< Deuteronomo 28 >
1 Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
Or il arrivera que si tu obéis exactement à la voix de l'Eternel ton Dieu, et que tu prennes garde de faire tous ses commandements que je te prescris aujourd'hui, l'Eternel ton Dieu te rendra haut élevé par dessus toutes les nations de la terre.
2 Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
Et toutes ces bénédictions ici viendront sur toi, et t'atteindront, quand tu obéiras à la voix de l'Eternel ton Dieu.
3 Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
Tu seras béni dans la ville, tu seras aussi béni aux champs.
4 Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
Le fruit de ton ventre sera béni, et le fruit de ta terre, et le fruit de ton bétail; les portées de tes vaches, et les brebis de ton troupeau.
5 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
Ta corbeille sera bénie; et ta maie aussi.
6 Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
Tu seras béni en ton entrée, et tu seras aussi béni en ta sortie.
7 Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
L'Eternel fera que tes ennemis qui s'élèveront contre toi, seront battus devant toi; ils sortiront contre toi par un chemin, et ils s'enfuiront devant toi par sept chemins.
8 Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
L'Eternel commandera à la bénédiction qu'elle soit avec toi, dans tes greniers, et dans tout ce à quoi tu mettras ta main; et il te bénira au pays que l'Eternel ton Dieu te donne.
9 Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
L'Eternel ton Dieu t'établira pour lui être un peuple saint, selon qu'il te l'a juré, quand tu garderas les commandements de l'Eternel ton Dieu, et que tu marcheras dans ses voies.
10 Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
Et tous les peuples de la terre verront que le Nom de l'Eternel est réclamé sur toi, et ils auront peur de toi.
11 Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
Et l'Eternel ton Dieu te fera abonder en biens, [multipliant] le fruit de ton ventre, et le fruit de tes bêtes, et le fruit de ta terre, sur la terre que l'Eternel a juré à tes pères de te donner.
12 Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
L'Eternel t'ouvrira son bon trésor, [savoir] les cieux, pour donner la pluie, telle qu'il faut à ta terre en sa saison, et pour bénir tout le travail de tes mains; et tu prêteras à beaucoup de nations, et tu n'emprunteras point.
13 Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
L'Eternel te mettra à la tête, et non à la queue, et tu seras seulement au dessus, et non point au dessous; quand tu obéiras aux commandements de l'Eternel ton Dieu que je te prescris aujourd'hui, afin que tu prennes garde de les faire;
14 Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
Et que tu ne te détournes ni à droite ni à gauche d'aucune des paroles que je te commande aujourd'hui, pour marcher après d'autres dieux, [et] pour les servir.
15 Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
Mais si tu n'obéis point à la voix de l'Eternel ton Dieu, pour prendre garde de faire tous ses commandements et ses statuts que je te prescris aujourd'hui, il arrivera que toutes ces malédictions-ci viendront sur toi, et t'atteindront.
16 Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
Tu seras maudit dans la ville, et tu seras aussi maudit aux champs.
17 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
Ta corbeille sera maudite, et ta maie aussi.
18 Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
Le fruit de ton ventre sera maudit, et le fruit de ta terre; les portées de tes vaches, et les brebis de ton troupeau.
19 Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
Tu seras maudit en ton entrée, tu seras aussi maudit en ta sortie.
20 Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
L'Eternel enverra sur toi la malédiction, l'effroi, et la dissipation dans tout ce à quoi tu mettras la main [et] que tu feras, jusqu'à ce que tu sois détruit, et que tu périsses [promptement], à cause de la méchanceté des actions par lesquelles tu m'auras abandonné.
21 Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
L'Eternel fera que la mortalité s'attachera à toi, jusqu'à ce qu'il t'aura consumé de dessus la terre en laquelle tu vas pour la posséder.
22 Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
L'Eternel te frappera de langueur, d'ardeur, de fièvre, de chaleur brûlante, d'épée, de sécheresse et de nielle, qui te poursuivront jusqu'à ce que tu périsses.
23 Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
Et tes cieux, qui [seront] sur ta tête, seront d'airain; et la terre qui [sera] sous toi, sera de fer.
24 Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
L'Eternel te donnera au lieu de la pluie telle qu'il faut à ta terre, une poussière menue, et une poudre [qui] descendra sur toi des cieux, jusqu'à ce que tu sois exterminé.
25 Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
Et l'Eternel fera que tu seras battu devant tes ennemis. Tu sortiras par un chemin contr'eux, et tu t'enfuiras devant eux par sept chemins; et tu seras vagabond par tous les Royaumes de la terre.
26 Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
Et tes corps morts seront en viande à tous les oiseaux des cieux, et aux bêtes de la terre, et il n'y aura personne qui les effarouche.
27 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
L'Eternel te frappera de l'ulcère d'Egypte, d'hémorroïdes, de gale, et de grattelle, dont tu ne pourras guérir.
28 Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
L'Eternel te frappera de frénésie, et d'aveuglement, et de stupidité.
29 Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
Tu iras tâtonnant en plein midi, comme un aveugle tâtonne dans les ténèbres; tu n'amèneras point tes entreprises à un heureux succès, tu ne feras autre chose que souffrir des injustices et le pillage; et il n'y aura personne qui te garantisse.
30 Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
Tu fianceras une femme, mais un autre couchera avec elle; tu bâtiras des maisons, mais tu n'y demeureras point; tu planteras des vignes, mais tu n'en cueilleras point le fruit pour toi.
31 Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
Ton bœuf sera tué devant tes yeux, mais tu n'en mangeras point; ton âne sera ravi de devant toi, et ne te sera point rendu; tes brebis seront livrées à tes ennemis, et tu n'auras personne qui [les] en retire.
32 Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
Tes fils et tes filles seront livrés à un autre peuple, et tes yeux le verront, et se consumeront tout le jour en [regardant] vers eux; et tu n'auras aucun pouvoir en ta main.
33 Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
Et le peuple que tu n'auras point connu, mangera le fruit de ta terre, et tout ton travail; et tu ne feras autre chose que souffrir des injustices et des concussions tous les jours.
34 Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
Et tu seras hors du sens à cause des choses que tu verras de tes yeux.
35 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
L'Eternel te frappera d'un ulcère malin sur les genoux, et sur les cuisses, dont tu ne pourras être guéri; [il t'en frappera] depuis la plante de ton pied jusqu'au sommet de ta tête.
36 Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
L'Eternel te fera marcher, toi et ton Roi que tu auras établi sur toi, vers une nation que tu n'auras point connue, ni toi, ni tes pères, et tu serviras là d'autres dieux, le bois, et la pierre.
37 Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
Et tu seras là un sujet d'étonnement, de railleries, et d'invectives parmi tous les peuples vers lesquels l'Eternel t'aura emmené.
38 Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
Tu jetteras beaucoup de semence dans ton champ, et tu en recueilleras peu; car les sauterelles la consumeront.
39 Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
Tu planteras des vignes, tu les cultiveras, mais tu n'en boiras point le vin, et tu n'[en] recueilleras rien; car les vers en mangeront le fruit.
40 Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
Tu auras des oliviers en tous tes quartiers, mais tu ne t'oindras point d'huile; car tes oliviers perdront leur fruit.
41 Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
Tu engendreras des fils et des filles, mais ils ne seront pas à toi, car ils iront en captivité.
42 Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
Les hannetons gâteront tous tes arbres, et le fruit de ta terre.
43 Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
L'étranger qui est au milieu de toi, montera au dessus de toi bien haut, et tu descendras bien bas.
44 Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
Il te prêtera, et tu ne lui prêteras point; il sera à la tête, et tu seras à la queue.
45 Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
Et toutes ces malédictions viendront sur toi, et te poursuivront, et t'atteindront, jusqu'à ce que tu sois exterminé; parce que tu n'auras pas obéi à la voix de l'Eternel ton Dieu, pour garder ses commandements et ses statuts qu'il t'a prescrits.
46 Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
Et ces choses seront en toi et en ta postérité, pour signes et pour prodiges à jamais.
47 Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
Et parce que tu n'auras pas servi l'Eternel ton Dieu avec joie, et de bon cœur, malgré l'abondance de toutes choses;
48 chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
Tu serviras, dans la faim, dans la soif, dans la nudité, et dans la disette de toutes choses, ton ennemi, que l'Eternel enverra contre toi; et il mettra un joug de fer sur ton cou, jusqu'à ce qu'il t'ait exterminé.
49 Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
L'Eternel fera lever contre toi de loin, du bout de la terre, une nation qui volera comme vole l'aigle; une nation dont tu n'entendras pas la langue.
50 mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
Une nation impudente, qui n'aura point d'égard à la personne du vieillard, et qui n'aura point pitié de l'enfant.
51 Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
Elle mangera le fruit de tes bêtes, et les fruits de ta terre, jusqu'à ce que tu sois exterminé. Elle ne te laissera rien de reste, soit froment, soit vin, soit huile, ou portée de tes vaches, ou brebis de ton troupeau, jusqu'à ce qu'elle t'ait ruiné.
52 Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Et elle t'assiégera dans toutes tes villes, jusqu'à ce que tes murailles les plus hautes et les plus fortes, sur lesquelles tu te seras assuré en tout ton pays, tombent par terre. Elle assiégera, dis-je, toutes tes villes dans tout le pays que l'Eternel ton Dieu t'aura donné.
53 Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
Tu mangeras le fruit de ton ventre, la chair de tes fils et de tes filles que l'Eternel ton Dieu t'aura donnés, dans le siège et dans la détresse dont ton ennemi te serrera.
54 Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
L'homme le plus tendre et le plus délicat d'entre vous regardera d'un œil malin son frère et sa femme bien-aimée, et le reste de ses enfants qu'il aura réservés;
55 ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
Pour ne donner à aucun d'eux de la chair de ses enfants, laquelle il mangera; parce qu'il ne lui sera rien demeuré du tout, à cause du siège et de la détresse dont ton ennemi te serrera dans toutes tes villes.
56 Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
La femme la plus tendre et la plus délicate d'entre vous, qui n'eût point osé mettre la plante de son pied sur la terre, par délicatesse et par mollesse, regardera d'un œil malin son mari bien-aimé, son fils, et sa fille;
57 zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
Et la taie de son petit enfant qui sortira d'entre ses pieds, et les enfants qu'elle enfantera; car elle les mangera secrètement dans la disette de toutes choses, à cause du siège et de la détresse, dont ton ennemi te serrera dans toutes les villes.
58 Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
Si tu ne prends garde de faire toutes les paroles de cette Loi, qui sont écrites dans ce livre, en craignant le Nom glorieux et terrible de l'Eternel ton Dieu;
59 Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
Alors l'Eternel rendra tes plaies et les plaies de ta postérité des plaies étranges, des plaies grandes et de durée, des maladies malignes et longues.
60 Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
Et il fera retourner sur toi toutes les langueurs d'Egypte, desquelles tu as eu peur, et elles s'attacheront à toi.
61 Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
Même l'Eternel fera venir sur toi toute [autre] maladie, et toute [autre] plaie, qui n'est point écrite au livre de cette Loi, jusqu'à ce que tu sois exterminé.
62 Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
Et vous resterez en petit nombre, après avoir été comme les étoiles des cieux, tant vous étiez en grand nombre; parce que tu n'auras point obéi à la voix de l'Eternel ton Dieu.
63 Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
Et il arrivera que comme l'Eternel s'est réjoui sur vous, en vous faisant du bien, et en vous multipliant; de même l'Eternel se réjouira sur vous en vous faisant périr, et en vous exterminant; et vous serez arrachés de dessus la terre dans laquelle vous allez pour la posséder.
64 Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
Et l'Eternel te dispersera parmi tous les peuples, depuis un bout de la terre jusqu'à l'autre; et tu serviras là d'autres dieux, que ni toi ni tes pères n'avez point connus, le bois et la pierre.
65 Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
Encore n'auras-tu aucun repos parmi ces nations-là; même la plante de ton pied n'aura aucun repos; car l'Eternel te donnera là un cœur tremblant, et défaillance d'yeux, et détresse d'âme.
66 Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
Et ta vie sera pendante devant toi; et tu seras dans l'effroi nuit et jour, et ne seras point assuré de ta vie.
67 Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
Tu diras le matin: Qui me fera voir le soir? et le soir tu diras: Qui me fera voir le matin? à cause de l'effroi dont ton cœur sera effrayé, et à cause des choses que tu verras de tes yeux.
68 Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.
Et l'Eternel te fera retourner en Egypte sur des navires, pour faire le chemin duquel je t'ai dit: Il ne t'arrivera plus de le voir; et vous vous vendrez là à vos ennemis pour [être] esclaves et servantes, et il n'y aura personne qui vous achète.