< Deuteronomo 27 >
1 Mose ndi akuluakulu a Israeli analamula anthu kuti, “Sungani malamulo onse amene ndikukupatsani lero lino.
And Moses with the elders of Israel commanded the people saying, —Observe all the commandment which I am commanding you to-day.
2 Mukawoloka mtsinje wa Yorodani kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, muyimiritse miyala ingapo ikuluikulu ndi kuyikulungiza.
So then it shall be in the day when ye shall pass over the Jordan, into the land which Yahweh thy God is giving unto thee, —that thou shalt rear thee up great stones, and plaster them with plaster;
3 Mulembepo mawu onse a malamulo amenewa pamene muwoloka kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, dziko loyenda mkaka ndi uchi, monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
and shalt write upon them all the words of this law, when thou shalt pass over, —to the end that thou mayest enter upon the land which Yahweh thy God is giving unto thee a land flowing with milk and honey, as Yahweh the God of thy fathers hath spoken unto thee.
4 Ndipo mukawoloka Yorodani muyimike miyala iyi pa Phiri la Ebala monga momwe ndikukulamulirani lero lino ndipo muyikulungize.
So then it shall be when ye shall pass over the Jordan, that ye shall rear up these stones which I am commanding you to-day in Mount Ebal, —and thou shalt plaster them with plaster.
5 Pamenepo mumange guwa lansembe la miyala la Yehova Mulungu wanu. Musagwiritse ntchito chida chilichonse chachitsulo pa miyalapo.
And thou shalt build there an altar unto Yahweh thy God, —an altar of stones, thou shalt not wield thereupon any tool of iron.
6 Mumange guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu ndi miyala yakutchire ndi kuperekerapo nsembe yopsereza kwa Yehova Mulungu wanu.
Of whole stones, shalt thou build the altar of Yahweh thy God, —then shalt thou cause to go up thereon ascending-sacrifices, unto Yahweh thy God;
7 Muperekerepo nsembe zopereka za chiyanjano, muzidye ndi kukondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
and thou shalt sacrifice peace-offerings and shalt eat there, —and rejoice before Yahweh thy God.
8 Ndipo pa miyalapo mudzalembepo mawu onse a malamulo ndi malemba akuluakulu.”
And thou shalt write upon the stones all the words of this law doing it plainly and well.
9 Kenaka Mose ndi ansembe, amene ndi Alevi anati kwa Aisraeli onse, “Khalani chete Aisraeli inu ndipo mumvetsere! Tsopano inu ndinu anthu a Yehova Mulungu wanu.
And Moses and the priests the Levites spake unto all Israel saying, —Keep silence and hear O Israel, This day, hast thou been made a people unto Yahweh thy God.
10 Muzimvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsata malamulo ake ndi malangizo ake omwe ndikukupatsani lero lino.”
Thou shalt therefore hearken unto the voice of Yahweh thy God, —and do his commandments and his statutes, which I am commanding thee to-day.
11 Tsiku lomwelo Mose analamula anthu kuti:
And Moses commanded the people on that day, saying:
12 Mukawoloka Yorodani, mafuko awa akayimirire pa Phiri la Gerizimu ndi kudalitsa anthu: Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Yosefe ndi Benjamini.
These, shall stand to bless the people upon Mount Gerizim, when ye have passed over the Jordan, —Simeon and Levi and Judah, and Issachar and Joseph and Benjamin;
13 Ndipo mafuko awa akayimirire pa Phiri la Ebala ndi kutchula matemberero: Rubeni, Gadi, Aseri, Zebuloni, Dani ndi Nafutali.
and, these, shall stand by the curse in Mount Ebal, —Reuben Gad and Asher, and Zebulun Dan and Naphtali.
14 Alevi adzayankhula mokweza kwa Aisraeli onse kuti:
Then shall the Levites respond and say unto every man of Israel with voice uplifted: —
15 “Ndi wotembereredwa munthu amene asema chifanizo kapena kupanga fano, ndi kuchiyika mobisa, pakuti chimenechi ndi chinthu chodetsedwa pamaso pa Yehova, ntchito za manja a anthu.”
Cursed, be the man that maketh an image—cut or molten—an abomination unto Yahweh the work of the hands of the craftsman and putteth it in a secret place. And all the people shall respond and say—Amen.
16 “Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira ulemu abambo ake kapena amayi ake.”
Cursed, be he that holdeth in light esteem his father or his mother. And all the people shall say—Amen.
17 “Ndi wotembereredwa munthu amene amasuntha mwala wa malire wa mnzake.”
Cursed, be he that moveth back the boundary of his neighbour. And all the people shall say—Amen.
18 “Ndi wotembereredwa munthu amene amasocheretsa munthu wosaona pa msewu.”
Cursed, be he that causeth the blind to wander in the way. And all the people shall say—Amen.
19 “Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira chilungamo mlendo, ana amasiye kapena mkazi wamasiye.”
Cursed, be he that perverteth the right of the sojourner, the fatherless, or the widow. And all the people shall say—Amen.
20 “Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mkazi wa abambo ake pakuti iye sachitira ulemu pogona pa abambo ake.”
Cursed, be he that lieth with his father’s wife, because he hath turned aside his father’s coverlet. And all the people shall say—Amen.
21 “Ndi wotembereredwa munthu amene achita chigololo ndi nyama ya mtundu uli wonse.”
Cursed, be he that lieth with any beast. And all the people shall say—Amen.
22 “Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake kapena mwana wamkazi wa amayi ake.”
Cursed, be he that lieth with his sister, daughter of his father or daughter of his mother. And all the people shall say—Amen.
23 “Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi apongozi ake.”
Cursed, be he that lieth with his mother-in-law. And all the people shall say—Amen.
24 “Ndi wotembereredwa munthu amene apha mnzake mwachinsinsi.”
Cursed, be he that smiteth his neighbour secretly. And all the people shall say—Amen.
25 “Ndi wotembereredwa munthu amene alandira chiphuphu kuti aphe munthu wosalakwa.”
Cursed, be he that taketh a bribe to shed innocent blood. And all the people shall say—Amen.
26 “Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita kapena sasunga mawu a malamulo awa.”
Cursed, be he that establisheth not the words of this law to do them. And all the people shall say—Amen.