< Deuteronomo 30 >

1 Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu,
Lors donc que seront venues sur toi toutes ces paroles, la bénédiction ou la malédiction, que j’ai exposées en ta présence, et que conduit par le repentir de ton cœur, parmi les nations, chez lesquelles t’aura dispersé le Seigneur ton Dieu,
2 ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino,
Tu seras revenu à lui avec tes enfants, et que tu obéiras à ses ordres en tout ton cœur et en toute ton âme, comme moi, je te prescris aujourd’hui,
3 pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani.
Le Seigneur ton Dieu ramènera tes captifs, il aura pitié de toi, et il te rassemblera encore du milieu de tous les peuples chez lesquels il t’avait auparavant dispersé.
4 Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso.
Quand tu aurais été dispersé jusqu’aux pôles du ciel, le Seigneur ton Dieu t’en retirera,
5 Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu.
Et il te prendra, et t’introduira dans la terre qu’ont possédée tes pères et tu en seras maître; et te bénissant il te rendra plus nombreux que furent tes pères.
6 Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo.
Le Seigneur ton Dieu circoncira ton cœur et le cœur de ta postérité, afin que tu aimes le Seigneur ton Dieu en tout ton cœur et en toute ton âme, afin que tu puisses vivre.
7 Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani.
Mais toutes ces malédictions, il les fera retourner sur tes ennemis et sur ceux qui te haïssent et te persécutent.
8 Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino.
Pour toi, tu reviendras, et tu écouteras la voix du Seigneur ton Dieu, et tu pratiqueras tous ses commandements que moi, je te prescris aujourd’hui;
9 Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu,
Et le Seigneur ton Dieu te fera abonder en toutes les œuvres de tes mains, en enfants de ton sein, en fruit de tes bestiaux, en fécondité de ta terre et en dons de toutes choses. Car le Seigneur reviendra pour se complaire en toi, en te comblant de tous les biens, comme il s’est complu dans tes pères;
10 ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Si cependant tu écoutes la voix du Seigneur ton Dieu, que tu gardes ses préceptes et ses cérémonies qui sont écrites dans cette loi, et que tu reviennes au Seigneur ton Dieu en tout ton cœur et en toute ton âme.
11 Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali.
Ce commandement que moi, je te prescris aujourd’hui, n’est pas au-dessus de toi, ni éloigné;
12 Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
Ni placé dans le ciel, en sorte que tu puisses dire: Qui de nous peut monter au ciel, pour nous l’apporter, et pour que nous l’entendions et l’accomplissions par nos œuvres?
13 Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
Il n’a pas été posé non plus au-delà de la mer, pour que tu trouves un prétexte et que tu dises: Qui de nous pourra passer la mer, et l’apporter jusqu’à nous, afin que nous puissions l’entendre, et faire ce qui est ordonné?
14 Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.
Mais ce commandement est tout près de toi, dans ta bouche et dans ton cœur, pour que tu le pratiques.
15 Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko.
Considère que j’ai proposé aujourd’hui en ta présence la vie et le bien, et d’un autre côté la mort et le mal,
16 Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.
Afin que tu aimes le Seigneur ton Dieu, que tu marches dans ses voies, que tu gardes ses commandements, ses cérémonies et ses ordonnances; et que tu vives, et qu’il te multiplie et qu’il te bénisse dans la terre dans laquelle tu entreras pour la posséder.
17 Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza,
Mais si ton cœur se détourne, si tu ne veux pas écouter, et que, séduit par l’erreur, tu adores des dieux étrangers, et tu les serves,
18 lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.
Je te prédis aujourd’hui que tu périras, et que tu demeureras peu de temps dans la terre, dans laquelle, le Jourdain passé, tu entreras pour la posséder.
19 Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo.
J’invoque à témoin aujourd’hui le ciel et la terre, que je vous ai proposé la vie et la mort, la bénédiction et la malédiction. Choisis donc la vie, afin que tu vives, et toi et ta postérité,
20 Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
Que tu aimes le Seigneur ton Dieu, que tu obéisses à sa voix et que tu t’attaches à lui (car c’est lui-même qui est ta vie et la longueur de tes jours), afin que tu habites dans la terre au sujet de laquelle le Seigneur a juré à tes pères, Abraham, Isaac et Jacob qu’il la leur donnerait.

< Deuteronomo 30 >