< Deuteronomo 28 >

1 Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
Ka uluoro Jehova Nyasaye ma Nyasachu kendo urito adimba chikene duto ma amiyou kawuono, to Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro tingʼou malo moloyo ogendini duto modak e piny.
2 Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
Gwethgi duto nobed magu kamoro amora ma untie ka uluoro Jehova Nyasaye ma Nyasachu, kendo magi e gin:
3 Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
Ibiro gwedhou ka un e dala kata ka un oko.
4 Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
Nogwedhu gi nyithindo mangʼeny gi cham mogundho kod jamni mathoth ma gin kweth mag nyiroye kod mag nyirombe.
5 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
Nogwedh atongeu gi dakuondeu duto.
6 Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
Nogwedhu ka udonjo e dala kendo ka uwuok.
7 Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
Jehova Nyasaye noket wasiku ma monjou e lwetu mi unulogi. Ginimonju ka gin oganda achiel, to ginike ka gia iru ka gin migepe abiriyo.
8 Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
Jehova Nyasaye biro gwedho decheu kaachiel gi gimoro amora ma uchiworu timo, Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro gwedhou e piny ma omiyou.
9 Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
Jehova Nyasaye biro gurou kaka joge maler, mana kaka ne owacho ka okwongʼore, ka urito chike mag Jehova Nyasaye ma Nyasachu kendo uwuotho e yorene.
10 Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
Eka ji duto modak e piny none ni un joma oluong gi nying Jehova Nyasaye kendo gibiro luorou.
11 Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
Jehova Nyasaye biro miyou gweth mogundho; ma gin nyithindo mangʼeny, jamni mathoth kod cham mogundho e piny mane Jehova Nyasaye osingore kokwongʼore ni kwereu ni nomiu.
12 Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
Jehova Nyasaye biro yawo polo, ma en kar keno mag mwandune, ka ochiwo koth e piny e ndalo mowinjore, kendo ka ogwedho tije duto mag lwetu. Ubiro chiwo hola ne pinje mangʼeny to un ok unuhol gimoro kuomgi.
13 Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
Jehova Nyasaye nomi ubed jotelo to ok joma itelonegi. Ka urito chike ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu miyou kawuononi kendo uluwogi adimba, to kinde duto unubed jotelo to ok joma itelonegi.
14 Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
Kik uwe chike ma amiyou kawuononi, ka udhi e bat korachwich kata koracham kendo ka uluwo nyiseche manono kendo utiyonegi.
15 Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
To ka ok uchiwo luor ne Jehova Nyasaye ma Nyasachu kendo ok urito chikene duto adimba kod buchene ma amiyou kawuononi, to kwongʼ-gi duto biro makou.
16 Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
Ibiro kwongʼou ka un e dala kata ka un oko.
17 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
Nokwongʼ atongeu gi dakuondeu.
18 Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
Nyithindu munywolo nokwongʼ, kaachiel gi chambu, gi nyiroye mag dhou kod nyithi jambu.
19 Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
Ibiro kwongʼou ka udonjo kendo kuwuok.
20 Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
Jehova Nyasaye biro oronu kwongʼ, ngʼengʼ kod achaya e gimoro amora ma utimo, nyaka urum chuth makaru lal nono nikech richo ma usetimo ma ujwangʼe.
21 Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
Jehova Nyasaye biro goyou gi tuoche mi otieku e piny ma udhi kawo.
22 Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
Jehova Nyasaye nogou gi tuo mar kahera, midhusi gi tuo akuodi kod gwonyo kendo obiro kelonu oro mi cham rochre ewi dongo; kendo gigo duto biro thagou nyaka urum chuth.
23 Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
Polo norieny ka mula ewiu, piny to nobed matek ka chuma.
24 Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
Jehova Nyasaye enolok koth machwe e pinyu obed mana lo kod buru malich, gini olre koa e polo nyaka unurum.
25 Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
Jehova Nyasaye nomi lou e nyim wasiku. Unumonjgi ka un e achiel, to unuring-gi kuke e migepe abiriyo, kendo unubed gima wichkuot ne ogendini duto manie piny.
26 Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
Ringreu modongʼ ema nobed chiemb winy manie kor polo gi ondiegi manie thim, kendo onge ngʼato angʼata manogolgi kuomu.
27 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
Jehova Nyasaye nogou gi tuo mag buche mag Misri, akuodi, gwonyo kod kalanga ma ok thiedhi.
28 Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
Jehova Nyasaye nogou gi tuo mar neko kendo noloku muofni kendo joma orundore.
29 Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
E dier odiechiengʼ tir ubiro rundoru ka muofni e mudho. Onge gima unutim manodhi maber, ndalo duto nothiru kendo noyak giu maonge ngʼama noresu.
30 Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
Inichan kendo nyako mihero, to ngʼat moro nono ema nokawe mabed kode. Iniger ot to ok inidagie, kendo inipidh mzabibu to ok inicham gik monyak kuomgi.
31 Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
Rwadhi noyangʼ kineno, to ok ni cham ringe. Kanyna mari nokaw kuomi githuon, to ok noduognigo. Rombe magi nomi wasiki, to onge ngʼama noresgi.
32 Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
Yawuoti kod nyigi noter e pinje mamoko, kendo inimanygi gi wengeni odiechiengʼ duto kionge gi teko mar resogi.
33 Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
Oganda ma ok ingʼeyo nocham gik mitiyo matek gi luchi e puotheni kendo onge gima initim makmana tingʼ mapek kod achune e ndalou duto.
34 Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
Gik ma wangʼi neno noloki neko.
35 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
Jehova Nyasaye nomi buche maremo ma ok thiedhi mak chongeni gi tiendeni kendo ginilandre koa e pat tiendi nyaka e wiyi.
36 Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
Jehova Nyasaye biro riembou, to ruoth ma unuyier notelnu noteru e lwet piny ma kata kwereu ne ok ongʼeyo. Kuno unulamie nyiseche mamoko, ma gin nyiseche mopa gi yien kod kite.
37 Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
Inibed gima mono miyanyo kendo ijaro e kind ogendini duto kuma Jehova Nyasaye noterue.
38 Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
Unuchwo kothe mangʼeny to unuka manok, nikech bonyo nokethgi.
39 Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
Unupidh mzabibu e puotheu ma ukagi to ok unumadh olemo mochwer kuomgi kata choko olembgigo nikech kute nochamgi.
40 Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
Ubiro bedo kod yien zeituni e pinyu to ok unukonyru gi moe nikech zeituni nolwar piny.
41 Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
Unubed gi yawuowi kod nyiri to ok unuritgi nimar notergi e twech e pinje mamoko.
42 Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
Kweth mag bonyo noketh yiendu kod chambu duto e pinyu.
43 Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
Jopinje mamoko modak e pinyu nonyaa mamedre moloyou, to un to unubed manok.
44 Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
Ginibed gi gik ma giholou, to un ok nubed gi gima unyalo hologi. Ginibed jotelo, to un nubed joma itelonegi.
45 Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
Kwongʼ-gi duto nobi kuomu. Kwongʼ-gi nolaw bangʼu mijuku manyaka urum uduto, nikech ne ok uwinjo Jehova Nyasaye ma Nyasachu, kata rito chikene kod buchene duto mane omiyou.
46 Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
Ginibed ranyisi kod midhiero kuomu kod nyikwau nyaka chiengʼ.
47 Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
Nikech ne ok utiyo ne Jehova Nyasaye ma Nyasachu gi ilo kod mor e ndalo mane un gi mwandu,
48 chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
omiyo e kech, e riyo, e duk, kod dhier unutine wasiku ma Jehova Nyasaye oseoronu. Enoket jok mar mula mapek e ngʼutu nyaka chop otieku.
49 Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
Jehova Nyasaye enokel piny moro moa mabor, ma en piny mantie e giko piny, machal gi ongo mafuyo, gin oganda ma dhogi ok unuwinji,
50 mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
oganda maneno makwiny maonge gi luor ne joma oti kata joma pod tindo.
51 Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
Ginineg jambu ma pod tindo kendo giniketh chambu e puothe mi nyaka ginitieku chuth. Ok ginicham, divai manyien kata mo, kata mana nyiroye mag dhou kod nyirombe mag jambu nyaka chop gitieku chuth.
52 Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Ginitim agengʼa ne miechu madongo duto nyaka kuonde mochiel motingʼore gi malo ma uketo genou kuomgi lwar. Ginikethi mier madongo e piny duto ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu miyou.
53 Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
Nikech chandruok maniyudi ka wasiki okeloni ka in e twech, nucham nyaka nyithindu munywolo, ma gin ringre yawuotu kod nyiu ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu osemiyou.
54 Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
Kata mana ngʼat maber kendo ngʼwon ahinya e dieru ok nobed gi miwafu ne owadgi owuon kata mana ne chiege mohero kata nyithinde modongʼ,
55 ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
kendo ok enomi ngʼato angʼata ringre nyathineno ma en owuon ochamo nikech mano kende e gima nodongʼ bangʼ ka wasigu osemonjo miechu.
56 Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
Dhako makare kendo man-gi lony mamalo e dieru, ngʼat modimbore kendo man-gi ngʼwono malach ma bende ok osewuotho e lowo gi tiende nono, nobed ka iye kwar kod chwore owuon kata mana gi yawuote kod nyige ma en owuon ema onywolo.
57 zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
Notamre pogonegi kata mana bieche owuon bangʼ nywol, nimar oparo mondo ochamgi lingʼ-lingʼ e ndalo ma wasiku nogonu agengʼa ka masira olworo miechu madongo.
58 Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
Ka ok urito weche duto manie chikni ma ondiki e kitabuni kendo ka ok uchiwo luor ne nyinge man-gi teko ma en Jehova Nyasaye ma Nyasachu,
59 Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
Jehova Nyasaye biro kelo masiche malich kuomu kaachiel gi nyikwau, tuoche maywayo dend ji kuom kinde mangʼeny.
60 Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
Obiro keto kuomu tuoche duto mag Misri ma uluoro kendo ginibed kuomu.
61 Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
Jehova Nyasaye nokel kuomu kit tuoche duto ma ok ondiki e kitabuni mar chik nyaka chop tieku chuth.
62 Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
Un ma ungʼeny ka sulwe manie polo unudongʼ matin nikech ne ok urito chike Jehova Nyasaye ma Nyasachu.
63 Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
Mana kaka ne omoro Jehova Nyasaye mondo omiu gweth kendo ubed mangʼeny, e kaka obiro bedo gi mor ka oranou kendo otiekou. Notieku e piny ma udonjoe mondo ukaw.
64 Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
Eka Jehova Nyasaye nokewu e pinje duto, koa e tungʼ piny konchiel nyaka machielo. Kanyo unulamie nyiseche mamoko, ma gin nyiseche mopa mag yiende kod kite ma un uwegi kod ka kwereu ne ok ongʼeyo.
65 Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
E kind pinjego ok unuyudie hoch kata yweyo ka ombongʼ tiendeu ool. Kuno Jehova Nyasaye nomiu paro maliw, wangʼ maneno ka ool gi dwaro to gi chuny machandore.
66 Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
Unudag ka ukia gima biro timorenu; ka un gilworo odiechiengʼ kod otieno, ka ukia gima biro timore ne ngimau.
67 Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
Ka piny oru gokinyi unuwach niya, “Mad ne bedni en odhiambo” kendo godhiambo unuwach niya, “Mad ne piny bed ni en okinyi” nikech masira ma unune nopongʼ chunyu kod gik ma wengeu none.
68 Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.
Jehova Nyasaye nooru dok Misri gi yiedhi, e wuoth mane awacho ni ok onego udhiye. Kuno unuchiwru ne wasiku kaka chwo kod mon ma jotich to onge ngʼama noyie ngʼiewou.

< Deuteronomo 28 >