< Deuteronomo 27 >
1 Mose ndi akuluakulu a Israeli analamula anthu kuti, “Sungani malamulo onse amene ndikukupatsani lero lino.
And Moses and the elders of Israel commanded the people, saying, Keep all the commandment which I command you this day.
2 Mukawoloka mtsinje wa Yorodani kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, muyimiritse miyala ingapo ikuluikulu ndi kuyikulungiza.
And it shall be on the day when ye shall pass over the Jordan to the land which Jehovah thy God gives thee, that thou shall set up for thee great stones, and plaster them with plaster.
3 Mulembepo mawu onse a malamulo amenewa pamene muwoloka kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, dziko loyenda mkaka ndi uchi, monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
And thou shall write upon them all the words of this law when thou have passed over, that thou may go in to the land which Jehovah thy God gives thee, a land flowing with milk and honey, as Jehovah, the God of thy fathers, has promised thee.
4 Ndipo mukawoloka Yorodani muyimike miyala iyi pa Phiri la Ebala monga momwe ndikukulamulirani lero lino ndipo muyikulungize.
And it shall be, when ye have passed over the Jordan, that ye shall set up these stones, which I command you this day, in mount Ebal, and thou shall plaster them with plaster.
5 Pamenepo mumange guwa lansembe la miyala la Yehova Mulungu wanu. Musagwiritse ntchito chida chilichonse chachitsulo pa miyalapo.
And there thou shall build an altar to Jehovah thy God, an altar of stones. Thou shall lift up no iron upon them.
6 Mumange guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu ndi miyala yakutchire ndi kuperekerapo nsembe yopsereza kwa Yehova Mulungu wanu.
Thou shall build the altar of Jehovah thy God of unhewn stones. And thou shall offer burnt offerings on it to Jehovah thy God.
7 Muperekerepo nsembe zopereka za chiyanjano, muzidye ndi kukondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
And thou shall sacrifice peace offerings, and shall eat there, and thou shall rejoice before Jehovah thy God.
8 Ndipo pa miyalapo mudzalembepo mawu onse a malamulo ndi malemba akuluakulu.”
And thou shall write upon the stones all the words of this law very plainly.
9 Kenaka Mose ndi ansembe, amene ndi Alevi anati kwa Aisraeli onse, “Khalani chete Aisraeli inu ndipo mumvetsere! Tsopano inu ndinu anthu a Yehova Mulungu wanu.
And Moses and the priests the Levites spoke to all Israel, saying, Keep silence, and hearken, O Israel. This day thou have become the people of Jehovah thy God.
10 Muzimvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsata malamulo ake ndi malangizo ake omwe ndikukupatsani lero lino.”
Thou shall therefore obey the voice of Jehovah thy God, and do his commandments and his statutes, which I command thee this day.
11 Tsiku lomwelo Mose analamula anthu kuti:
And Moses charged the people the same day, saying,
12 Mukawoloka Yorodani, mafuko awa akayimirire pa Phiri la Gerizimu ndi kudalitsa anthu: Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Yosefe ndi Benjamini.
These shall stand upon mount Gerizim to bless the people, when ye have passed over the Jordan: Simeon, and Levi, and Judah, and Issachar, and Joseph, and Benjamin.
13 Ndipo mafuko awa akayimirire pa Phiri la Ebala ndi kutchula matemberero: Rubeni, Gadi, Aseri, Zebuloni, Dani ndi Nafutali.
And these shall stand upon mount Ebal for the curse: Reuben, Gad, and Asher, and Zebulun, Dan, and Naphtali.
14 Alevi adzayankhula mokweza kwa Aisraeli onse kuti:
And the Levites shall answer, and say to all the men of Israel with a loud voice,
15 “Ndi wotembereredwa munthu amene asema chifanizo kapena kupanga fano, ndi kuchiyika mobisa, pakuti chimenechi ndi chinthu chodetsedwa pamaso pa Yehova, ntchito za manja a anthu.”
Cursed be the man who makes a graven or molten image, an abomination to Jehovah, the work of the hands of the craftsman, and sets it up in secret. And all the people shall answer and say, Truly.
16 “Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira ulemu abambo ake kapena amayi ake.”
Cursed be he who dishonors his father or his mother. And all the people shall say, Truly.
17 “Ndi wotembereredwa munthu amene amasuntha mwala wa malire wa mnzake.”
Cursed be he who removes his neighbor's landmark. And all the people shall say, Truly.
18 “Ndi wotembereredwa munthu amene amasocheretsa munthu wosaona pa msewu.”
Cursed be he who makes the blind to wander out of the way. And all the people shall say, Truly.
19 “Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira chilungamo mlendo, ana amasiye kapena mkazi wamasiye.”
Cursed be he who distorts the justice to the sojourner, fatherless, and widow. And all the people shall say, Truly.
20 “Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mkazi wa abambo ake pakuti iye sachitira ulemu pogona pa abambo ake.”
Cursed be he who lies with his father's wife, because he has uncovered his father's skirt. And all the people shall say, Truly.
21 “Ndi wotembereredwa munthu amene achita chigololo ndi nyama ya mtundu uli wonse.”
Cursed be he who lies with any manner of beast. And all the people shall say, Truly.
22 “Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake kapena mwana wamkazi wa amayi ake.”
Cursed be he who lies with his sister, the daughter of his father, or the daughter of his mother. And all the people shall say, Truly.
23 “Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi apongozi ake.”
Cursed be he who lies with his mother-in-law. And all the people shall say, Truly.
24 “Ndi wotembereredwa munthu amene apha mnzake mwachinsinsi.”
Cursed be he who smites his neighbor in secret. And all the people shall say, Truly.
25 “Ndi wotembereredwa munthu amene alandira chiphuphu kuti aphe munthu wosalakwa.”
Cursed be he who takes a bribe to kill an innocent man. And all the people shall say, Truly.
26 “Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita kapena sasunga mawu a malamulo awa.”
Cursed is every man who does not continue in all the words of this law to do them. And all the people shall say, Truly.