< Deuteronomo 28 >

1 Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
No dumngegkayo a naimbag iti timek ni Yahweh a Diosyo tapno masalimetmetanyo dagiti amin a bilbilinna nga ibilbilinko kadakayo ita nga aldaw, aramidennakayonto a napatpateg ni Yahweh a Diosyo ngem dagiti amin a nasion iti daga.
2 Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
Umayto kadakayo dagitoy a bendision ket makamakamdakayo, no dumngegkayo iti timek ni Yahweh a Diosyo.
3 Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
Mabendisionankayonto idiay siudad, ken mabendisionankayonto idiay taltalon.
4 Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
Mabendisionanto ti bunga ti bagiyo, ken ti bunga ti dagayo, ken ti bunga dagiti ayupyo, ti panagadu dagiti bakayo, ken dagiti urbon ti arbanyo.
5 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
Mabendisionanto ti basket ken ti pagmasmasaanyo.
6 Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
Mabendisionankayonto inton umunegkayo, ken mabendisionankayonto inton rummuarkayo.
7 Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
Kabilento ni Yahweh dagiti kabusoryo a tumakder a maibusor kadakayo iti sangoananyo; rumuarda a bumusor kadakayo iti maysa a dalan, ngem agtataraydanto ti sangoananyo kadagiti pito a dalan.
8 Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
Bilinento ni Yahweh ti bendision a mapan kadakayo kadagiti kamaligyo ken amin nga aramiden ti imayo; bendisionannakayonto idiay daga nga it-tedna kadakayo.
9 Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
Bangonennakayonto ni Yahweh a kas tattao a naisina a para kenkuana, kas insapatana kadakayo, no salimetmetanyo dagiti bilin ni Yahweh a Diosyo, ken magnakayo kadagiti dalanna.
10 Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
Makitanto iti amin a tattao iti daga a naawagankayo babaen iti nagan ni Yahweh, ket agbutengdanto kadakayo.
11 Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
Parang-ayennakayonto unay ni Yahweh iti bunga ti bagiyo, iti bunga dagiti ayupyo, ti bunga ti dagayo, iti daga nga insapatana kadagiti ammayo nga itedna kadakayo.
12 Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
Lukatanto ni Yahweh kadakayo dagiti kamaligna kadagiti langit a mangted ti tudo iti dagayo iti umno a tiempo, ken mangbendision kadagiti amin nga aramid ti imayo; agpautangkayonto kadagiti adu a nasion, ngem saankayonto a bumulod.
13 Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
Pagbalinennakayonto ni Yahweh a pangulo kadagiti pagilian ken saan a paspasurot; narang-aykayonto latta, ken saankayonto a pulos nga agkasapulan, no dumngegkayo kadagiti bilbilin ni Yahweh a Diosyo nga ibilbilinko kadakayo ita nga aldaw, tapno tungpalen ken aramidenyo dagitoy,
14 Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
ken no saanyo a labsingen iti aniaman a sasao nga ibilbilinko kadakayo ita nga aldaw, iti makannawan wenno ti makannigid, a mapankayo kadagiti sabali a dios tapno agserbi kadagitoy.
15 Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
Ngem no saankayo a dumngeg iti timek ni Yahweh a Diosyo, tapno salimetmetanyo dagiti amin a bilbilinna ken dagiti alagadenna nga ibilbilinko kadakayo ita nga aldaw, umayto ngarud kadakayo amin dagitoy a lunod ket makamakamnakayo.
16 Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
Mailunodkayonto iti siudad ken mailunodkayonto iti taltalon.
17 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
Mailunodto ti basket ken ti pagmasaanyo.
18 Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
Mailunodto ti bunga ti bagiyo, ti bunga ti dagayo, ti panagado ti ayupyo, ken dagiti urbon ti arbanyo.
19 Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
Mailunodkayonto inton umunegkayo, ken mailunodkayonto inton rummuarkayo.
20 Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
Mangibaonto ni Yahweh kadakayo kadagiti lunod, pannakatikaw ken babalaw iti amin a banag nga aramiden iti imayo, aginggana a madadaelkayo, ken aginggana a mapukawkayo a dagus gapu kadagiti nadangkes a tignayyo nga isu ti gapu a pinanawandak.
21 Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
Ikapetto kadakayo ni Yahweh ti didigra aginggana a madadaelnakayo manipud iti daga a serrekenyo tapno tagikuaen.
22 Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
Darupennakayonto ni Yahweh babaen kadagiti makaakar a sakit, babaen iti gurigor, iti ilulumteg, ken iti tikag ken napalalo a pudot, ken kadagiti makalanet nga angin ken linna-aw. Kamatennakayonto dagitoy aginggana a mapukawkayo.
23 Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
Agbalinto a kas iti bronse dagiti tangatangyo nga adda iti ngatoen ti uloyo, ket agbalinto a kas iti landok iti daga nga adda iti babaenyo.
24 Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
Pagbalinento ni Yahweh a tapok ken dapo ti dagayo imbes a mangparnuay isuna iti tudo; manipud kadagiti langit bumabanto dagitoy kadakayo, aginggana a madadaelkayo.
25 Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
Ipalubosto ni Yahweh a makabilkayo iti sangoanan dagiti kabusoryo; rummuarkayo iti maysa a dalan a bumusor kadakuada, ket aglibaskayonto iti pito a dalan iti sangoananda. Maisubli-sublikayonto kadagiti amin a pagarian ti daga.
26 Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
Ti bangkayyo ket agbalinto a taraon dagiti amin a billit dagiti langit ken kadagiti ayup iti daga; awanto ti mangbugaw kadagitoy.
27 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
Darupennakayonto ni Yahweh babaen kadagiti letteg iti Egipto ken babaen kadagiti gaddil, kurad, ken gagatel, ket saankayonto a maagasan.
28 Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
Darupennakayonto ni Yahweh babaen iti panagmauyong, babaen iti pannakabulsek, ken babaen iti pannakatikaw ti panunot.
29 Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
Agar-arikapkayonto iti katengngaan ti aldaw a kasla panagar-arikap ti bulsek iti kasipngetan, ken saankayonto a rumang-ay kadagiti wagasyo; kankanyonkayonto a maidadanes ken matakawan, ket awanto ti mangispal kadakayo.
30 Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
Makitulagkayonto iti maysa a babai, ngem gammatanto ti sabali a lalaki isuna ket makikaiddanto kenkuana. Mangibangonkayonto iti balay ngem saankayo nga agnaed iti daytoy, agmulakayonto iti ubas ngem saanyo a pagnumaran ti bungana.
31 Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
Mapapatayto dagiti bakayo iti imatangyo ngem saanyonto a kanen ti karnena. Pilitendanto nga alaen ti asnoyo iti imatangyo, ngem saanto a maisubli kadakayo. Maitedto dagiti karneroyo kadagiti kabusoryo, ket awanto ti umay mangispal kadakayo.
32 Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
Maitedto dagiti annakyo a lallaki ken annakyo a babbai kadagiti sabali a tattao; sapsapulento ida dagiti matayo iti agmalmalem, ngem maupaykayonto iti iliwyo kadakuada. Awanto ti pigsa ti imayo.
33 Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
Ti apit ti dagayo ken ti amin a nagbannoganyo— kanento ti nasion a saanyo nga am-ammo; kankanayonkayonto a maidaddadanes ken madadael,
34 Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
tapno agbalinkayonto nga agmauyong babaen kadagiti makitkitayo a mapaspasamak.
35 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
Darupennakayonto ni Yahweh kadagiti tumengyo ken kadagiti luppoyo babaen iti nakaro a panagletteg a saanyonto a maagasan, manipud iti dapanyo aginggana iti tuktok ti uloyo.
36 Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
Ipannakayonto ni Yahweh ken ti ari nga isaadyonto a mangaywan kadakayo iti nasion a saanyo nga am-ammo. uray dakayo wenno dagiti kapuonanyo, agdayawkayonto sadiay kadagiti sabali a dios a kayo ken bato.
37 Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
Agbalinkayonto a paggapuan iti pagbutbutngan, maysa a proberbio, ken pagkakatawaan kadagiti amin a tattao a pangipanan kadakayo ni Yahweh.
38 Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
Mangipankayonto iti adu a bukel idiay taltalon, ngem bassitto ti maurnongyo a bukel iti daytoy, gapu ta kanento dagiti dudon daytoy.
39 Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
Mulaanyonto dagiti kaubasan ken taripatoenyo dagitoy, ngem saankayonto nga uminom iti aniaman kadagiti arak, wenno uray agapit kadagiti ubas, gapu ta kanen dagiti igges dagitoy.
40 Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
Maddaankayonto kadagiti kayo nga olibo iti amin a masakupanyo, ngem saanyonto a maiyaprus ti lana iti bagiyo, gapu ta dagiti kayoyo nga olibo ket agregregto dagiti bungada.
41 Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
Maadddaankayonto kadagiti annak a lallaki ken annak a babbai, ngem saandanto nga agtalinaed a kukuayo, gapu ta maitalawdanto a kas balud ti gubat.
42 Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
Amin a kayoyo ken ti bunga ti dagayo—tagikuaento dagiti dudon dagitoy.
43 Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
Rumang-ayto a rumang-ay dagiti ganggannaet nga adda kadakayo; pumanglawto a pumanglaw ti kasasaadyo.
44 Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
Pautangadnakayonto, ngem saanyonto a mapautangan isuda; iturayandakayonto ket dakayonto ti agpaituray kadakuada.
45 Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
Amin dagitoy a lunod ket umayto kadakayo ket kamatendakayonto ken makamakamdakayo aginggana a madadaelkayo. Mapasamakto daytoy gapu ta saankayo a dimngeg iti timek ni Yahweh a Diosyo, tapno salimetmetanyo dagiti bilbilinna ken dagiti alagadenna nga imbilinna kadakayo.
46 Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
Addanto kadakayo dagitoy a lunod a kas pagilasinan ken pammaneknek, ken addanto kadagiti kaputotanyo iti agnanayon.
47 Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
Gapu ta saanyo a dinayaw ni Yahweh a Diosyo nga addaan kinarag-o ken kinaragsak iti puso idi narang-aykayo,
48 chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
pagserbianyonto ngarud dagiti kabusor nga ibaonto ni Yahweh a maibusor kadakayo; pagserbianyonto ida babaen iti panagbisin, iti pannakawaw, iti kinalamulamo ken iti kinakurapay. Mangikabilto isuna iti sangol a landok iti tengngedyo aginggana a madadaelnakayo.
49 Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
Iyegto ni Yahweh ti maysa a nasion manipud iti adayo a maibusor kadakayo, manipud kadagiti pungto iti daga, a kasla maysa a tumatayab nga agila nga agturong iti biktimana, maysa a nasion a saanyo a maawatan ti pagsasaona;
50 mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
maysa a nasion nga addaan kadagiti narungsot a langa nga awan iti panagraemna kadagiti nataengan wenno naimbag a nakem para kadagiti ubbing.
51 Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
Kanendanto dagiti urbon dagiti ayuymo ken ti bunga ti dagayo aginggana a madadaelkayo. Awanto ti ibatida kadakayo a bukel, baro nga arak wenno lana, awan ti urbon dagiti bakayo wenno arbanyo, aginggana a mapukawdakayo.
52 Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Lakubendakayonto iti amin a ruangan ti siudadyo, aginggana a marba dagiti nangato ken natibker a paderyo iti sadinoman iti dagayo, dagiti pader a pagtaltalkanyo. Lakubendakayonto kadagiti amin a ruangan ti siudadyo iti entero a daga nga inted kadakayo ni Yahweh a Diosyo.
53 Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
Kanenyonto ti bunga ti bukodyo a bagi, ti lasag dagiti annakyo a lallaki ken babbai, nga inted kadakayo ni Yahweh a Diosyo, iti pannakalakub ken iti pannakaparigat nga ikabilto kadakayo dagiti kabusoryo.
54 Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
Ti natakneng ken nakapuy la unay a lalaki kadakayo—umapalto isuna iti kabsatna a lalaki ken iti ay-ayatenna nga asawa, ken aniaman kadagiti annakna a nabati.
55 ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
Isu a saanto isuna a mangted iti siasinoman kadakuada ti lasag iti bukodna nga annak a kanennanto, gapu ta awanton ti nabati para kenkuana iti pananglakub ken kinarigat nga ipaayto dagiti kabusoryo kadakayo iti amin a ruangan ti siudadyo.
56 Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
Ti natakneng ken nakapuy unay a babai kadakayo, a saanna a maitured nga ibaddek ti dapanna iti daga gapu iti kinakapuy ken kinatakneng—umapalto isuna iti ay-ayatenna nga asawa, iti anakna a lalaki, ken iti anakna a babai,
57 zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
ken iti kaipaspasngay a rimmuar manipud iti baet dagiti luppona, ken kadagiti ubbing nga ipasngayna. Kanennanto ida iti nalimed gapu iti kinakurang iti aniaman a banag, bayat iti pannakalukob ken kinarigat nga ipaayto dagiti kabusoryo kadagiti ruangan ti siudadyo.
58 Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
No saanyo a salimetmetan amin dagitoy a sasao iti daytoy a linteg a naisurat iti daytoy a libro, tapno dayawen daytoy a naglorian ken nakabutbuteng a nagan, ni Yahweh a Diosyo,
59 Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
Aramidento ngarud ni Yahweh a nakabutbuteng dagiti didigrayo ken dagiti kaputotanyo; addanto dagiti napalalo a didigra a napaut, ken nakaro a sakit a napaut.
60 Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
Iyegnanto manen kadakayo dagiti amin a sakit ti Egipto a pagbutbutnganyo; kumpetdanto kadakayo.
61 Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
Kasta met a tunggal sakit ken didigra a saan a naisurat iti libro iti daytoy a linteg, dagitoy ti iyegto pay ni Yahweh kadakayo aginggana a madadaelkayo.
62 Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
Bassitto laeng ti mabati kadakayo, uray no kaslakayo la kaadu dagiti bituen kadagiti langit, gapu ta saankayo a dimngeg iti timek ni Yahweh a Diosyo.
63 Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
Kas iti naminsan a nagrag-o ni Yahweh kadakayo babaen iti panangaramidna iti nasayaat kadakayo, ken iti panangpaaduna kadakayo, isu nga agragsakto isuna kadakayo iti panangpukawna ken iti panangdadaelna kadakayo. Maparutkayonto iti daga a serrekenyo tapno tagikua-en.
64 Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
Iwarasnakayonto ni Yahweh kadagiti amin a tattao iti amin a suli ditoy lubong; agdayawkayonto sadiay iti sabali a dios a saanyo nga am-ammo, dakayo wenno dagiti kapuonanyo, dagiti dios a kayo ken bato.
65 Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
Saankayonto a makasarak iti nam-ay kadagitoy a nasion, ken awanto ti panaginana kadagiti dapan dagiti sakayo; ngem ketdi, pagdanagennakayonto ni Yahweh sadiay, pagkapsutenna dagita matayo, ken pagladingitenna dagita kararuayo.
66 Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
Nakabitinto ti biagyo iti panagdua-dua iti sangoananyo; mabutbutengkayonto iti tunggal rabii ken aldaw ket awanankayonto iti talged iti amin a biagyo.
67 Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
Ibagayonto iti bigat, 'Rabii koman!' ken iti rabii ibagayo, 'Bigat koman!' gapu iti buteng iti pusoyo ken kadagiti banbanag a makitkitanto dagiti matayo.
68 Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.
Ipannakayonto manen ni Yahweh idiay Egipto babaen kadagiti bangka, iti dalan nga imbagak kadakayo, 'Saanyonto a makita manen ti Egipto ni kaanoman.' Ilakoyonto ti bagiyo sadiay kadagiti kabusoryo kas tagabu a lalaki ken babai, ngem awanto ti gumatang kadakayo.”

< Deuteronomo 28 >