< Deuteronomo 30 >

1 Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu,
Musa melanjutkan pengajarannya kepada umat Israel, “Pada masa mendatang, kalian semua dan keturunanmu akan mengalami semua berkat TUHAN Allahmu yang sudah saya sampaikan. Ketika kalian menjauh dari TUHAN, kamu sekalian akan mengalami semua kutukan yang sudah saya sampaikan juga. Namun, di negeri bangsa asing ke mana TUHAN mencerai-beraikan kalian nanti, kalian akan teringat kepada semua yang tertulis dalam kitab Taurat ini.
2 ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino,
Apabila besok kamu dan keturunanmu berbalik kepada TUHAN dengan segenap hati dan dengan segenap nafas hidupmu mematuhi perintah-Nya yang saya sampaikan hari ini,
3 pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani.
maka TUHAN Allah akan berbelas kasihan dan membebaskan kalian dari penawanan. Dia juga akan mengumpulkan kalian kembali dari negeri bangsa-bangsa lain itu.
4 Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso.
Sekalipun kalian dibuang ke ujung bumi, Dia tetap akan membawamu kembali.
5 Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu.
TUHAN Allah akan membawa kalian pulang ke negeri nenek moyang kalian, dan kalian akan kembali menduduki negeri Israel. Dia akan membuat keturunan kalian menjadi lebih makmur dan lebih banyak daripada jumlah nenek moyang kalian.
6 Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo.
TUHAN akan mengubah hatimu dan seluruh keturunanmu sehingga setiap orang sungguh-sungguh mengasihi Dia dengan segenap hati, supaya kalian dapat terus hidup di negeri ini.
7 Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani.
Lalu TUHAN akan menimpakan semua kutuk tersebut kepada musuh-musuh yang membenci dan menindas kalian.
8 Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino.
Sedangkan kalian akan berbalik kepada TUHAN, menjadi taat kembali, dan melakukan semua perintah TUHAN yang saya sampaikan hari ini.
9 Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu,
Kemudian Dia akan membuat kalian berhasil dalam semua pekerjaanmu. Dia akan memberkatimu dengan banyak anak, banyak ternak, dan hasil panen yang melimpah, karena Dia ingin membuat kalian makmur, sama seperti Dia senang memberkati nenek moyangmu.
10 ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Tetapi untuk menerima semua berkat itu, kalian harus kembali kepada-Nya dengan segenap hatimu dan sungguh-sungguh menaati semua perintah dan ketetapan-Nya yang tertulis dalam kitab Taurat ini.”
11 Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali.
“Seluruh perintah yang saya sampaikan kepada kalian hari ini tidak terlalu sulit untuk kalian lakukan dan tidak di luar pemahamanmu.
12 Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
Perintah-perintah TUHAN itu tidak disimpan di surga sehingga kalian harus bertanya, ‘Siapakah yang bisa naik ke sana untuk mengambilkannya bagi kita, supaya kita bisa mendengar dan melakukannya?’
13 Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
Perintah-perintah itu juga tidak disimpan di seberang laut sehingga kalian harus bertanya, ‘Siapakah yang bisa menyeberangi laut besar itu untuk mengambilkannya bagi kita, supaya kita bisa mendengar dan melakukannya?’
14 Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.
Sesungguhnya perintah TUHAN sangat dekat denganmu! Kalian sudah mengetahuinya dan bisa membicarakannya dengan sesamamu. Jadi, sekarang hanya tinggal melakukannya saja.
15 Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko.
“Perhatikanlah! Hari ini saya mengajukan dua pilihan kepada kamu sekalian: Hidup dengan sejahtera, atau ditimpa kesialan sampai mati.
16 Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.
Kasihilah TUHAN Allahmu, hiduplah menurut kehendak-Nya, dan taatilah perintah, ketetapan, serta peraturan-Nya. Dengan demikian, bangsa kita akan tetap hidup serta bertambah besar, dan TUHAN Allah akan memberkati kalian di negeri yang sebentar lagi kalian duduki.
17 Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza,
“Namun, jika hatimu berpaling dari TUHAN dan kamu menolak mendengarkan Dia, malahan terpikat untuk menyembah dewa-dewa,
18 lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.
saya memperingatkanmu hari ini: Kamu pasti akan binasa! Kamu tidak akan hidup lama di negeri di seberang sungai Yordan itu.
19 Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo.
“Jadi, hari ini saya sudah memberi dua pilihan kepada kamu sekalian, yakni hidup dengan berkat TUHAN, atau mengalami kutuk-Nya sampai mati. Biarlah langit dan bumi menjadi saksi atas pilihanmu! Demi kebaikanmu sendiri dan keturunanmu, pilihlah hidup!
20 Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
Kasihilah TUHAN Allah kita, taatilah Dia, dan berpeganglah erat kepada-Nya selalu. Seharusnya begitulah cara hidupmu! Jika kamu mengasihi Dia dan taat kepada-Nya, kamu dan keturunanmu akan tinggal selamanya di negeri yang TUHAN janjikan untuk diberikan kepada nenek moyang kita Abraham, Isak, dan Yakub.”

< Deuteronomo 30 >