< Deuteronomo 31 >
1 Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
Et Moïse alla et adressa ces paroles à tous les Israélites
2 “Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
et leur dit: Je suis maintenant âgé de cent vingt ans, et je ne puis plus entrer et sortir, et l'Éternel m'a dit: Tu ne passeras pas ce Jourdain;
3 Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
l'Éternel, ton Dieu, c'est Lui qui te précédera, Lui qui exterminera devant toi ces nations pour que vous en soyez maîtres. C'est Josué qui passera à votre tête, comme l'Éternel l'a annoncé.
4 Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
Et l'Éternel les traitera, comme Il a traité Sihon et Og, rois des Amoréens, et leur pays qu'il a détruit.
5 Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
Mais quand l'Éternel vous les livrera, traitez-les en tout point selon l'ordre que je vous ai prescrit.
6 Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
Soyez courageux et fermes, n'ayez ni crainte ni peur d'eux, car c'est l'Éternel, ton Dieu, qui marchera avec toi. Il ne vous fera pas défaut, ne vous abandonnera pas.
7 Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
Et Moïse appela Josué et lui dit en présence de tout Israël: Sois courageux et ferme, car c'est toi qui entreras avec ce peuple dans le pays que l'Éternel a juré à leurs pères de leur donner, et toi qui le leur partageras.
8 Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
Et c'est l'Éternel qui te précédera; Il sera avec toi, et ne te fera pas défaut, ne t'abandonnera pas; sois sans crainte et sans alarmes.
9 Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
Et Moïse mit par écrit cette Loi et la remit aux Prêtres, fils de Lévi, porteurs de l'Arche de l'alliance de l'Éternel, et à tous les Anciens d'Israël.
10 Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
Et Moïse leur donna cette instruction: Au terme de sept ans, à l'époque de l'année du relâche, à la Fête des Loges,
11 pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
lorsque tout Israël viendra se présenter devant l'Éternel, ton Dieu, dans le lieu choisi par Lui, tu donneras lecture de cette Loi devant tout Israël, à leurs oreilles.
12 Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
Rassemble le peuple, les hommes et les femmes et les enfants et tes étrangers qui seront dans tes Portes, afin qu'ils entendent, et qu'ils apprennent à craindre l'Éternel, votre Dieu, et à s'appliquer à la pratique de tous les préceptes de cette Loi.
13 Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
Et vos fils qui ignorent, écouteront et apprendront à craindre l'Éternel, votre Dieu, aussi longtemps que vous vivrez dans le pays dont après le passage du Jourdain vous allez faire la conquête.
14 Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
Et l'Éternel dit à Moïse: Voici, le moment de ta mort approche; appelle Josué, et placez-vous dans la Tente du Rendez-vous, et je lui donnerai mes ordres. Et Moïse et Josué allèrent se placer dans la Tente du Rendez-vous.
15 Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
Alors l'Éternel apparut dans la Tente, dans une colonne de nuée; et la colonne de nuée s'arrêta à la porte de la Tente.
16 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
Et l'Éternel dit à Moïse: Voici, tu vas être couché à côté de tes pères, et ce peuple se lèvera, et se prostituera à la suite des dieux étrangers du pays dans lequel il va entrer, et il m'abandonnera, et rompra l'alliance que j'ai conclue avec lui;
17 Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
et ma colère s'allumera contre lui dans ce moment-là, et je l'abandonnerai et lui cacherai ma face, et il sera livré comme proie, et atteint par beaucoup de maux et de détresses, et il dira alors: N'est-ce pas parce que notre Dieu n'est pas au milieu de moi, que ces maux m'ont atteint?
18 Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
Et je cacherai ma face dans ce temps-là, à cause de tout le mal qu'il aura fait en se tournant vers des dieux étrangers.
19 “Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
Et maintenant écrivez ce cantique, et apprends-le aux enfants d'Israël, mets-le dans leur bouche, afin que ce cantique me serve de témoin contre les enfants d'Israël.
20 Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
Car je les introduirai dans le pays que j'ai promis par serment à leurs pères, pays découlant de lait et de miel; puis ils mangeront et se rassasieront et s'engraisseront et se tourneront vers d'autres dieux et les serviront et me mépriseront et rompront mon alliance,
21 Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
et quand alors ils seront atteints par beaucoup de maux et de détresses, que ce cantique dépose contre eux comme un témoin, car il ne doit ni être oublié, ni cesser d'être dans la bouche de leurs descendants. En effet, je connais leurs pensées qu'ils forment dès à présent, avant que je les aie introduits dans le pays que je leur ai promis par serment.
22 Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
Moïse écrivit donc ce cantique ce jour-là, et il l'apprit aux enfants d'Israël.
23 Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
Et il donna ses instructions à Josué, fils de Nun, en ces termes: Aie courage et fermeté, car c'est toi qui introduiras les enfants d'Israël dans le pays que je leur ai promis par serment, et Moi-même Je serai avec toi.
24 Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
Et lorsque Moïse eut achevé de transcrire sur un volume les paroles de cette Loi, au complet,
25 analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
Moïse fit cette injonction aux Lévites, porteurs de l'Arche de l'alliance de l'Éternel:
26 “Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
Prenez ce Volume de la Loi et le placez à côté de l'Arche de l'alliance de l'Éternel, votre Dieu, et qu'il y serve de témoin contre vous.
27 Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
Car je connais ton caractère rebelle, et la roideur de ton col; voici, pendant que je suis encore vivant à vos côtés, déjà vous vous montrez rebelles à l'Éternel: combien plus le serez-vous après ma mort!
28 Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
Assemblez auprès de moi tous les Anciens de vos Tribus, et vos Officiers, afin que je redise à leurs oreilles ces choses-là, et que je prenne à témoin contre eux les Cieux et la terre.
29 Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
Car je sais qu'après ma mort vous vous perdrez et quitterez la voie que je vous ai tracée, et que les maux fondront sur vous dans les temps à venir, parce que vous ferez ce qui est mal aux yeux de l'Éternel pour le provoquer par l'œuvre de vos mains.
30 Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:
Moïse prononça donc aux oreilles de toute l'Assemblée d'Israël les paroles de ce cantique dans leur entier: