< Deuteronomo 32 >
1 Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
Słuchajcie niebiosa, a mówić będę; niech słucha i ziemia wymowy ust moich.
2 Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
Kropić będzie jako deszcz nauka moja, popłynie jako rosa wymowa moja, jako drobny deszcz na zioła, a jako krople na trawę.
3 Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
Albowiem imienia Pańskiego będę wzywał; dajcież wielmożność Bogu naszemu,
4 Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
Skale, której sprawy są doskonałe; bo wszystkie drogi jego są sprawiedliwe. Boć jest Bóg prawdziwy, a nie masz w nim nieprawości, sprawiedliwy i prawy jest.
5 Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
Pokazili mu się, jakoby nie byli synami jego, sprosnością swoją, naród zły, a przewrotny.
6 Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
I także to oddawacie Panu, ludu głupi i szalony? izali nie on jest ojcem twoim, który cię sobie nabył? on cię uczynił, i stworzył cię.
7 Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
Wspomnij na dni dawne, uważajcie lata każdego wieku; spytaj ojca twego, a oznajmi tobie; starszych twoich, a powiedząć.
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
Gdy rozdzielił dziedzictwa Najwyższy narodom, a rozsadził syny Adamowe, położył granice narodom według liczby synów Izraelskich;
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
Albowiem działem Pańskim jest lud jego, Jakób sznurem dziedzictwa jego.
10 Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
Znalazł go w ziemi pustej, i na puszczy wielkiej i strasznej; obwodził go, uczył go, strzegł go, jako źrenicy oka swego.
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
Jako orzeł wybawia orlęta swoje, nad orlętami swojemi latając, rozszerza skrzydła swoje, bierze je i nosi je na skrzydłach swoich;
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
Tak Pan sam prowadził go, a żaden obcy bóg nie był z nim.
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
Wyniósł go na wysokie miejsca ziemi, aby używał urodzajów polnych, i uczynił, aby ssał miód z skały i oliwę z opoki twardej;
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
Aby jadł masło od krów, i mleko od owiec, z tłustością jagniąt, i barany odchowane w Basan, i kozły z tłustością ziarn pszenicznych, a pił czerwone wino wyborne.
15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
I roztył Izrael, i wierzgał (otyłeś, stłuściałeś, zgrubiałeś, i opuściłeś Boga, który cię uczynił, ) i lekce poważył Boga, opokę zbawienia swego.
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
Ku zapalczywości pobudzili go przez cudze bogi, i przez obrzydliwości rozdraźnili go.
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
Ofiarowali dyjabłom, nie Bogu, bogom, których nie znali, nowym, którzy z bliska przyszli, których się nie bali ojcowie wasi.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
Opoki, która cię spłodziła, zapomniałeś, zapomniałeś Boga, Stworzyciela twego.
19 Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
Co widząc Pan poruszył się gniewem na syny swoje, i na córki swoje.
20 Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
I rzekł: Skryję oblicze moje przed nimi, obaczę, jaki będzie koniec ich; albowiem są narodem przewrotnym, synami, w których wiary nie masz.
21 Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
Oni mię wzruszyli ku zapalczywości przez to, co nie jest Bogiem; pobudzili mię próżnościami swemi. Ja też do zazdrości pobudzę je przez te, którzy nie są ludem, przez naród głupi rozdraźnię je.
22 Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol )
Albowiem ogień rozpalił się w popędliwości mojej, i będzie gorzał aż do najgłębszego piekła, i pożre ziemię, i urodzaj jej, i wypali grunty gór. (Sheol )
23 “Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
Zgromadzę na nie złe rzeczy, strzały moje na nie wystrzelam.
24 Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
Zniszczeją od głodu, i będą strawieni gorączką, i śmiercią gorzką; zęby też bestyi poślę na nie, z jadem gadzin ziemskich.
25 Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
Zewnątrz osieroci je miecz, a w pokojach będzie strach, tak na młodzieńca, jako na pannę, na ssącego piersi, i na męża sędziwego.
26 Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
Rzekłem: Rozproszę je po kątach, i wygubię między ludźmi pamiątkę ich.
27 koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
Gdybym się na pychę nieprzyjaciół nie oglądał, by się snać nie podnieśli nieprzyjaciele ich, a nie rzekli: Ręka nasza wyniosła, a nie Pan, sprawiła to wszystko.
28 Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
Albowiem ten naród ginie przez rady swe, i nie ma rozumu.
29 Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
O by mądrymi byli! wyrozumieliby to, i oglądaliby się na ostatnie rzeczy swoje.
30 Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
Jakoby uganiał jeden z nich tysiąc, a dwaj goniliby dziesięć tysięcy! gdyby ich Bóg, opoka ich, nie zaprzedał, i Pan ich nie wydał:
31 Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
Albowiem nie jako skała nasza skała ich, co nieprzyjaciele nasi sami osądzą.
32 Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
Albowiem z macicy Sodomskiej macica ich, i z latorośli Gomorskich jagody ich, jagody jadowite, grona ich gorzkie.
33 Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
Jad smoczy wino ich, i trucizną żmij okrutną.
34 “Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
Izali to nie jest skryto u mnie; zapieczętowano w skarbie moim?
35 Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
Mojać jest pomsta i nagroda; czasu swego powinie się noga ich, ponieważ bliski jest dzień zginienia ich, a spieszą się przyszłe rzeczy do nich.
36 Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
Albowiem sądzić będzie Pan lud swój, a sług swoich użali się, gdy ujrzy, że ustała siła, a iż tak pojmany, jako zostawiony, nic nie mogą.
37 Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
I rzecze: Gdzież bogowie ich? Ona opoka, w której ufali?
38 milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
Którzy tłustość ofiar ich jadali, i pijali wino ofiar ich mokrych? Niechże wstaną, i ratują was, i niechaj będą ucieczką waszą.
39 “Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
Obaczcież teraz, żem Ja, Jam jest sam, a że nie masz bogów oprócz Mnie; Ja zabijam i ożywiam, zranię, i Ja uleczę, a nie masz kto by z ręki mojej wyrwał.
40 Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
Albowiem podniosę ku niebu rękę moję, i rzekę: Żyję Ja na wieki.
41 pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
Jeźli zaostrzę błyszczący się miecz swój, i porwie sąd ręka moja, oddam pomstę nieprzyjaciołom moim, i tym, którzy mię nienawidzą, nagrodzę.
42 Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
Opoję strzały moje krwią, a miecz mój naje się mięsa ze krwi pobitych i pojmanych, skoro zacznę mścić się nad nieprzyjacioły.
43 Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
Weselcie się narodowie z ludem jego; albowiem krwi sług swoich pomści się, i pomstę odda nieprzyjaciołom swoim, a miłościw będzie ziemi swojej, i ludowi swemu.
44 Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
Tedy przyszedł Mojżesz, i mówił wszystkie słowa pieśni tej w uszach ludu tego, on i Jozue, syn Nunów.
45 Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
A gdy dokonał Mojżesz mówić tych wszystkich słów do wszystkiego Izraela,
46 iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
Rzekł do nich: Przyłóżcie serca wasze do wszystkich słów, któremi się ja oświadczam przeciwko wam dziś, abyście je przykazywali synom waszym, żeby strzegli i pełnili wszystkie słowa zakonu tego;
47 Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
Albowiem to słowo nie ma być próżne u was, gdyż jest żywotem waszym; i w tem słowie przedłużycie dni na ziemi, do której się przeprawiacie przez Jordan, abyście ją osiedli.
48 Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
I rzekł Pan do Mojżesza tegoż dnia, mówiąc:
49 “Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
Wstąp na tę górę Abarym, na górę Nebo, która jest w ziemi Moabskiej przeciw Jerychu, a oglądaj ziemię Chananejską, którą Ja dawam synom Izraelskim w osiadłość.
50 Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
I umrzesz na tej górze, na którą wstąpisz, i będziesz przyłączony do ludu twego, jako umarł Aaron, brat twój, na górze Hor, i przyłączon jest do ludu swego;
51 Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
Dla tego żeście wystąpili przeciwko mnie w pośród synów Izraelskich przy wodach w poswarku w Kades na puszczy Syn, i żeście mię nie poświęcili w pośród synów Izraelskich.
52 Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”
Bo przed sobą oglądasz ziemię; ale tam nie wnijdziesz, do tej ziemi, którą ja daję synom Izraelskim.