< Deuteronomo 31 >

1 Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
Et Moïse s'en alla, et tint à tout Israël ces discours,
2 “Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
Et leur dit: Je suis aujourd'hui âgé de cent vingt ans; je ne pourrai plus aller ni venir, et l'Éternel m'a dit: Tu ne passeras point ce Jourdain.
3 Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
C'est l'Éternel ton Dieu qui passera devant toi, c'est lui qui exterminera ces nations de devant toi, et tu posséderas leur pays. C'est Josué qui doit passer devant toi, comme l'Éternel l'a dit.
4 Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
Et l'Éternel leur fera comme il a fait à Sihon et à Og, rois des Amoréens, et à leur pays, qu'il a détruits.
5 Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
Et l'Éternel vous les livrera, et vous leur ferez selon tout le commandement que je vous ai donné.
6 Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
Fortifiez-vous et prenez courage; ne craignez point, et ne soyez point effrayés devant eux; car c'est l'Éternel ton Dieu qui marche avec toi; il ne te laissera point, et ne t'abandonnera point.
7 Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
Puis Moïse appela Josué, et lui dit, devant tout Israël: Fortifie-toi et prends courage; car tu entreras avec ce peuple au pays que l'Éternel a juré à leurs pères de leur donner, et c'est toi qui les en mettras en possession.
8 Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
C'est l'Éternel qui marche devant toi; il sera lui-même avec toi; il ne te laissera point, et ne t'abandonnera point; ne crains point, et ne sois point effrayé.
9 Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
Et Moïse écrivit cette loi, et la donna aux sacrificateurs, enfants de Lévi, qui portaient l'arche de l'alliance de l'Éternel, et à tous les anciens d'Israël.
10 Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
Et Moïse leur commanda, en disant: Au bout de sept ans, à l'époque de l'année de relâche, à la fête des tabernacles,
11 pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
Quand tout Israël viendra pour comparaître devant l'Éternel ton Dieu, au lieu qu'il choisira, tu liras cette loi devant tout Israël, de manière qu'ils l'entendent.
12 Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
Rassemble le peuple, les hommes, les femmes, et les enfants, et ton étranger qui sera dans tes portes, afin qu'ils entendent, et qu'ils apprennent à craindre l'Éternel votre Dieu, et qu'ils prennent garde de faire toutes les paroles de cette loi;
13 Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
Et que leurs enfants qui n'en ont pas eu connaissance, entendent, et apprennent à craindre l'Éternel votre Dieu, tous les jours que vous serez vivants sur la terre que vous allez posséder après avoir passé le Jourdain.
14 Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
Alors l'Éternel dit à Moïse: Voici, le jour de ta mort approche; appelle Josué, et présentez-vous dans le tabernacle d'assignation, afin que je lui donne mes ordres. Moïse et Josué allèrent donc, et se présentèrent dans le tabernacle d'assignation.
15 Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
Et l'Éternel apparut, dans le tabernacle, dans une colonne de nuée; et la colonne de nuée s'arrêta à l'entrée du tabernacle.
16 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
Et l'Éternel dit à Moïse: Voici, tu vas être couché avec tes pères; et ce peuple se lèvera, et se prostituera après les dieux étrangers qui seront au milieu de lui au pays où il va. Et il m'abandonnera, et il enfreindra mon alliance, que j'ai traitée avec lui.
17 Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
En ce jour-là ma colère s'allumera contre lui; je les abandonnerai, je cacherai d'eux ma face; et il sera exposé à être dévoré, et il souffrira des maux nombreux et des angoisses. Et il dira en ce jour-là: N'est-ce pas parce que mon Dieu n'est plus au milieu de moi, que je souffre ces maux?
18 Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
Mais moi, je cacherai entièrement ma face en ce jour-là, à cause de tout le mal qu'il aura fait, parce qu'il se sera détourné vers d'autres dieux.
19 “Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
Maintenant donc, écrivez ce cantique. Enseigne-le aux enfants d'Israël; mets-le dans leur bouche, afin que ce cantique me serve de témoin contre les enfants d'Israël.
20 Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
Car j'introduirai ce peuple dans le pays au sujet duquel j'ai fait serment à ses pères, pays où coulent le lait et le miel, et il mangera, et sera rassasié et engraissé; puis il se détournera vers d'autres dieux, et il les servira; il me méprisera, et il enfreindra mon alliance.
21 Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
Et il arrivera, quand il souffrira des maux et des angoisses, que ce cantique déposera comme témoin contre lui, parce qu'il ne sera point oublié de la bouche de sa postérité. Car je connais sa nature, ce qu'il fait aujourd'hui, avant que je l'introduise au pays que j'ai juré de lui donner.
22 Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
Et Moïse écrivit ce cantique en ce jour-là, et l'enseigna aux enfants d'Israël.
23 Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
Et l'Éternel commanda à Josué, fils de Nun, et lui dit: Fortifie-toi et prends courage; car c'est toi qui introduiras les enfants d'Israël au pays que j'ai juré de leur donner, et moi, je serai avec toi.
24 Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
Et quand Moïse eut achevé d'écrire les paroles de cette loi sur un livre, jusqu'à la fin,
25 analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
Il fit ce commandement aux Lévites qui portaient l'arche de l'alliance de l'Éternel, et leur dit:
26 “Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
Prenez ce livre de la loi, et mettez-le à côté de l'arche de l'alliance de l'Éternel votre Dieu. Et il sera là comme témoin contre toi;
27 Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
Car je connais ta rébellion et ton cou roide. Voici, pendant que je suis encore aujourd'hui vivant avec vous, vous avez été rebelles contre l'Éternel; combien plus le serez-vous après ma mort!
28 Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
Faites assembler vers moi tous les anciens de vos tribus et vos officiers, et je prononcerai ces paroles à leurs oreilles, et je prendrai à témoin contre eux les cieux et la terre.
29 Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
Car je sais qu'après ma mort vous ne manquerez pas de vous corrompre et de vous détourner de la voie que je vous ai prescrite; et que le malheur vous arrivera dans les jours à venir, parce que vous ferez ce qui est mal aux yeux de l'Éternel, en l'irritant par les œuvres de vos mains.
30 Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:
Et Moïse prononça aux oreilles de toute l'assemblée d'Israël les paroles de ce cantique jusqu'à la fin.

< Deuteronomo 31 >