< Deuteronomo 34 >

1 Ndipo Mose anakwera Phiri la Nebo kuchokera ku chigwa cha Mowabu ndi kukafika pamwamba pa Phiri la Pisiga, kummawa kwa Yeriko. Kumeneko Yehova anamuonetsa dziko lonse; kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani.
Tedy vstoupil Mojžíš z rovin Moábských na horu Nébo, na vrch hory, kteráž jest proti Jerichu, a ukázal jemu Hospodin všecku zemi Galád až do Dan,
2 Dera lonse la Nafutali, dziko lonse la Efereimu ndi Manase, dziko lonse la Yuda mpaka kukafika kumadzulo kwa nyanja,
I všecku Neftalím, a zemi Efraim a Manasse, a všecku zemi Juda až k moři nejdalšímu,
3 Negevi ndi chigawo chonse kuchokera ku Chigwa cha Yeriko, Mzinda wa mitengo ya migwalangwa, mpaka ku Zowari.
Polední také stranu a roviny údolí Jericha, města palmovím osazeného, až do Segor.
4 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti, “Limenelo ndi dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo pamene ndinanena kuti, ‘Ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’ Ndakulola kuti ulione, koma sudzawoloka kuti ukalowemo.”
A řekl jemu Hospodin: Tato jest země, kterouž s přísahou zaslíbil jsem Abrahamovi, Izákovi a Jákobovi, řka: Semeni tvému dám ji. Způsobil jsem to, abys ji viděl očima svýma, však do ní nevejdeš.
5 Choncho Mose mtumiki wa Yehova anamwalira kumeneko ku Mowabu, monga momwe ananenera Yehova.
I umřel tam Mojžíš, služebník Hospodinův, v zemi Moábské, vedlé řeči Hospodinovy.
6 Yehova anamuyika mʼmanda ku Mowabu, mʼchigwa choyangʼanana ndi Beti-Peori, koma mpaka lero palibe amene amadziwa pamene pali manda ake.
A pochoval jej v Gai, v zemi Moábské naproti Betfegor, a žádný nezvěděl o jeho hrobu až do tohoto dne.
7 Mose anamwalira ali ndi zaka 120, koma maso ake ankaonabe ndipo anali amphamvu.
Byl pak Mojžíš ve stu a dvadcíti letech, když umřel, a nepošly oči jeho, aniž síla odešla od něho.
8 Aisraeli analira maliro a Mose mʼchikhwawa cha Mowabu kwa masiku makumi atatu mpaka nthawi ya kulira maliro ndi kukhuza inatha.
I plakali synové Izraelští Mojžíše na rovinách Moábských třidceti dní, a vyplněni jsou dnové pláče a kvílení nad Mojžíšem.
9 Tsono Yoswa, mwana wa Nuni anadzazidwa ndi mzimu wanzeru chifukwa nʼkuti Mose atamusanjika manja. Choncho Aisraeli anamumvera ndipo anachita zomwe Yehova analamula Mose.
Jozue pak, syn Nun, naplněn jest duchem moudrosti; nebo byl vložil Mojžíš ruce své na něj. I poslouchali ho synové Izraelští, a činili, jakož přikázal Hospodin skrze Mojžíše.
10 Kuyambira nthawi imeneyi, mu Israeli simunakhalepo mneneri wina aliyense wofanana ndi Mose, amene Yehova amayankhula naye maso ndi maso.
Ale nepovstal více prorok v Izraeli podobný Mojžíšovi, (kteréhož by tak znal Hospodin tváří v tvář, )
11 Amene anachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi ndi zozizwitsa zimene Yehova anamutuma kuti achite mu Igupto, kwa Farao ndi kwa nduna zake zonse ndiponso mʼdziko lake lonse.
Ve všech znameních a zázracích, pro něž poslal jej Hospodin, aby činil je v zemi Egyptské, před Faraonem a přede všechněmi služebníky jeho, a vší zemí jeho,
12 Ndithudi palibe mneneri wina aliyense amene anachita zinthu zazikulu ndi zoopsa zofanana ndi zomwe Mose anachita pamaso pa Aisraeli onse.
Také i ve všech skutcích ruky silné, a ve všeliké hrůzi veliké, kteréžto věci činil Mojžíš před očima všeho Izraele.

< Deuteronomo 34 >