< Deuteronomo 32 >
1 Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
Give ear O heavens so let me speak and it may hear the earth [the] words of mouth my.
2 Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
May it drop like the rain teaching my may it distil like the dew speech my like showers of rain on grass and like copious showers on vegetation.
3 Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
For [the] name of Yahweh I will proclaim ascribe greatness to God our.
4 Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
The rock [is] perfect work his for all ways his [are] justice a God of faithfulness and there not [is] injustice [is] righteous and upright he.
5 Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
It has acted corruptly to him not children his blemish their a generation perverse and crooked.
6 Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
¿ To Yahweh do you repay this O people foolish and not wise ¿ not [is] he father your he created you he he made you and he established you.
7 Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
Remember [the] days of antiquity consider [the] years of a generation and a generation ask father your so he will tell you old [people] your so they may say to you.
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
When gave inheritances to [the] Most High nations when separated he [the] children of humankind he fixed boundaries of peoples to [the] number of [the] people of Israel.
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
For [the] portion of Yahweh [is] people his Jacob [is] [the] measured portion of inheritance his.
10 Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
He found it in a land of wilderness and in a wasteland of howling of a desolate place he surrounded it he took care of it he guarded it like [the] pupil of eye his.
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
Like an eagle [which] it stirs up nest its over young ones its it hovers it spreads out wings its it takes it it carries it on pinion its.
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
Yahweh alone he guided it and there not with him [was] a god of foreignness.
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
He caused to ride it on ([the] high places of *Q(k)*) [the] land and it ate fruits of [the] field and he suckled him honey from a rock and oil from flint of rock.
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
Curd of [the] herd and milk of [the] flock with fat of lambs and rams [the] sons of Bashan and goats with [the] fat of [the] kidneys of wheat and blood of grape[s] you drank wine.
15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
And he grew fat Jeshurun and he kicked you have grown fat you have become bloated you have become gorged and he abandoned God [who] he made him and he treated with contempt [the] rock of salvation his.
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
They made jealous him by strange [gods] by abominations they provoked to anger him.
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
They sacrificed to the demons [which] not [are] God gods [which] not they had known them new [gods] [which] from near they had come [which] not they had known about them ancestors your.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
[the] rock [which] he fathered You you forgot and you forgot God [who] gave birth to you.
19 Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
And he saw Yahweh and he spurned from [the] provocation of sons his and daughters his.
20 Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
And he said I will hide face my from them I will see what? [will be] end their for [are] a generation of perversiti they children [whom] not faithfulness [is] in them.
21 Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
They they have made jealous me by not a god they have provoked to anger me by vanities their and I I will make jealous them by not a people by a nation foolish I will provoke to anger them.
22 Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol )
For a fire it has been kindled by anger my and it has burned to Sheol lowest and it has consumed [the] earth and produce its and it has set ablaze [the] foundations of [the] mountains. (Sheol )
23 “Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
I will catch up on them calamities arrows my I will use up on them.
24 Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
[people] weakened of Famine and [people] consumed of plague and destruction bitter and tooth of animals I will send on them with [the] venom of [things which] crawl of [the] dust.
25 Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
From outside it will make childless a sword and [will be] from inner rooms terror both young man as well as young woman a suckling-child with a person of gray hair.
26 Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
I said I will cut in pieces them I will make cease from humankind memory their.
27 koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
If not [the] provocation of an enemy I was afraid lest they should misconstrue opponents their lest they should say hands our it was raised and not Yahweh he did all this.
28 Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
For [are] a nation perishing of counsel they and there not in them [is] understanding.
29 Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
If they were wise they will comprehend this they will understand end their.
30 Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
How? will he pursue one [person] a thousand and two [people] will they put to flight? ten thousand if in-deed rock their he had sold them and Yahweh he had delivered up them.
31 Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
For not [is] like rock our rock their and enemies our assessments.
32 Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
For [is] from [the] vine of Sodom vine their and from [the] terraced fields of Gomorrah grapes their [are] grapes of poison clusters [are] bitter of them.
33 Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
[is the] venom of Serpents wine their and [the] poison of cobras cruel.
34 “Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
¿ Not [is] that stored up with me sealed up in storehouses my.
35 Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
[belong] to Me vengeance and retribution to a time [when] it will slip foot their for [is] near [the] day of disaster their and it will make haste impending [things] to them.
36 Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
For he will judge Yahweh people his and on servants his he will have compassion if he will see that it has been used up hand and there not [is] shut up and freed.
37 Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
And he will say where? [are] gods their [the] rock [which] they sought refuge in it.
38 milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
Which [the] fat of sacrifices their they ate they drank [the] wine drink-offering their let them arise and let them help you let it be over you a shelter.
39 “Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
See - now that I I [am] he and there not [is] a god with me I I put to death and I may restore to life I wound and I I heal and there not from hand my [is] a deliverer.
40 Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
For I lift up to heaven hand my and I will say [am] living I for ever.
41 pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
If I sharpen [the] lightning of sword my so it may take hold on judgment hand my I will return vengeance to foes my and to [those who] hate me I will repay.
42 Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
I will make drunk arrows my from blood and sword my it will devour flesh from [the] blood of [the] slain and [the] captive from [the] head of [the] leaders of [the] enemy.
43 Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
Shout for joy O nations people his for [the] blood of servants his he will avenge and vengeance he will return to foes his and he will make atonement for land his people his.
44 Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
And he came Moses and he spoke all [the] words of the song this in [the] ears of the people he and Hoshea [the] son of Nun.
45 Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
And he finished Moses to speak all the words these to all Israel.
46 iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
And he said to them set heart your to all the words which I [am] warning you this day that you will command them children your to take care to do all [the] words of the law this.
47 Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
For not [is] a word [too] empty it for you for it [is] lives your and by the word this you will prolong days on the land where you [are] about to pass over the Jordan there towards to take possession of it.
48 Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses on [the] substance of the day this saying.
49 “Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
Go up to [the] mountain of the Abarim this [the] mountain of Nebo which [is] in [the] land of Moab which [is] on [the] face of Jericho and see [the] land of Canaan which I [am] about to give to [the] people of Israel to a possession.
50 Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
And die on the mountain where you [are] about to go up there towards and be gathered to people your just as he died Aaron brother your on Hor the mountain and he was gathered to people his.
51 Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
On that you acted unfaithfully against me in among [the] people of Israel at [the] waters of Meribah Kadesh [the] wilderness of Zin on that not you honored as holy me in among [the] people of Israel.
52 Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”
For from before you will see the land and there towards not you will go into the land which I [am] about to give to [the] people Israel.