< Deuteronomo 31 >
1 Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
Mojzes je odšel in te besede spregovoril vsemu Izraelu.
2 “Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
Rekel jim je: »Jaz sem ta dan star sto dvajset let. Ne morem več hoditi ven in vstopati noter. Tudi Gospod mi je rekel: ›Ti ne boš šel preko tega Jordana.‹
3 Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
Gospod, tvoj Bog, bo šel preko pred teboj in on bo izpred tebe uničil te narode in ti jih boš vzel v last in Józue, on bo šel preko pred teboj, kakor je rekel Gospod.
4 Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
Gospod jim bo storil kakor je storil Sihónu in Ogu, kraljema Amoréjcev in njuni deželi, ki ju je uničil.
5 Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
Gospod ju bo izročil pred tvoj obraz, da jima boš lahko storil glede na vse zapovedi, ki sem ti jih zapovedal.
6 Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
Bodi močan in odločnega poguma, ne boj se niti se jih ne plaši, kajti Gospod, tvoj Bog, on je ta, ki gre s teboj; ne bo te razočaral niti te ne bo zapustil.«
7 Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
Mojzes je zaklical k Józuetu in mu pred očmi vsega Izraela rekel: »Bodi močan in odločnega poguma, kajti s tem ljudstvom moraš iti v deželo, ki jo je Gospod prisegel njihovim očetom, da jim jo da; in ti jim boš povzročil, da jo podedujejo.
8 Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
Gospod, on je ta, ki gre pred teboj. S teboj bo, ne bo te razočaral niti te ne bo zapustil. Ne boj se niti ne bodi zaprepaden.«
9 Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
Mojzes je zapisal to postavo in jo izročil duhovnikom, sinovom Lévijevcev, ki so nosili skrinjo Gospodove zaveze, in vsem Izraelovim starešinam.
10 Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
Mojzes jim je zapovedal, rekoč: »Ob koncu vsakih sedmih let, na slovesno leto odpusta, na šotorski praznik,
11 pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
ko pride ves Izrael, da se prikaže pred Gospodom, tvojim Bogom, na kraju, ki ga bo on izbral, boš to postavo bral pred vsem Izraelom v njihovo uho.
12 Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
Skupaj zberi ljudstvo, može, žene, otroke in svojega tujca, ki je znotraj tvojih velikih vratih, da lahko slišijo in da se lahko naučijo in se bojijo Gospoda, svojega Boga in obeležujejo, da storijo vse besede te postave
13 Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
in da njihovi otroci, ki niso poznali ničesar, lahko slišijo in se naučijo bati se Gospoda, svojega Boga, tako dolgo kot vi živite v deželi, kamor greste prek Jordana, da jo vzamete v last.«
14 Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
Gospod je rekel Mojzesu: »Glej, približujejo se tvoji dnevi, ko moraš umreti. Pokliči Józueta in se postavita v šotorskem svetišču skupnosti, da mu lahko dam naročilo.« Mojzes in Józue sta odšla in se postavila v šotorskem svetišču skupnosti.
15 Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
Gospod se je prikazal v šotorskem svetišču, v oblačnem stebru in oblačni steber je stal nad vrati šotorskega svetišča.
16 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
Gospod je rekel Mojzesu: »Glej, zaspal boš s svojimi očeti in to ljudstvo se bo vzdignilo in se šlo vlačugat za bogovi tujcev dežele, v katero gredo, da bi bili med njimi in zapustili me bodo in prelomili mojo zavezo, ki sem jo sklenil z njimi.
17 Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
Potem bo na tisti dan moja jeza vneta zoper njih in zapustil jih bom in svoj obraz bom skril pred njimi in použiti bodo in številna zla in težave jih bodo zadele, tako da bodo na tisti dan rekli: ›Ali niso nad nas prišla ta zla, ker med nami ni našega Boga?‹
18 Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
Na tisti dan bom zagotovo skril svoj obraz zaradi vseh hudobij, ki jih bodo naredili v tem, da so se obrnili k drugim bogovom.
19 “Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
Zdaj si torej zapišite to pesem in jo učite Izraelove otroke. Položite jo v njihova usta, da bo ta pesem lahko priča zame zoper Izraelove otroke.
20 Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
Kajti ko jih bom privedel v deželo, ki sem jo prisegel njihovim očetom, kjer tečeta mleko in med in bodo jedli in se nasitili in postali debeli, potem se bodo obrnili k drugim bogovom in jim služili in me izzivali in prelomili mojo zavezo.
21 Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
Zgodilo se bo, ko jih bodo doletela mnoga zla in stiske, da bo ta pesem pričala zoper njih kakor priča, kajti ta ne bo pozabljena iz ust njihovega semena, kajti jaz poznam njihove zamisli, s katerimi hodijo naokoli, celo sedaj, preden sem jih privedel v deželo, ki sem jim jo prisegel.«
22 Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
Zato je Mojzes isti dan napisal to pesem in jo učil Izraelove otroke.
23 Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
Nunovemu sinu Józuetu je dal zadolžitev in rekel: »Bodi močan in odločnega poguma, kajti ti boš Izraelove otroke privedel v deželo, ki sem jim jo prisegel in jaz bom s teboj.«
24 Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
Pripetilo se je, ko je Mojzes končal s pisanjem besed te postave v knjigo, dokler niso bile dokončane,
25 analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
da je Mojzes zapovedal Lévijevcem, ki so nosili skrinjo Gospodove zaveze, rekoč:
26 “Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
»Vzemite to knjigo postave in jo postavite v stran skrinje zaveze Gospoda, svojega Boga, da bo ta lahko tam za pričo zoper tebe.
27 Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
Kajti poznam tvoj upor in tvoj trdi vrat. Glej, medtem ko sem z vami ta dan še živ, ste bili uporni zoper Gospoda in koliko bolj po moji smrti?
28 Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
Zberite k meni vse starešine svojih rodov in svoje častnike, da lahko te besede govorim v njihova ušesa in kličem nebo in zemljo, da pričata zoper njih.
29 Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
Kajti vem, da se boste po moji smrti popolnoma izpridili in odvrnili od poti, ki sem vam jo zapovedal in zlo vas bo zadelo v zadnjih dneh, ker boste počeli zlo v Gospodovih očeh, da ga dražite k jezi skozi dela svojih rok.«
30 Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:
Mojzes je na ušesa vse Izraelove skupnosti govoril besede te pesmi, dokler se niso končale.