< Deuteronomo 31 >

1 Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
Потом дође Мојсије и каза ове речи свему Израиљу,
2 “Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
И рече им: Мени има данас сто и двадесет година, не могу више одлазити и долазити; а и Господ ми је рекао: Нећеш прећи преко тог Јордана.
3 Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
Господ ће Бог твој ићи пред тобом, и истребиће оне народе испред тебе, и ти ћеш их наследити; Исус ће ићи пред тобом као што је казао Господ.
4 Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
И учиниће Господ с њима како је учинио са Сионом и Огом, царевима аморејским и са земљом њиховом, те их је истребио.
5 Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
Зато кад вам их преда Господ учините им сасвим онако како сам вам заповедио.
6 Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
Будите слободни и храбри, и не бојте их се и не плашите се од њих; јер Господ Бог твој иде с тобом, неће одступити од тебе, нити ће те оставити.
7 Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
Потом дозва Мојсије Исуса, и рече му пред свим Израиљем: Буди слободан и храбар; јер ћеш ући с овим народом у земљу за коју се заклео Господ оцима њиховим да ће им је дати, а ти ћеш им је разделити у наследство.
8 Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
Јер Господ који иде пред тобом биће с тобом, неће одступити од тебе, нити ће те оставити, не бој се и не плаши се.
9 Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
И Мојсије написа овај закон, и даде га свештеницима, синовима Левијевим, који ношаху ковчег завета Господњег, и свим старешинама Израиљевим.
10 Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
И заповеди им Мојсије говорећи: Сваке седме године, у одређено време године опросне, на празник сеница,
11 pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
Кад дође сав Израиљ и стане пред Господа Бога свог на месту које изабере, читај овај закон пред свим Израиљем да чују,
12 Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
Сабравши народ, људе и жене, децу и дошљаке, који буду у местима твојим, да чују и уче да се боје Господа Бога вашег, и држе и творе све речи овог закона;
13 Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
И синови њихови, који још не знају, нека чују и уче бојати се Господа Бога вашег, докле сте год живи на земљи у коју идете преко Јордана да је наследите.
14 Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
А Господ рече Мојсију: Ево, приближи се време да умреш. Дозови Исуса и станите обојица у шатору од састанка, да му дам заповести. И отиде Мојсије и Исус, и стадоше у шатору од састанка.
15 Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
И јави се Господ у шатору у ступу од облака, и стајаше ступ од облака над вратима од шатора.
16 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
И рече Господ Мојсију: Ево, ти ћеш починути с оцима својим; а народ овај уставши чиниће прељубу за туђим боговима оне земље у коју иде, и оставиће ме и поквариће завет мој, који учиних с њима.
17 Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
И онда ће се распалити мој гнев на њих, и оставићу их, и сакрићу лице своје од њих; они ће се прождрети, и снаћи ће их зла многа и невоље; и онда ће рећи: Да ме не снађоше ова зла зато што Бог мој није посред мене?
18 Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
А ја ћу онда сасвим сакрити лице своје за сва зла која учинише обративши се к другим боговима.
19 “Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
Зато сад напишите себи ову песму, и научи је синове Израиљеве; метни им је у уста да ми та песма буде сведок на синове израиљеве.
20 Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
Јер ћу га одвести у земљу за коју сам се заклео оцима његовим, у којој тече млеко и мед; онде ће јести и наситиће се и угојиће се, па ће се онда обратити к другим боговима и њима ће служити, а за мене неће марити, и поквариће завет мој.
21 Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
А кад га снађу зла многа и невоље, онда ће та песма сведочити на њих; јер се неће заборавити нити ће је нестати из уста семена њиховог. Јер знам мисли њихове и шта ће још данас чинити, пре него их уведем у земљу за коју сам се заклео.
22 Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
И написа Мојсије ту песму онај дан, и научи синове Израиљеве.
23 Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
И Господ даде заповести Исусу Навином говорећи: Буди слободан и храбар, јер ћеш ти увести синове Израиљеве у земљу за коју сам им се заклео и ја ћу бити с тобом.
24 Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
И кад написа речи овог закона у књигу, све до краја,
25 analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
Заповеди Мојсије Левитима, који ношаху ковчег завета Господњег, говорећи:
26 “Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
Узмите ову књигу закона и метните је покрај ковчега завета Господа Бога свог, да буде онде сведок на вас.
27 Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
Јер знам непокорност твоју и тврди врат твој. Ето, докле сам још жив с вама, до данас, бејасте непокорни Господу; а камоли кад ја умрем?
28 Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
Скупите мени све старешине од племена својих и управитеље своје да им кажем да чују ове речи, и да им засведочим небом и земљом.
29 Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
Јер знам да ћете се по смрти мојој покварити, и заћи с пута који вам заповедих; и зато ће вас задесити ово зло најпосле, кад станете чинити што је зло пред Господом гневећи Га делом руку својих.
30 Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:
И изговори Мојсије да чује сав збор Израиљев речи ове песме до краја.

< Deuteronomo 31 >