< Deuteronomo 29 >

1 Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.
Voici les paroles de l’alliance que Yahweh ordonna à Moïse de conclure avec les enfants d’Israël au pays de Moab, outre l’alliance qu’il avait conclue avec eux en Horeb.
2 Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo: Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto.
Moïse convoqua tout Israël et leur dit: « Vous avez vu tout ce que Yahweh a fait sous vos yeux, dans le pays d’Égypte, à Pharaon, à tous ses serviteurs et à tout son pays,
3 Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija.
les grandes épreuves que tes yeux ont vues, ces signes et ces grands prodiges.
4 Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva.
Mais Yahweh ne vous a pas donné, jusqu’à ce jour, un cœur qui comprenne, des yeux qui voient, des oreilles qui entendent.
5 Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike.
Je vous ai conduits pendant quarante ans dans le désert; vos vêtements ne se sont pas usés sur vous, et ta chaussure ne s’est pas usée à ton pied;
6 Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
vous n’avez pas mangé de pain, et vous n’avez bu ni vin ni cervoise, afin que vous puissiez connaître que je suis Yahweh, votre Dieu.
7 Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo.
Vous êtes ainsi arrivés dans ce lieu. Séhon, roi de Hésebon, et Og, roi de Basan, sont sortis à notre rencontre, pour nous combattre, et nous les avons battus.
8 Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.
Nous avons pris leur pays, et nous l’avons donné en propriété aux Rubénites, aux Gadites et à la moitié de la tribu des Manassites.
9 Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse.
Observez donc les paroles de cette alliance et mettez-les en pratique, afin de réussir dans tout ce que vous ferez.
10 Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli,
Vous vous présentez tous aujourd’hui devant Yahweh, votre Dieu, vos chefs, vos tribus, vos anciens, vos officiers, tous les hommes d’Israël,
11 pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi.
vos enfants, vos femmes et l’étranger qui est au milieu de ton camp, depuis celui qui coupe ton bois jusqu’à celui qui puise ton eau:
12 Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro,
tu te présentes pour entrer dans l’alliance de Yahweh, ton Dieu, et dans son serment, alliance que Yahweh, ton Dieu, conclut en ce jour avec toi,
13 kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
pour t’établir aujourd’hui comme son peuple et être lui-même ton Dieu, comme il te l’a dit et comme il l’a juré à tes pères, Abraham, Isaac et Jacob.
14 Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha,
Ce n’est pas avec vous seuls que je conclus cette alliance, et que je fais ce serment;
15 amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.
mais c’est avec quiconque se tient ici aujourd’hui avec nous devant Yahweh, notre Dieu, et avec quiconque n’est pas ici avec nous en ce jour.
16 Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno.
Vous savez, en effet, comment nous avons habité dans le pays d’Égypte, et comment nous avons passé au milieu des nations parmi lesquelles vous avez passé:
17 Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide.
vous avez vu leurs abominations et leur idoles, bois et pierre, argent et or, qui sont chez elles.
18 Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.
Qu’il n’y ait donc parmi vous ni homme, ni femme, ni famille, ni tribu, dont le cœur se détourne aujourd’hui de Yahweh, notre Dieu, pour aller servir les dieux de ces nations; qu’il n’y ait pas parmi vous de racine produisant du poison et de l’absinthe.
19 Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe.
Que personne, en entendant les paroles de ce serment, ne se flatte dans son cœur, en disant: « J’aurai la paix, alors même que je marcherai dans l’endurcissement de mon cœur, » de sorte que celui qui est assouvi entraîne celui qui a soif.
20 Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi.
Yahweh ne consentira pas à pardonner à cet homme; mais alors la colère et la jalousie de Yahweh s’enflammeront contre cet homme, toutes les malédictions écrites dans ce livre reposeront sur lui, et Yahweh effacera son nom de dessous les cieux.
21 Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.
Yahweh le séparera, pour le livrer au malheur, de toutes les tribus d’Israël, selon toutes les malédictions de l’alliance écrite dans ce livre de la loi.
22 Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli.
La génération à venir, vos enfants qui naîtront après vous, et l’étranger qui viendra d’une terre lointaine, — à la vue des plaies de ce pays et de ses maladies, dont Yahweh l’aura frappé,
23 Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu.
du soufre et du sel, de l’embrasement de toute cette terre, qui ne sera pas ensemencée, ne produira pas de fruits, sur laquelle ne croîtra aucune herbe, comme il arriva au bouleversement de Sodome, de Gomorrhe, d’Adama et de Seboïm, que Yahweh bouleversa dans sa colère et dans sa fureur, —
24 Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”
toutes ces nations diront: « Pourquoi Yahweh a-t-il ainsi traité ce pays? D’où vient l’ardeur de cette grande colère? »
25 Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto.
Et l’on dira: « C’est parce qu’ils ont abandonné l’alliance de Yahweh, le Dieu de leurs pères, qu’il avait conclue avec eux, lorsqu’il les fit sortir du pays d’Égypte;
26 Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse.
ils sont allés servir d’autres dieux et se prosterner devant eux, des dieux qu’ils ne connaissaient pas et que Yahweh ne leur avait pas donnés en partage.
27 Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino.
La colère de Yahweh s’est enflammée contre ce pays, et il a fait venir sur lui toutes les malédictions écrites dans ce livre.
28 Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”
Yahweh les a arrachés de leur sol avec colère, avec fureur et avec une grande indignation, et il les a jetés sur une autre terre, comme on le voit aujourd’hui. »
29 Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.
Les choses cachées sont à Yahweh, notre Dieu; les choses révélées sont pour nous et pour nos enfants, à jamais, afin que nous mettions en pratique toutes les paroles de cette loi.

< Deuteronomo 29 >