< Deuteronomo 31 >

1 Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
And Moses went and spoke these words unto all Israel.
2 “Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
And he said unto them, I am a hundred and twenty years old this day; I am not able any more to go out and come in; for the Lord hath said unto me, Thou shalt not go over this Jordan.
3 Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
The Lord thy God it is who goeth over before thee; he will destroy these nations from before thee, and thou shalt dispossess them: Joshua it is who goeth over before thee, as the Lord hath spoken.
4 Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
And the Lord will do unto them as he hath done to Sichon and to 'Og, the kings of the Emorites, and unto their land, whom he hath destroyed.
5 Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
And the Lord will give them up before you; and ye shall do unto them according unto the whole of the commandment which I have commanded you.
6 Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
Be strong and of a good courage, be not afraid and be not dismayed on account of them; for the Lord thy God it is that goeth with thee; he will not let thee fail, nor forsake thee.
7 Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
And Moses called unto Joshua, and said unto him before the eyes of all Israel, Be strong and of a good courage; for thou must go with this people unto the land which the Lord hath sworn unto their fathers to give unto them; and thou shalt divide it for them as a possession.
8 Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
And the Lord it is that goeth before thee; he will be with thee, he will not let thee fail, nor will he forsake thee: fear not, nor be thou discouraged.
9 Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
And Moses wrote down this law, and delivered it unto the priests the sons of Levi, who bore the ark of the covenant of the Lord, and unto all the elders of Israel.
10 Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
And Moses commanded them, saying, At the end of [every] seven years, at the fixed time of the year of release, on the feast of tabernacles,
11 pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
When all Israel come to appear before the Lord thy God in the place which he will choose, shalt thou read this law in the presence of all Israel in their hearing.
12 Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
Assemble the people together, the men, and the women, and the children, and thy stranger that is within thy gates; in order that they may hear, and in order that they may learn how they are to fear the Lord your God, and observe to do all the words of this law;
13 Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
And that their children, who have not yet any knowledge, may hear, and learn to fear the Lord your God, all the days which ye live in the land whither ye go over the Jordan to possess it.
14 Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
And the Lord said unto Moses, Behold, thy days approach that thou must die; call Joshua, and place yourselves in the tabernacle of the congregation, that I may give him a charge: and Moses and Joshua went, and placed themselves in the tabernacle of the congregation.
15 Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
And the Lord appeared in the tabernacle in a pillar of cloud; and the pillar of cloud stood at the door of the tabernacle.
16 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
And the Lord said unto Moses, Behold, thou shalt sleep with thy fathers: and then will this people rise up, and go astray after the gods of the strangers of the land, whither they go to be in the midst of them, and they will forsake me, and break my covenant which I have made with them.
17 Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
And my anger shall be kindled against them on that day, and I will forsake them, and I will hide my face from them, and they shall be given to be devoured, and many evils and troubles shall overtake them; and they will say on that day, Is it not, because my God is not in the midst of me, that these evils have overtaken me?
18 Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
But I will assuredly hide my face on that day on account of all the evils which they have wrought, because they have turned unto other gods.
19 “Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
Now therefore write ye for yourselves this song, and teach it the children of Israel, put it in their mouth; in order that this song may become for me a witness against the children of Israel.
20 Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
For when I shall have brought them into the land which I have sworn unto their fathers, that floweth with milk and honey; and they shall have eaten and filled themselves, and grown fat: then will they turn unto other gods, and serve them, and provoke me, and break my covenant.
21 Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
And it shall come to pass, when many evils and troubles have befallen them, that this song shall testify against them as a witness; for it shall not be forgotten out of the mouth of their seed; for I know their inclination which they have shown, even this day, before I have brought them into the land which I have sworn.
22 Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
And Moses wrote down this song on the same day, and taught it the children of Israel.
23 Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
And he gave a charge unto Joshua the son of Nun, and said, Be strong and of a good courage; for thou shalt bring the children of Israel into the land which I have sworn unto them; and I will be with thee.
24 Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
And it came to pass, when Moses had made an end of writing the words of this law in a book, until they were finished,
25 analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
That Moses commanded the Levites, the bearers of the ark of the covenant of the Lord, saying,
26 “Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
Take this book of the law, and put it at the side of the ark of the covenant of the Lord your God, that it may remain there against thee for a witness.
27 Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
For I know thy rebellion, and thy stiff neck: behold, while I am yet alive with you this day, have ye been rebellious against the Lord, and how much more after my death?
28 Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
Assemble unto me all the elders of your tribes, and your officers; and I will speak in their ears these words, and I will call as witnesses against them the heavens and the earth.
29 Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
For I know that after my death ye will to a surety become corrupt, and turn aside from the way which I have commanded you; and that the evil will befall you in the latter days, when ye do the evil in the eyes of the Lord, to incense him through the work of your hands.
30 Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:
And Moses spoke in the ears of all the congregation of Israel the words of this song, until they were ended.

< Deuteronomo 31 >