< Deuteronomo 26 >
1 Mukalowa ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu,
“Tanrınız RAB'bin miras olarak size vereceği ülkeye girip orayı mülk edinerek yerleştiğinizde,
2 mutengeko zina mwa zipatso zoyamba pa zonse zimene mudzakola mʼnthaka ya dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndi kuziyika mʼdengu. Mukatero mupite kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzakhazikitsako dzina lake
Tanrınız RAB'bin size vereceği ülkenin topraklarından topladığınız bütün ürünlerin ilk yetişenlerini alıp sepete koyacaksınız. Sonra Tanrınız RAB'bin adını yerleştirmek için seçeceği yere gideceksiniz.
3 ndipo mudzamuwuze wansembe amene ali pa ntchito pa nthawiyo kuti, “Ndikunenetsa lero kwa Yehova Mulungu wanu kuti ndabwera ku dziko limene Yehova analumbirira makolo athu kuti adzatipatsa ife.”
O dönemde görevli kâhine gidip, ‘RAB'bin bize ant içerek atalarımıza söz verdiği ülkeye geldiğimi Tanrın RAB'be bugün bildiriyorum’ diyeceksiniz.
4 Wansembe adzatenga dengulo mʼmanja mwanu ndi kuliyika pansi patsogolo pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
Kâhin sepeti elinizden alıp Tanrınız RAB'bin sunağının önüne koyacak.
5 Ndipo mudzanenetsa pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, “Abambo anga anali Mwaramu woyendayenda, anapita ku Igupto ndi anthu ochepa nakhala kumeneko. Pambuyo pake anakhala mtundu waukulu, wamphamvu ndi wochuluka.
Sonra Tanrınız RAB'bin önünde şu açıklamayı yapacaksınız: ‘Atam göçebe bir Aramlı'ydı. Sayıca az kişiyle Mısır'a gidip orada yaşamaya başladı. Orada büyük, güçlü, kalabalık bir ulus oldu.
6 Koma Aigupto anatisautsa natizunza, kumatigwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Mısırlılar bize kötü davranarak baskı yaptılar. Bizi ağır işlere zorladılar.
7 Kenaka tinafuwulira Yehova, Mulungu wa makolo athu ndipo Yehova anamva mawu athu ndi kuona kusauka, kuvutika ndi kuponderezedwa kwathu.
Atalarımızın Tanrısı RAB'be yakardık. RAB yakarışımızı duydu; çektiğimiz sıkıntıyı, emeği, bize yapılan baskıyı gördü.
8 Kotero Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndi mkono wotambasuka ndi zoopsa zazikulu ndi zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa.
Bunun üzerine güçlü elle, kudretle, büyük ve ürkütücü olaylarla, belirtilerle, şaşılası işlerle bizi Mısır'dan çıkardı.
9 Iye anatibweretsa ku malo ano natipatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi lino.
Bizi buraya getirdi; bu toprakları, süt ve bal akan ülkeyi bize verdi.
10 Ndipo tsopano ndikubweretsa zipatso zoyamba zimene inu Yehova mwandipatsa.” Ikani dengulo pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kuwerama mopereka ulemu pamaso pake.
Şimdi, ya RAB, bize verdiğin toprağın ürününün ilk yetişenini getiriyorum.’ Sonra sepeti Tanrınız RAB'bin önüne koyup O'nun önünde yere kapanacaksınız.
11 Ndipo inu ndi Alevi pamodzi ndi alendo okhala pakati panu mudzakondwera mʼzinthu zonse zabwino zimene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, inu ndi a pa banja panu.
Sizler, Levililer ve aranızda yaşayan yabancılar Tanrınız RAB'bin size ve ailenize verdiği bütün iyi şeyler için sevineceksiniz.
12 Mukatha kupatula chakhumi pa zonse zimene mwakolola mʼchaka chachitatu chimene ndi chaka chakhumi, muzichipereka kwa wansembe, mlendo, ana ndi akazi amasiye, kuti pamenepo adye mʼmizinda yanu nakhuta.
“Üçüncü yıl, ondalığı verme yılı, bütün ürününüzün ondalığını bir yana ayırın. Ayırma işini bitirdiğinizde, ondalığı Levililer'e, yabancılara, öksüzlere ve dul kadınlara vereceksiniz. Öyle ki, onlar da kentlerinizde yiyip doysunlar.
13 Kenaka munene kwa Yehova Mulungu wanu kuti “Ndatulutsamo mʼnyumba mwanga gawo lopatulika ndipo ndalipereka kwa Mlevi, mlendo, ana ndi akazi amasiye, monga mwa zonse zimene munalamula. Sindinapatuke pa zimene munalamula kapena kuyiwala ndi chimodzi chomwe.
Sonra Tanrınız RAB'be, ‘Bana buyurduğun gibi, RAB'be ayırdıklarımı evden çıkarıp Levililer'e, yabancılara, öksüzlere ve dul kadınlara verdim’ diyeceksiniz, ‘Buyruklarından ayrılmadım, hiç birini unutmadım.
14 Sindinadye kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndimalira maliro kapena kuchotsapo kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndinali wodetsedwa, kapena kuperekako nsembe kwa akufa kalikonse ka gawoli. Ine ndamvera Yehova Mulungu wanga, ndachita chilichonse chimene inu munandilamula.
Ne yas tutarken ayırdıklarımdan yedim, ne dinsel açıdan kirliyken onlara dokundum, ne de ölülere sundum. Tanrım RAB'bin sözüne kulak verdim. Bana bütün buyurduklarını yaptım.
15 Yangʼanani pa dziko kuchokera kumwamba, ku malo anu wopatulika, ndi kudalitsa anthu anu Aisraeli ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi limene mwatipatsa ife monga momwe munalonjezera pa malumbiro anu kwa makolo athu.”
Kutsal konutundan, göklerden aşağıya bak! Halkın İsrail'i ve atalarımıza içtiğin ant uyarınca bize verdiğin ülkeyi, süt ve bal akan ülkeyi kutsa.’”
16 Yehova Mulungu wanu akukulamulani lero lino kuti mutsate malangizo ndi malamulo ake ndipo muwasunge mosamalitsa ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
“Bugün Tanrınız RAB bu kurallara, ilkelere uymanızı buyuruyor. Onlara bütün yüreğinizle, canınızla uymaya dikkat edin.
17 Mwanena motsimikiza lero lino kuti Yehova ndiye Mulungu wanu ndi kuti mudzayenda mʼnjira zake, kusunga malangizo, malamulo ndi zonse akukulamulani ndi kutinso mudzamumvera.
Bugün RAB'bin Tanrınız olduğunu, O'nun yollarında yürüyeceğinizi, kurallarına, buyruklarına, ilkelerine uyacağınızı, O'nun sözünü dinleyeceğinizi açıkladınız.
18 Ndipo Yehova wanenetsa lero lino kuti inu ndinu anthu ake, chuma chake chamtengowapatali monga momwe analonjezera, ndipo mukuyenera kusunga malamulo ake onse.
Bugün RAB, size verdiği söz uyarınca, öz halkı olduğunuzu açıkladı. Bütün buyruklarına uyacaksınız.
19 Iye wanenetsa kuti adzakuyikani kukhala oyamikika, otchuka ndi olemekezeka koposa mitundu yonse imene anayilenga. Komanso mudzakhala anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu monga momwe analonjezera.
Tanrınız RAB sizi övgüde, ünde, onurda yarattığı bütün uluslardan üstün kılacağını, verdiği söz uyarınca kendisi için kutsal bir halk olacağınızı açıkladı.”