< Deuteronomo 33 >

1 Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe.
Ятэ бинекувынтаря ку каре Мойсе, омул луй Думнезеу, а бинекувынтат пе копиий луй Исраел ынаинте де моартя луй.
2 Iye anati: “Yehova anabwera kuchokera ku Sinai ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri; anawala kuchokera pa Phiri la Parani. Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.
Ел а зис: „Домнул а венит дин Синай Ши а рэсэрит песте ей дин Сеир, А стрэлучит дин мунтеле Паран Ши а ешит дин мижлокул зечилор де мий де сфинць, Авынд ын дряпта Луй фокул леӂий.
3 Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu; opatulika ake onse ali mʼmanja mwake. Onse amagwada pansi pa mapazi anu kuchokera kwa inu amalandira malangizo,
Да, Ел юбеште попоареле; Тоць сфинций сунт ын мына Та. Ей ау стат ла пичоареле Тале, Ау примит кувинтеле Тале.
4 malamulo amene Mose anatipatsa, chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.
Мойсе не-а дат леӂя, Моштениря адунэрий луй Иаков.
5 Iye anali mfumu ya Yesuruni pamene atsogoleri a anthu anasonkhana, pamodzi ndi mafuko a Israeli.
Ел ера ымпэрат ын Исраел Кынд се адунау кэпетенииле попорулуй Ши семинцииле луй Исраел.
6 “Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe, anthu ake asachepe pa chiwerengero.”
Трэяскэ Рубен ши сэ ну моарэ Ши бэрбаций луй сэ фие мулць ла нумэр!”
7 Ndipo ponena za Yuda anati: “Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda; mubweretseni kwa anthu ake. Ndi manja ake omwe adziteteze yekha. Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”
Ятэ че а зис деспре Иуда: „Аскултэ, Доамне, гласул луй Иуда Ши аду-л ла попорул луй. Путерниче сэ-й фие мыниле Ши сэ-й фий ажутор ымпотрива врэжмашилор луй!”
8 Za fuko la Alevi anati: “Tumimu wanu ndi Urimu ndi za mtumiki wanu wokhulupirika. Munamuyesa ku Masa; munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.
Деспре Леви а зис: „Тумим ши Урим ау фост ынкрединцаць бэрбатулуй сфынт Пе каре л-ай испитит ла Маса Ши ку каре Те-ай чертат ла апеле Мериба.
9 Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti, ‘Sindilabadira za iwo.’ Sanasamale za abale ake kapena ana ake, koma anayangʼanira mawu anu ndipo anateteza pangano lanu.
Леви а зис деспре татэл сэу ши деспре мама са: ‘Ну й-ам вэзут!’ Ши деспре фраций луй: ‘Ну вэ куноск!’ Яр де копий н-а врут сэ май штие. Кэч ей пэзеск Кувынтул Тэу Ши цин легэмынтул Тэу;
10 Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu ndi malamulo anu kwa Israeli. Amafukiza lubani pamaso panu ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.
Ей ынвацэ пе Иаков порунчиле Тале Ши пе Исраел, леӂя Та; Ей пун тэмые суб нэриле Тале Ши ардере-де-тот пе алтарул Тэу.
11 Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake. Menyani adani awo mʼchiwuno kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”
Бинекувынтязэ тэрия луй, Доамне! Примеште лукраря мынилор луй! Фрынӂе шалеле потривничилор луй Ши врэжмаший луй сэ ну се май скоале!”
12 Za fuko la Benjamini anati: “Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye, pakuti amamuteteza tsiku lonse, ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”
Деспре Бениамин а зис: „Ел есте пряюбитул Домнулуй, Ел ва локуи ла адэпост лынгэ Дынсул. Домнул ыл ва окроти тотдяуна Ши се ва одихни ынтре умерий Луй.”
13 Za fuko la Yosefe anati: “Yehova adalitse dziko lake ndi mame ambiri ochokera kumwamba ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;
Деспре Иосиф а зис: „Цара луй ва прими де ла Домнул, ка семн де бинекувынтаре, Чел май бун дар ал черулуй, роуа, Челе май буне апе каре сунт жос,
14 ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;
Челе май буне роаде але соарелуй, Челе май буне роаде але фиекэрей лунь,
15 ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;
Челе май буне роаде дин мунций чей векь, Челе май буне роаде де пе дялуриле челе вешниче,
16 ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto. Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe, wapaderadera pakati pa abale ake.
Челе май буне роаде але пэмынтулуй ши дин тот че купринде ел. Бунэвоинца Челуй че С-а арэтат ын руг Сэ винэ песте капул луй Иосиф, Пе крештетул капулуй домнулуй фрацилор луй!
17 Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa; nyanga zake zili ngati za njati. Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina, ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi. Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu; nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”
Ел аре фрумусеця ынтыюлуй нэскут ал таурулуй; Коарнеле луй сунт кум сунт коарнеле биволулуй; Ку еле ва ымпунӂе пе тоате попоареле, Пынэ ла марӂиниле пэмынтулуй: Еле сунт зечиле де мий але луй Ефраим, Еле сунт мииле луй Манасе.”
18 Za fuko la Zebuloni anati: “Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka, ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.
Деспре Забулон а зис: „Букурэ-те, Забулоане, де алергэриле тале Ши ту, Исахар, де кортуриле тале!
19 Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri, kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo; kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja, chuma chobisika mu mchenga.”
Ей вор кема попоареле пе мунте; Аколо вор адуче жертфе де дрептате, Кэч вор суӂе богэция мэрий Ши комориле аскунсе ын нисип.”
20 Za fuko la Gadi anati: “Wodala amene amakulitsa malire a Gadi! Gadi amakhala kumeneko ngati mkango, kukhadzula mkono kapena mutu.
Деспре Гад а зис: „Бинекувынтат сэ фие чине лэрӂеште пе Гад! Гад се одихнеште ка ун леу ши сфышие ла браце ши капете.
21 Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri; gawo la mtsogoleri anasungira iye. Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana, anachita chifuniro cha Yehova molungama, ndiponso malamulo onena za Israeli.”
Ел а алес чя динтый парте а цэрий, Кэч аколо стэ аскунсэ моштениря леӂюиторулуй; Ел а мерс ку фрунташий попорулуй, А адус ла ындеплинире дрептатя Домнулуй Ши порунчиле Луй фацэ де Исраел.”
22 Za fuko la Dani anati: “Dani ndi mwana wamkango, amene akutuluka ku Basani.”
Деспре Дан а зис: „Дан есте ун пуй де леу Каре се арункэ дин Басан.”
23 Za fuko la Nafutali anati: “Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake; cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”
Деспре Нефтали а зис: „Нефтали, сэтул де бунэвоинцэ Ши коплешит ку бинекувынтэрь де ла Домнул, Я ын стэпынире партя де апус ши мязэзи!”
24 Za fuko la Aseri anati: “Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri; abale ake amukomere mtima, ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.
Деспре Ашер а зис: „Бинекувынтат сэ фие Ашер ынтре копиий луй Исраел! Плэкут сэ фие фрацилор луй Ши сэ-шь ынмоае пичорул ын унтделемн!
25 Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa, ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.
Зэвоареле тале сэ фие де фер ши де арамэ Ши путеря та сэ цинэ кыт зилеле тале!
26 “Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni, amene amakwera pa thambo kukuthandizani ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.
Нимень ну есте ка Думнезеул луй Исраел, Ел трече пе черурь ка сэ-ць винэ ын ажутор, Трече ку мэрецие пе норь.
27 Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu, ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha. Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu, adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’
Думнезеул чел вешник есте ун лок де адэпост Ши суб брацеле Луй челе вешниче есте ун лок де скэпаре. Ел а изгонит пе врэжмаш динаинтя та Ши а зис: ‘Нимичеште-л.’
28 Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere; zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano, kumene thambo limagwetsa mame.
Исраел есте фэрэ фрикэ ын локуинца луй, Изворул луй Иаков есте деопарте, Ынтр-о царэ плинэ де грыу ши де муст, Ши черул луй пикурэ роуа.
29 Iwe Israeli, ndiwe wodala! Wofanana nanu ndani anthu opulumutsidwa ndi Yehova? Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu ndi lupanga lanu la ulemerero. Adani ako adzakugonjera, ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”
Фериче де тине, Исраеле! Чине есте ка тине, Ун попор мынтуит де Домнул, Скутул каре ыць дэ ажутор Ши сабия каре те фаче слэвит? Врэжмаший тэй вор фаче пе приетений ынаинтя та, Ши ту вей кэлка песте ынэлцимиле лор.”

< Deuteronomo 33 >