< Deuteronomo 30 >
1 Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu,
“Kuzakuthi zonke lezizibusiso lalezi ziqalekiso engilimisele zona sezehlele phezu kwenu beselizigcina ezinhliziyweni zenu kuyo yonke indawo lapho uThixo uNkulunkulu wenu azalihlakazela khona phakathi kwezizwe,
2 ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino,
lalapho lina labantwabenu selibuyela kuThixo uNkulunkulu wenu limlalela ngenhliziyo yenu yonke langomphefumulo wenu wonke kusiya njengokulilaya kwami lamuhla,
3 pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani.
kulapho uThixo uNkulunkulu wenu ezabuyisela ukuphumelela kwenu abe lozwelo kini njalo alibuthe yena lapho alihlakazela khona ezizweni.
4 Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso.
Kungaze kube khatshana okunganani ngaphansi kwelanga lapho elizabe lixotshelwe khona, kusukela khonapho uThixo uNkulunkulu wenu uzalithatha libuye ekhaya.
5 Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu.
Uzalikhokhelela elizweni alinika okhokho benu, lina-ke lizalithatha libe ngelenu. Uzalenza liphumelele njalo lande ukwedlula okhokho benu.
6 Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo.
UThixo uNkulunkulu wenu uzasoka inhliziyo zenu kanye lezinhliziyo zezizukulwane zenu, ukuze limthande ngezinhliziyo zenu zonke langomoya wenu wonke, liphile.
7 Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani.
UThixo uNkulunkulu wenu uzakwehlisela zonke leziziqalekiso phezu kwezitha zenu ezilizondayo lezilihlukuluzayo.
8 Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino.
Lizaphinda njalo limlalele uThixo wenu njalo liyilandele imilayo yakhe engilinika yona lamuhla.
9 Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu,
Ngakho uThixo uNkulunkulu wenu uzaliphumelelisa kakhulu kuyo yonke imisebenzi yezandla zenu njalo alibusise ngenzalo langamazinyane ezifuyo zenu lamabele amasimu enu. UThixo uzathokoza ngani njalo aliphumelelise, njengoba wathokoza ngokhokho benu,
10 ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
nxa lizalalela uThixo uNkulunkulu wenu ligcine imilayo lezimiso lezo ezabhalwa kule iNcwadi yoMthetho liphendukele kuThixo uNkulunkulu wenu ngenhliziyo yenu yonke langomphefumulo wenu wonke.”
11 Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali.
“Engililaya ngakho lamuhla akunzima kakhulu njalo akukhatshana lani ukuba likufinyelele.
12 Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
Akukho phezulu ezulwini, okungabangela ukuthi libuze lithi: ‘Ngubani ozakwenyukela ezulwini ayesithathela ukuze akwethule kithi sibe lakho ukukulandela sikwenze na?’
13 Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
Kanti njalo akukho ngaphetsheya kolwandle, okungabangela ukuthi libuze lithi, ‘Ngubani ozachapha ulwandle ayesithathela ukuze akwethule kithi sibe lakho ukukulandela sikwenze na?’
14 Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.
Akunjalo, ilizwi liseduzane lawe kakhulu, lisemlonyeni wakho lasenhliziyweni yakho ukuze ulilalele.
15 Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko.
Khangelani, ngiletha phambi kwenu lamuhla ukuphila lokuphumelela, ukufa lokubhidlika.
16 Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.
Ngakho ngiyalilaya lamuhla ukuthi lithande uThixo uNkulunkulu wenu, lihambe ezindleleni zakhe, kanye lokugcina imilayo yakhe, izimiso lemithetho; ngalokho lizaphila lande, njalo uThixo uNkulunkulu wenu uzalibusisa elizweni eselingena kulo ukuba lilithathe libe ngelenu.
17 Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza,
Kodwa nxa inhliziyo zenu zifulathela lingabe lisalalela ngokuzithoba, njalo lingaholelwa ekuthini likhonze abanye onkulunkulu libe selibakhonza,
18 lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.
ngiyalitshela lamuhla ukuthi ngeqiniso lizabhujiswa. Aliyi kuphila isikhathi eside ezweni elizalithatha ekuchapheni kwenu iJodani.
19 Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo.
Lamuhla nginxusa izulu lomhlaba ukuba ngofakazi bami ukumelana lani ngisithi sengimise phambi kwenu ukuphila lokufa, izibusiso leziqalekiso. Khathesi zikhetheleni ukuphila, ukuze kuthi lina kanye labantwabenu libe lokuphila
20 Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
kanye lokuthi limthande uThixo uNkulunkulu wenu, lilalele ilizwi lakhe, libambelele liqine kuye, ngoba uThixo uyikuphila kwenu, njalo nguye ozalinika iminyaka eminengi lihlezi elizweni afunga ukuba uzalinika okhokho benu, u-Abhrahama, u-Isaka loJakhobe.”