< Deuteronomo 28 >
1 Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
"Kalau kamu mentaati TUHAN Allahmu dan setia melakukan segala perintah yang saya berikan kepadamu hari ini, maka Ia akan menjadikan kamu bangsa yang paling masyhur di dunia.
2 Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
Taatilah TUHAN Allahmu, maka semua berkat ini akan diberikan kepadamu:
3 Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
Diberkatilah kota-kota dan ladang-ladangmu.
4 Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
Diberkatilah kamu, sehingga anak-anakmu banyak, hasil tanahmu berlimpah dan sapi serta kambing dombamu berjumlah besar.
5 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
Diberkatilah panen gandummu serta makanan yang kamu buat dari gandum itu.
6 Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
Diberkatilah segala usahamu.
7 Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
Jika kamu diserang, TUHAN akan mengalahkan musuhmu. Mereka akan melancarkan serangan dengan teratur, tetapi lari dengan berantakan.
8 Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
TUHAN Allahmu akan memberkati usahamu dan mengisi lumbung-lumbungmu dengan gandum. Ia akan memberkati kamu di negeri yang diberikan-Nya kepadamu.
9 Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
Kalau kamu mentaati TUHAN Allahmu dan melakukan segala perintah-Nya, kamu akan dijadikan umat-Nya sendiri, seperti yang dijanjikan-Nya.
10 Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
Maka semua bangsa di bumi akan melihat bahwa kamu bangsa pilihan TUHAN, dan mereka akan menyegani kamu.
11 Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
Kamu akan dianugerahi banyak anak. Ternakmu akan banyak dan hasil tanahmu berlimpah di negeri yang dijanjikan TUHAN kepada nenek moyangmu untuk diberikan kepadamu.
12 Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
TUHAN akan menurunkan hujan pada musimnya dari tempat penyimpanan-Nya yang berlimpah di langit. Ia akan memberkati segala usahamu, sehingga kamu dapat memberi pinjaman kepada banyak bangsa, tetapi kamu sendiri tidak usah meminjam.
13 Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
TUHAN Allahmu akan menjadikan kamu pemimpin di antara bangsa-bangsa, dan bukan pengikut. Kalau kamu setia mentaati semua perintah TUHAN yang saya berikan kepadamu hari ini, kamu akan semakin makmur dan tak pernah mundur.
14 Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
Tetapi jangan sekali-kali melalaikan perintah-perintah itu dengan cara bagaimanapun juga. Jangan juga memuja dan mengabdi kepada ilah-ilah lain."
15 Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
"Tetapi kalau kamu tidak mentaati TUHAN Allahmu, dan tidak setia melakukan segala perintah dan hukum-Nya yang saya berikan kepadamu hari ini, maka segala kutuk ini akan menimpa kamu:
16 Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
Terkutuklah kota-kota dan ladang-ladangmu.
17 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
Terkutuklah panen gandummu dan makanan yang kamu buat dari gandum itu.
18 Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
Terkutuklah kamu, sehingga hanya sedikit anakmu, hasil tanahmu, serta sapi dan kambing dombamu.
19 Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
Terkutuklah segala usahamu.
20 Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
Kalau kamu berbuat jahat dan menolak TUHAN, Ia akan mendatangkan bencana, kekacauan dan kesulitan dalam segala yang kamu lakukan, sehingga dalam waktu singkat saja kamu dibinasakan sama sekali.
21 Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
Penyakit demi penyakit akan menimpa kamu, sampai akhirnya tak seorang pun dari kamu masih tinggal di negeri yang kamu duduki itu.
22 Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
TUHAN akan menghukum kamu dengan penyakit-penyakit menular, bengkak-bengkak dan demam. Ia akan mendatangkan kekeringan dan angin yang menghanguskan sehingga panenmu rusak. Bencana-bencana itu terus menimpa kamu sampai kamu binasa.
23 Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
Hujan tak akan turun dan tanahmu menjadi keras seperti besi.
24 Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
TUHAN tak akan menurunkan hujan air, melainkan hujan debu dan pasir sampai kamu habis binasa.
25 Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
Kalau kamu tidak mentaati TUHAN Allahmu, Ia akan membuat kamu dikalahkan musuh-musuhmu. Kamu akan melancarkan serangan dengan teratur, tetapi lari dengan berantakan. Semua bangsa di bumi akan merasa ngeri melihat kemalanganmu.
26 Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
Kalau kamu mati, mayatmu menjadi makanan burung-burung dan binatang buas, dan tidak ada yang mengusir binatang-binatang itu.
27 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
TUHAN akan menghukum kamu dengan bisul-bisul seperti yang dilakukan-Nya terhadap orang Mesir. Badanmu akan penuh dengan borok dan kudis yang gatal, tetapi tak ada obatnya.
28 Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
TUHAN akan membuat kamu menjadi gila, buta dan kebingungan.
29 Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
Di siang bolong kamu meraba-raba seperti orang buta, tetapi tak dapat menemukan jalan. Segala usahamu akan gagal. Kamu terus-menerus ditindas dan dirampok, dan tidak ada yang menolong kamu.
30 Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
Kalau kamu tidak mentaati TUHAN Allahmu, hal-hal ini akan menimpa dirimu: Kamu akan bertunangan, tetapi orang lain kawin dengan tunanganmu. Kamu akan membangun rumah, tetapi tidak mendiaminya. Kamu akan menanami kebun anggur tetapi tidak makan buah-buahnya.
31 Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
Sapimu akan disembelih di depan matamu, tetapi kamu tidak makan dagingnya. Keledai-keledaimu akan digiring pergi sementara kamu memandanginya dan tak akan dikembalikan. Domba-dombamu akan diberikan kepada musuh-musuhmu dan tak ada yang menolong.
32 Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
Di depan matamu anak-anakmu akan diberikan sebagai budak kepada orang asing. Tiap hari matamu pedih mencari anak-anakmu, tetapi usahamu sia-sia, sebab mereka tidak akan kembali.
33 Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
Bangsa asing akan mengambil semua hasil tanah yang kamu peroleh dengan kerja keras, tetapi kamu sendiri tidak mendapat apa-apa selain penindasan terus-menerus dan perlakuan yang kejam.
34 Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
Kamu akan menjadi gila karena apa yang kamu alami.
35 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
TUHAN akan membuat kakimu penuh borok-borok yang sakit dan tak dapat sembuh; dari kaki sampai ujung kepala kamu akan penuh bisul-bisul.
36 Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
Kamu dan rajamu akan dibawa TUHAN ke negeri asing yang tidak kamu kenal dan tidak pula dikenal nenek moyangmu. Di situ kamu akan mengabdi kepada ilah-ilah yang dibuat dari kayu dan batu.
37 Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
Di negeri-negeri tempat kamu diceraiberaikan TUHAN, orang-orang akan ngeri melihat kamu; kamu akan diolok-olok dan ditertawakan mereka.
38 Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
Banyak benih yang kamu taburkan, tetapi sedikit hasil yang kamu peroleh, karena tanamanmu habis dimakan belalang.
39 Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
Kamu akan menanami kebun-kebun anggur dan memeliharanya, tetapi tidak memetik buah anggur atau minum air anggurnya, karena pohon-pohon anggur itu habis dimakan ulat.
40 Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
Di seluruh negerimu tumbuh pohon zaitun, tetapi buah-buahnya akan gugur, sehingga kamu tidak memperoleh minyaknya.
41 Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
Kamu akan mendapat anak-anak laki-laki dan perempuan, tetapi mereka diambil sebagai tawanan perang, sehingga kamu kehilangan mereka.
42 Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
Semua pohon dan tanamanmu akan habis dimakan serangga.
43 Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
Orang asing yang tinggal di negerimu akan semakin berkuasa, sedangkan kuasamu sendiri semakin berkurang.
44 Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
Mereka punya uang untuk dipinjamkan kepadamu, tetapi kamu tidak punya apa-apa untuk dipinjamkan kepada mereka. Dan akhirnya kamu dikuasai mereka.
45 Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
Segala malapetaka itu akan menimpa kamu dan terus mengganggu kamu sampai kamu binasa, karena kamu tidak taat kepada TUHAN Allahmu dan tidak melakukan hukum-hukum yang diberikan-Nya kepadamu.
46 Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
Bencana-bencana itu merupakan bukti dari hukuman TUHAN atas kamu dan keturunanmu untuk selama-lamanya.
47 Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
Kamu sudah diberkati TUHAN Allahmu dalam segala hal, tetapi tidak mau mengabdi kepada-Nya dengan hati yang ikhlas dan gembira.
48 chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
Karena itu kamu harus mengabdi kepada musuh-musuh yang dikirim TUHAN untuk melawan kamu. Kamu akan kelaparan, kehausan dan telanjang serta berkekurangan dalam segala hal. TUHAN akan menindas kamu dengan kejam sampai kamu binasa.
49 Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
Suatu bangsa yang tidak kamu mengerti bahasanya akan didatangkan TUHAN dari ujung bumi untuk melawan kamu. Seperti burung rajawali mereka akan menyambar kamu.
50 mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
Mereka kejam dan tidak menaruh kasihan kepada orang tua-tua maupun anak-anak.
51 Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
Mereka akan menghabiskan ternak dan hasil tanahmu, dan tidak meninggalkan bagimu gandum, air anggur, minyak zaitun atau sapi dan kambing dombamu sampai kamu mati kelaparan.
52 Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Mereka akan menyerang setiap kota di negeri yang diberikan TUHAN Allahmu kepadamu sehingga tembok-temboknya yang tinggi dan diperkuat yang kamu andalkan itu runtuh.
53 Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
Sementara musuh-musuhmu mengepung kota-kotamu, kamu akan putus asa karena kelaparan, sehingga kamu memakan anak-anakmu sendiri, anak-anak yang dianugerahkan TUHAN Allahmu kepadamu.
54 Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
Bahkan orang bangsawan yang paling luhur budinya akan putus asa selama pengepungan itu, sehingga ia makan anak-anaknya sendiri karena tidak ada makanan lain. Tak sedikit pun ia berikan kepada saudaranya atau istrinya yang dicintainya atau anak-anaknya yang masih hidup.
55 ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
56 Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
Bahkan wanita bangsawan yang paling luhur budinya dan yang sangat kaya sehingga tak pernah harus berjalan kaki, akan berbuat begitu juga. Pada waktu musuh mengepung kota, wanita itu akan putus asa karena kelaparan, sehingga ia dengan sembunyi-sembunyi makan anaknya yang baru lahir dan ari-arinya. Tidak sedikit pun ia berikan kepada suaminya yang dicintainya atau kepada anak-anaknya.
57 zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
58 Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
Kalau kamu tidak setia mentaati semua hukum TUHAN Allahmu yang tertulis dalam buku ini dan tidak menghormati TUHAN Allahmu yang agung dan menakjubkan,
59 Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
TUHAN akan mendatangkan atas kamu dan keturunanmu penyakit-penyakit yang tak dapat disembuhkan dan wabah-wabah yang tak dapat dihentikan.
60 Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
Penyakit-penyakit mengerikan yang kamu saksikan di Mesir akan menimpa kamu, dan kamu tak dapat sembuh.
61 Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
TUHAN juga akan mendatangkan macam-macam penyakit dan wabah yang tidak disebut dalam buku ini, buku Hukum TUHAN. Lalu kamu akan dibinasakan.
62 Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
Walaupun jumlahmu sudah sebanyak bintang di langit, hanya sedikit saja di antara kamu yang masih hidup, karena kamu tidak taat kepada TUHAN Allahmu.
63 Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
Seperti TUHAN senang memberi kemakmuran kepadamu dan menambah jumlahmu, Ia akan senang membinasakan dan memusnahkan kamu. Kamu akan dicabut dari negeri yang tak lama lagi kamu duduki.
64 Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
TUHAN akan menceraiberaikan kamu di antara bangsa-bangsa di seluruh muka bumi. Di sana kamu akan menyembah ilah-ilah yang dibuat dari kayu dan batu, ilah-ilah yang tidak kamu kenal dan tidak pula dikenal nenek moyangmu.
65 Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
Di antara bangsa-bangsa itu kamu tak akan menemukan ketentraman, dan tak ada tempat yang dapat kamu sebut milikmu; TUHAN akan membuat kamu sangat cemas dan putus asa tanpa harapan.
66 Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
Hidupmu akan selalu terancam bahaya. Siang malam kamu merasa ngeri dan takut mati.
67 Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
Waktu melihat apa saja jantungmu berdebar-debar karena takut. Pagi-pagi kamu mengharapkan malam, dan malam-malam kamu mengharapkan pagi.
68 Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.
TUHAN akan mengirim kamu kembali ke Mesir dengan kapal, biarpun Ia telah berkata bahwa kamu tak akan kembali lagi ke sana. Di sana kamu akan berusaha menjual dirimu sebagai budak kepada musuhmu, tetapi tak seorang pun mau membeli kamu."