< Deuteronomo 30 >
1 Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu,
Inton umay kadakayo amin dagitoy a banbanag, dagiti bendision ken dagiti lunod nga inkabilko iti sangoananyo, ket no lagipenyo dagitoy kadagiti amin a dadduma a nasion a nangiturongan ni Yahweh a Diosyo kadakayo,
2 ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino,
ken inton agsublikayo kenni Yahweh a Diosyo ken agtulnogkayo iti timekna, surotenyo amin dagiti ibilbilinko kadakayo ita nga aldaw— dakayo ken dagiti annakyo — iti isu-amin a pusoyo ken iti isu-amin a kararuayo,
3 pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani.
ket ibabawinto ni Yahweh ti pannakaibaludyo ken maasi isuna kadakayo; agsublinto isuna ken ummongennakayonto manipud kadagiti amin a tattao a nangiwarasan ni Yahweh a Diosyo kadakayo.
4 Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso.
No aniaman kadagiti napapanaw a tattaoyo ket addada iti kaadayoan a luglugar iti langit, ummongennakayonto ni Yahweh a Diosyo manipud sadiay, ken iyegnakayonto manipud sadiay.
5 Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu.
Ipannakayonto ni Yahweh a Diosyo iti daga a natagikua dagiti kapuonanyo, ket tagikuaenyonto manen daytoy; naimbagto isuna kadakayo ken ad-adda a paadoennakayonto ngem iti inaramidna kadagiti kapuonanyo.
6 Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo.
Kugitento ni Yahweh a Diosyo ta pusoyo ken ti puso dagiti kaputotanyo, tapno ayatenyo ni Yahweh a Diosyo iti isu-amin a pusoyo ken iti isu-amin a kararuayo, tapno agbiagkayo.
7 Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani.
Ikabilto ni Yahweh a Diosyo amin dagitoy a lunod kadagiti kabusoryo ken kadagiti manggurgura kadakayo, ken dagiti nangidaddadanes kadakayo.
8 Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino.
Agsubli ken agtulnogkayonto iti timek ni Yahweh, ken aramidenyonto amin a bilbilinna nga ibilbilinko kadakayo ita nga aldaw.
9 Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu,
Parang-ayennakayonto ni Yahweh a Diosyo iti amin nga aramidyo, iti bunga ti bagiyo, iti bunga dagiti ay-ayupyo, ken iti bunga ti dagayo, para iti panagrang-ay; ta agrag-onto manen ni Yahweh kadakayo gapu iti panagrang-ay, kas ti panagrag-ona kadagiti ammayo.
10 ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Aramidennanto daytoy no agtulnogkayo iti timek ni Yahweh a Diosyo, tapno salimetmetanyo dagiti bilbilin ken alagadenna a naisurat iti daytoy a libro ti linteg, no agsublikayo kenni Yahweh a Diosyo iti isu-amin a pusoyo ken iti isu-amin a kararuayo.
11 Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali.
Ta saan unay a narigat kadakayo daytoy a bilin nga ibilbilinko kadakayo ita nga aldaw, wenno saan nga adayo unay daytoy kadakayo a gaw-aten.
12 Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
Awan daytoy idiay langit, tapno rumbeng a kunaenyo, 'Siasino ti umuli idiay langit para kadatayo ken mangibaba daytoy kadatayo ken mangipangngeg kadatayo, tapno mabalintayo nga aramiden daytoy?'
13 Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
Wenno awan daytoy iti ballasiw ti baybay, tapno kasapulan nga ibagayo, 'Siasino ti bumallasiw iti baybay ken mangiyeg daytoy kadatayo ken mangipangngeg kadatayo, tapno mabalintayo nga aramiden daytoy?'
14 Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.
Ngem asideg unay ti sao kadakayo, iti ngiwatyo, ken iti pusoyo, tapno mabalinyo nga aramiden daytoy.
15 Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko.
Kitaem, inkabilko ita nga aldaw iti sangoananyo ti biag ken imbag, patay ken dakes.
16 Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.
No tungpalenyo dagiti bilbilin ni Yahweh a Diosyo, nga ibilbilinko kadakayo ita nga aldaw nga ayatenyo ni Yahweh a Diosyo, a magnakayo kadagiti wagasna, ken salimetmetanyo dagiti bilbilinna, dagiti alagadenna ken dagiti linlintegna, agbiag ken umadukayo, ket bendisionannakayo ni Yahweh a Diosyo iti daga a papananyo a tagikuaen.
17 Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza,
Ngem no tumallikod ti pusoyo, ken saankayo a dumngeg ngem ketdi maiyaw-awankayo ken agrukbabkayo kadagiti sabali a dios ken agdaydayawkayo kadakuada,
18 lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.
ket ibagak kadakayo ita nga aldaw nga awan dua-dua a mapukawkayo; saanyonto a mapaatiddug dagiti al-adawyo iti daga a lasatenyo ti Jordan a papananyo ken tagikuaen.
19 Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo.
Awagak ti langit ken daga tapno agsaksi maibusor kadakayo ita nga aldaw nga inkabilko iti sangoananyo ti biag ken patay, dagiti bendision ken dagiti lunod; pilienyo ngarud ti biag tapno agbiagkayo, dakayo ken dagiti kaputotanyo.
20 Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
Aramidenyo daytoy tapno ayatenyo ni Yahweh a Diosyo, tapno agtulnogkayo iti timekna, ken tapno kumpetkayo kenkuana. Ta isuna ti biagyo ken ti kaatiddug dagiti al-aldawyo; aramidenyo daytoy tapno agbiagkayo iti daga nga insapata ni Yahweh nga itedna kadagiti kapuonanyo, a ni Abraham, Isaac ken ni Jacob.”