< Deuteronomo 31 >

1 Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
and to go: continue Moses and to speak: speak [obj] [the] word [the] these to(wards) all Israel
2 “Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
and to say to(wards) them son: aged hundred and twenty year I [the] day not be able still to/for to come out: come and to/for to come (in): come and LORD to say to(wards) me not to pass [obj] [the] Jordan [the] this
3 Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
LORD God your he/she/it to pass to/for face: before your he/she/it to destroy [obj] [the] nation [the] these from to/for face: before your and to possess: take them Joshua he/she/it to pass to/for face: before your like/as as which to speak: speak LORD
4 Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
and to make: do LORD to/for them like/as as which to make: do to/for Sihon and to/for Og king [the] Amorite and to/for land: country/planet their which to destroy [obj] them
5 Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
and to give: give them LORD to/for face: before your and to make: do to/for them like/as all [the] commandment which to command [obj] you
6 Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
to strengthen: strengthen and to strengthen not to fear and not to tremble from face of their for LORD God your he/she/it [the] to go: went with you not to slacken you and not to leave: forsake you
7 Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
and to call: call to Moses to/for Joshua and to say to(wards) him to/for eye: seeing all Israel to strengthen: strengthen and to strengthen for you(m. s.) to come (in): come with [the] people [the] this to(wards) [the] land: country/planet which to swear LORD to/for father their to/for to give: give to/for them and you(m. s.) to inherit her [obj] them
8 Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
and LORD he/she/it [the] to go: went to/for face: before your he/she/it to be with you not to slacken you and not to leave: forsake you not to fear and not to to be dismayed
9 Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
and to write Moses [obj] [the] instruction [the] this and to give: give her to(wards) [the] priest son: child Levi [the] to lift: bear [obj] ark covenant LORD and to(wards) all old: elder Israel
10 Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
and to command Moses [obj] them to/for to say from end seven year in/on/with meeting: time appointed year [the] remission in/on/with feast [the] booth
11 pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
in/on/with to come (in): come all Israel to/for to see: see with face: before LORD God your in/on/with place which to choose to call: read out [obj] [the] instruction [the] this before all Israel in/on/with ear: hearing their
12 Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
to gather [obj] [the] people [the] human and [the] woman and [the] child and sojourner your which in/on/with gate your because to hear: hear and because to learn: learn and to fear: revere [obj] LORD God your and to keep: careful to/for to make: do [obj] all word [the] instruction [the] this
13 Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
and son: child their which not to know to hear: hear and to learn: learn to/for to fear: revere [obj] LORD God your all [the] day: always which you(m. p.) alive upon [the] land: soil which you(m. p.) to pass [obj] [the] Jordan there [to] to/for to possess: take her
14 Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
and to say LORD to(wards) Moses look! to present: come day your to/for to die to call: call to [obj] Joshua and to stand in/on/with tent meeting and to command him and to go: went Moses and Joshua and to stand in/on/with tent meeting
15 Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
and to see: see LORD in/on/with tent in/on/with pillar cloud and to stand: stand pillar [the] cloud upon entrance [the] tent
16 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
and to say LORD to(wards) Moses behold you to lie down: lay down with father your and to arise: rise [the] people [the] this and to fornicate after God foreign [the] land: country/planet which he/she/it to come (in): come there [to] in/on/with entrails: among his and to leave: forsake me and to break [obj] covenant my which to cut: make(covenant) with him
17 Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
and to be incensed face: anger my in/on/with him in/on/with day [the] he/she/it and to leave: forsake them and to hide face my from them and to be to/for to eat and to find him distress: evil many and distress and to say in/on/with day [the] he/she/it not upon for nothing God my in/on/with entrails: among my to find me [the] distress: evil [the] these
18 Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
and I to hide to hide face my in/on/with day [the] he/she/it upon all [the] distress: evil which to make: do for to turn to(wards) God another
19 “Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
and now to write to/for you [obj] [the] song [the] this and to learn: teach her [obj] son: descendant/people Israel to set: put her in/on/with lip their because to be to/for me [the] song [the] this to/for witness in/on/with son: descendant/people Israel
20 Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
for to come (in): bring him to(wards) [the] land: soil which to swear to/for father his to flow: flowing milk and honey and to eat and to satisfy and to prosper and to turn to(wards) God another and to serve: minister them and to spurn me and to break [obj] covenant my
21 Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
and to be for to find [obj] him distress: evil many and distress and to answer [the] song [the] this to/for face: before his to/for witness for not to forget from lip seed: children his for to know [obj] intention his which he/she/it to make: do [the] day in/on/with before to come (in): bring him to(wards) [the] land: country/planet which to swear
22 Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
and to write Moses [obj] [the] song [the] this in/on/with day [the] he/she/it and to learn: teach her [obj] son: descendant/people Israel
23 Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
and to command [obj] Joshua son: child Nun and to say to strengthen: strengthen and to strengthen for you(m. s.) to come (in): bring [obj] son: descendant/people Israel to(wards) [the] land: country/planet which to swear to/for them and I to be with you
24 Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
and to be like/as to end: finish Moses to/for to write [obj] word [the] instruction [the] this upon scroll: book till to finish they
25 analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
and to command Moses [obj] [the] Levi to lift: bear ark covenant LORD to/for to say
26 “Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
to take: take [obj] scroll: book [the] instruction [the] this and to set: put [obj] him from side ark covenant LORD God your and to be there in/on/with you to/for witness
27 Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
for I to know [obj] rebellion your and [obj] neck your [the] severe look! in/on/with still I alive with you [the] day to rebel to be with LORD and also for after death my
28 Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
to gather to(wards) me [obj] all old: elder tribe your and official your and to speak: speak in/on/with ear: to ears their [obj] [the] word [the] these and to testify in/on/with them [obj] [the] heaven and [obj] [the] land: country/planet
29 Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
for to know after death my for to ruin to ruin [emph?] and to turn aside: turn aside from [the] way: conduct which to command [obj] you and to encounter: chanced [obj] you [the] distress: evil in/on/with end [the] day for to make: do [obj] [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD to/for to provoke him in/on/with deed: work hand your
30 Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:
and to speak: speak Moses in/on/with ear: to ears all assembly Israel [obj] word [the] song [the] this till to finish they

< Deuteronomo 31 >