< Deuteronomo 33 >
1 Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe.
Lesi yiso isibusiso esethulwa nguMosi umuntu kaNkulunkulu kwabako-Israyeli engakafi.
2 Iye anati: “Yehova anabwera kuchokera ku Sinai ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri; anawala kuchokera pa Phiri la Parani. Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.
Wathi: “UThixo wehla evela eSinayi njalo wakhazimula kubo ngaseSeyiri; wakhanyisa njalo kusiya eNtabeni yasePharani. Wabuya labazinkulungwane ezilitshumi zabangcwele bevelela eningizimu, emehlweni ezintaba zakhe.
3 Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu; opatulika ake onse ali mʼmanja mwake. Onse amagwada pansi pa mapazi anu kuchokera kwa inu amalandira malangizo,
Ngempela nguwe othanda abantu, bonke abangcwele basezandleni zakho. Ezinyaweni zakho bayakhothama bonke bamukele iziqondiso ezivela kuwe,
4 malamulo amene Mose anatipatsa, chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.
umthetho esawuphiwa nguMosi, inotho yebandla likaJakhobe.
5 Iye anali mfumu ya Yesuruni pamene atsogoleri a anthu anasonkhana, pamodzi ndi mafuko a Israeli.
Wayeyinkosi phezu kukaJeshuruni lapho abakhokheli babantu bebuthene, ndawonye lezizwana zako-Israyeli.
6 “Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe, anthu ake asachepe pa chiwerengero.”
Kaphile uRubheni njalo angafi, abesilisa bakhe bangaphunguki babebalutshwana.”
7 Ndipo ponena za Yuda anati: “Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda; mubweretseni kwa anthu ake. Ndi manja ake omwe adziteteze yekha. Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”
Lokhu wakutsho ngoJuda: “Zwana, wena Thixo wami, ukukhala kukaJuda; mlethe ebantwini bakhe. Ngezandla zakhe uvikela lokho akumeleyo. Yebo, msize amelane lezitha zakhe!”
8 Za fuko la Alevi anati: “Tumimu wanu ndi Urimu ndi za mtumiki wanu wokhulupirika. Munamuyesa ku Masa; munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.
NgoLevi wathi: “IThumimi kanye le-Urimi yakho ngokwayo inceku yakho ethembekileyo. Wamhlola eMasa; waba laye emachibini aseMeribha.
9 Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti, ‘Sindilabadira za iwo.’ Sanasamale za abale ake kapena ana ake, koma anayangʼanira mawu anu ndipo anateteza pangano lanu.
Wathi ngoyise lonina, ‘Angilandaba labo mina.’ Kazange akwamukele ukuthi ulabafowabo njalo kazange ananze abantwabakhe, kodwa walilondoloza ilizwi lakho wasigcina isivumelwano sakho.
10 Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu ndi malamulo anu kwa Israeli. Amafukiza lubani pamaso panu ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.
Ufundisa amanyathelo akho kuJakhobe lomthetho wakho ku-Israyeli. Unikela ngempepha phambi kwakho langeminikelo egcweleyo yokutshiswa e-alithareni.
11 Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake. Menyani adani awo mʼchiwuno kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”
Busisa bonke ubuciko bakhe, Thixo, ujabule ngomsebenzi wezandla zakhe. Babhubhise labo abamvukelayo; zitshaye izitha zakhe zingaphindi zimvukele.”
12 Za fuko la Benjamini anati: “Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye, pakuti amamuteteza tsiku lonse, ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”
NgoBhenjamini wathi: “Yekelani othandekayo kaThixo aphumule kuye evikelekile, ngoba umvikela ilanga lonke, kanti njalo lowo uThixo amthandayo uphumula emahlombe akhe.”
13 Za fuko la Yosefe anati: “Yehova adalitse dziko lake ndi mame ambiri ochokera kumwamba ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;
NgoJosefa wathi: “Sengathi uThixo angabusisa umhlaba wakhe ngamazolo aligugu avela phezulu ezulwini langamanzi ajulileyo ageleza ngaphansi;
14 ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;
langobuhle obuyingqala obulethwa lilanga kanye lokucoleka okungalethwa yinyanga;
15 ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;
lezipho zekhethelo zasezintabeni zendulo lokuthela kwezithelo zamaqaqa emi nini lanini;
16 ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto. Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe, wapaderadera pakati pa abale ake.
langezipho eziyingqala zomhlaba lokugcwala kwawo lozwelo lwakhe yena owayesesixukwini esivuthayo. Konke lokhu akube sekhanda likaJosefa, ebunzini lobuso benkosana phakathi kwabafowabo.
17 Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa; nyanga zake zili ngati za njati. Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina, ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi. Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu; nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”
Ebukhosini unjengenkunzi encane elizibulo; impondo zakhe zinjengezenyathi. Ngazo uzagweba abhuqe izizwe, aze agwebe lalezo ezisemaphethelweni omhlaba. Banjalo abezinkulungwane zamatshumi baka-Efrayimi; banjalo abezinkulungwane zikaManase.”
18 Za fuko la Zebuloni anati: “Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka, ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.
NgoZebhuluni wathi: “Jabula, Zebhuluni, ekuphumeni kwakho, lawe wena, Isakhari, emathenteni akho.
19 Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri, kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo; kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja, chuma chobisika mu mchenga.”
Bazabizela abantu ezintabeni khonale banikele imihlatshelo yabo yokulunga; bazakudla baminze ngobunengi bokusolwandle ngawo amagugu afihlakele etshebetshebeni.”
20 Za fuko la Gadi anati: “Wodala amene amakulitsa malire a Gadi! Gadi amakhala kumeneko ngati mkango, kukhadzula mkono kapena mutu.
NgoGadi wathi: “Ubusisiwe lowo oqhelisa umbuso kaGadi! UGadi uhlala khona njengesilwane, edlithiza engalweni loba ekhanda.
21 Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri; gawo la mtsogoleri anasungira iye. Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana, anachita chifuniro cha Yehova molungama, ndiponso malamulo onena za Israeli.”
Wazikhethela umhlaba omuhle okwamagama waba ngowakhe; isabelo somkhokheli sagcinelwa yena. Kwathi ekuhlanganeni kwabakhokheli babantu, wakwenza lokho okufunwa nguThixo olungileyo, kanye lokwahlulela kwakhe kwabako-Israyeli.”
22 Za fuko la Dani anati: “Dani ndi mwana wamkango, amene akutuluka ku Basani.”
NgoDani wathi: “UDani ngumdlwane wesilwane, otshakala uphuma eBhashani.”
23 Za fuko la Nafutali anati: “Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake; cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”
NgoNafithali wathi: “UNafithali uyaphuphuma ngozwelo lukaThixo njalo ugcwele izibusiso zakhe; elakhe ilifa uzazuza kusiya eningizimu ngechibini.”
24 Za fuko la Aseri anati: “Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri; abale ake amukomere mtima, ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.
Ngo-Asheri wathi: “Obusisiweyo kakhulu kulawo wonke amadodana ngu-Asheri; ababelozwelo kuye abafowabo, myekeleni ageze inyawo zakhe emafutheni.
25 Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa, ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.
Amabhawudo emasangweni akho azakuba ngawensimbi lethusi njalo amandla akho azalingana insuku zakho.
26 “Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni, amene amakwera pa thambo kukuthandizani ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.
Kakho ofana loNkulunkulu kaJeshuruni, ophezulu emazulwini ukuze akuncede kanti njalo lasemayezini ngobukhosi bakhe.
27 Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu, ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha. Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu, adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’
UNkulunkulu ongusimakade uyisiphephelo sakho, njalo ngaphansi kuzingalo ezingelakuphela. Uzazixotsha izitha phambi kwakho esithi, ‘Mbulale!’
28 Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere; zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano, kumene thambo limagwetsa mame.
Ngakho u-Israyeli uzaphila yedwa evikelekile, umthombo kaJakhobe uvikelekile, elizweni lamabele kanye lewayini elitsha, lapho amazulu phezulu akhithizela khona amazolo.
29 Iwe Israeli, ndiwe wodala! Wofanana nanu ndani anthu opulumutsidwa ndi Yehova? Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu ndi lupanga lanu la ulemerero. Adani ako adzakugonjera, ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”
Ubusisiwe wena, Oh Israyeli! Ngubani onjengawe, abantu abahlengwa nguThixo? Ulihawu lakho lomsizi wakho njalo uyinkemba yakho ekhazimulayo. Izitha zakho zizatshotshobala phambi kwakho njalo uzazinyathela phansi zonke izindawo zabo zokukhonza eziphakemeyo.”