< Deuteronomo 32 >
1 Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
Ņemiet vērā, debesis, jo es runāšu, un zeme lai dzird manas mutes vārdus.
2 Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
Mana mācība lai līst kā lietus, un mana valoda lai pil kā rasa, kā lietutiņš uz zaļumu, un kā lāses uz zāli
3 Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
Jo es slavēšu Tā Kunga vārdu; dodiet godu mūsu Dievam.
4 Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
Viņš ir tas akmens kalns, Viņa darbs ir pilnīgs, jo visi Viņa ceļi ir tiesa; Dievs ir patiesība un bez viltus, Viņš ir taisns un patiesīgs.
5 Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
Pret Viņu tie apgrēkojušies; tie nav Viņa bērni, bet sev par kaunu, nikna un netikla cilts.
6 Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
Vai jūs Tam Kungam tā atmaksājiet, tu ģeķīga un negudra tauta? Vai Viņš nav tavs tēvs, kam tu piederi, kas tevi radījis un sataisījis?
7 Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
Piemini tās senās dienas, ņemiet vērā tos gadus no radu radiem, vaicā savam tēvam, tas tev to stāstīs, saviem vecajiem, tie tev to sacīs.
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
Kad tas visuaugstais tautām deva viņu daļas un šķīra cilvēku bērnus, tad Viņš tautām cēla robežas pēc Israēla bērnu skaita.
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
Jo Tā Kunga daļa ir Viņa ļaudis, Jēkabs ir Viņa īpaša mantība.
10 Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
Viņš to atrada tuksneša zemē, briesmīgā kaukšanas postažā, Viņš to pasargāja, kā Savu acs raugu.
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
Kā ērglis savu perēkli vedina un lidinājās pār saviem bērniem, izplāta savus spārnus un tos uzņem un tos nes uz saviem spārniem,
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
Tā Tas Kungs vien tos vadīja, un sveša dieva nebija ar viņu.
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
Viņš to spēcīgi vadīja pār zemes augstumiem, to ēdināja ar tīruma augļiem un to zīdināja ar medu no klints un ar eļļu no cieta akmens.
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
Sviestu no govīm, un pienu no avīm, līdz ar jēru taukiem, un Basanas aunus un āžus ar taukām īkstīm, tīrus treknus kviešus un vīnogu sulu, - vīna ogu asinis tu dzēri, vīnu.
15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
Kad nu Ješuruns (t.i. Israēls) palika trekns, tad viņš spēra, - tu paliki trekns un tukls un resns, - tad viņš atstāja Dievu, savu Radītāju, un nicināja savas pestīšanas akmens kalnu.
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
Tie Viņu tirināja caur svešiem (dieviem), caur negantībām tie Viņu apkaitināja.
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
Tie upurēja jodiem, nedievam, dieviem, ko tie nepazina, jauniem, kas nesen cēlušies, ko jūsu tēvi nav bijušies.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
To akmens kalnu, kas tevi dzemdinājis, tu atstāji, un aizmirsi Dievu, kas tevi radījis.
19 Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
Kad Tas Kungs to redzēja, tad Viņš atmeta īgnumā Savus dēlus un Savas meitas,
20 Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
Un sacīja: Es paslēpšu Savu vaigu no viņiem, Es redzēšu, kā tiem pēc klāsies, jo tie ir netikla tauta, bērni bez ticības.
21 Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
Tie Mani tirinājuši caur nedievu, tie Mani kaitinājuši caur savām nelietībām; tad arī Es viņus tirināšu caur netautu, caur ģeķīgu tautu Es tos kaitināšu.
22 Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol )
Jo uguns ir iededzies no Manām dusmām un degs līdz visdziļākai ellei un aprīs zemi ar viņas augļiem un iededzinās kalnu pamatus. (Sheol )
23 “Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
Es sakrāšu pār tiem ļaunumus, Savas bultas Es uz tiem izšaušu.
24 Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
Badā tiem būs izģinst, mēris un rūgtas sērgas tos aprīs, Es sūtīšu zvēru zobus pret tiem un pīšļos līdēju čūsku dzeloņus.
25 Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
Ārā tos postīs zobens un iekšā briesmas, kā jaunekļus, tā jaunavas, zīdāmos līdz ar sirmgalvjiem.
26 Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
Es sacītu: Es tos izputināšu, Es izdeldēšu viņu piemiņu starp cilvēkiem, -
27 koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
Ja Es nebītos, ka viņu ienaidnieki Mani nesadusmo, ka viņu spaidītāji nesaprazdami nesaka: mūsu roka bija augsta, un ne Tas Kungs visu to darījis.
28 Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
Jo tie ir ļaudis bez padoma, un saprašanas tiem nav.
29 Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
Ak kaut viņi būtu gudri to saprast, un ņemtu vērā, kā tiem pēcgalā klāsies.
30 Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
Kā viens var tūkstošus vajāt un kā divi var dzenāt desmit tūkstošus? Vai ne tāpēc, ka viņu akmens kalns tos ir pārdevis, un Tas Kungs tos ir nodevis.
31 Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
Jo viņu akmens kalns nav kā mūsu akmens kalns, par to mūsu ienaidnieki paši ir spriedēji.
32 Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
Jo viņu vīna koks ir no Sodomas vīna koka un no Gomoras laukiem; viņu vīna ķekari ir žults ķekari, tiem ir rūgtas ogas.
33 Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
Viņu vīns ir pūķu siekalas un briesmīga odžu žults.
34 “Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
Vai tas nav pie Manis paslēpts, aizzieģelēts Manā padomā.
35 Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
Man pieder atriebšana un atmaksāšana, uz to laiku, kad viņu kāja slīdēs; jo viņu posta diena ir tuvu, un viņu liktenis nāk steigšus.
36 Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
Jo Tas Kungs tiesās Savus ļaudis un par Saviem kalpiem Viņš apžēlosies, kad Viņš redzēs, ka spēks ir izzudis, ka beigti mazs un liels.
37 Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
Tad Viņš sacīs: Kur ir viņu dievi, tas akmens kalns, uz ko tie cerēja?
38 milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
Viņu upura taukus tie ēda, viņu dzeramā upura vīnu tie dzēra, - lai viņi ceļas un jums palīdz, ka jums ir patvērums.
39 “Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
Raugāt nu, ka Es, Es tas esmu, un neviena nav, kā vien Es! Es nonāvēju un daru dzīvu, Es ievainoju un dziedināju, un glābēja nav no Manas rokas.
40 Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
Jo Es paceļu pret debesīm Savu roku un saku: tik tiešām, kā Es dzīvoju mūžīgi,
41 pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
Kad Es trīšu Sava zobena zibeni un Mana roka izstiepsies uz sodību, tad Es atkal atriebšos pie Saviem pretiniekiem un atmaksāšu Saviem ienaidniekiem.
42 Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
Es dzirdināšu Savas bultas ar asinīm, - un Mans zobens ēdīs miesas, - ar nokauto un gūstīto asinīm, no ienaidnieku varenām galvām.
43 Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
Gavilējiet, tautas, par Viņa ļaudīm, - jo Viņš atriebj Savu kalpu asinis un atriebjas pie Saviem pretiniekiem un apžēlojās par Savu zemi un par Saviem ļaudīm. -
44 Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
Un Mozus nāca un runāja visus šīs dziesmas vārdus to ļaužu ausīs, viņš un Jozuas, Nuna dēls.
45 Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
Kad nu Mozus bija beidzis runāt visus šos vārdus uz visu Israēli,
46 iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
Tad viņš uz tiem sacīja: ņemiet pie sirds visus šos vārdus, ko es šodien jums apliecināju; tos jums būs pavēlēt saviem bērniem, ka tie tur un dara visus šīs bauslības vārdus.
47 Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
Jo tas jums nav tukšs vārds, bet ir jūsu dzīvība, un caur šo vārdu jūs ilgi dzīvosiet tai zemē, ko iemantot jūs ejat pār Jardāni.
48 Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
Un Tas Kungs runāja uz Mozu tai pašā dienā sacīdams:
49 “Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
“Kāp uz šo Abarim kalnu, tas ir Nebus kalns, Moaba zemē pret Jēriku, un skaties Kanaāna zemi, ko Es Israēla bērniem došu iemantot.
50 Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
Un tev būs mirt uz tā kalna, kur tu uzkāpsi, un tapt piepulcinātam pie saviem ļaudīm, kā Ārons, tavs brālis, nomira uz Hora kalna un tapa piepulcināts pie saviem ļaudīm;
51 Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
Tādēļ ka jūs Israēla bērnu vidū esat noziegušies pret Mani pie strīdus ūdens Kādešā, Cin tuksnesī, tāpēc ka jūs Mani neesat svētījuši Israēla bērnu vidū.
52 Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”
Jo tu redzēsi to zemi savā priekšā, bet tur tu nenonāksi, tai zemē, ko Es došu Israēla bērniem.”