenjih in čudežih, ki mu jih je Gospod poslal, da jih v egiptovski deželi stori faraonu in vsem njegovim služabnikom in vsej njegovi deželi
12 Ndithudi palibe mneneri wina aliyense amene anachita zinthu zazikulu ndi zoopsa zofanana ndi zomwe Mose anachita pamaso pa Aisraeli onse.
in v vsej tisti mogočni roki in vsej veliki strahoti, ki jo je Mojzes pokazal pred očmi vsega Izraela.