< Deuteronomo 26 >

1 Mukalowa ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu,
När du kommer in i landet, som Herren din Gud dig till arfs gifva skall, och du tager det in, och bor der;
2 mutengeko zina mwa zipatso zoyamba pa zonse zimene mudzakola mʼnthaka ya dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndi kuziyika mʼdengu. Mukatero mupite kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzakhazikitsako dzina lake
Så skall du taga allahanda landsens första frukter, som af jordene komma, som Herren din Gud dig gifver, och skall lägga dem uti en korg, och gå bort på det rum, som Herren din Gud utväljandes varder, att hans Namn der bo skall;
3 ndipo mudzamuwuze wansembe amene ali pa ntchito pa nthawiyo kuti, “Ndikunenetsa lero kwa Yehova Mulungu wanu kuti ndabwera ku dziko limene Yehova analumbirira makolo athu kuti adzatipatsa ife.”
Och skall gå till Presten, som på den tiden är, och säga till honom: Jag förkunnar på denna dag Herranom dinom Gud, att jag är kommen in uti det land, som Herren vårom fädrom svorit hafver till att gifva oss.
4 Wansembe adzatenga dengulo mʼmanja mwanu ndi kuliyika pansi patsogolo pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
Och Presten skall taga korgen utu dine hand, och sätta honom ned för Herrans dins Guds altare.
5 Ndipo mudzanenetsa pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, “Abambo anga anali Mwaramu woyendayenda, anapita ku Igupto ndi anthu ochepa nakhala kumeneko. Pambuyo pake anakhala mtundu waukulu, wamphamvu ndi wochuluka.
Då skall du svara, och säga för Herranom dinom Gud: De Syrer ville förgöra min fader, han drog neder i Egypten, och var der en främling med fögo folk; och vardt der ett stort, starkt och mycket folk.
6 Koma Aigupto anatisautsa natizunza, kumatigwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Men de Egyptier handlade illa med oss, och tvingade oss, och lade en hård träldom på oss.
7 Kenaka tinafuwulira Yehova, Mulungu wa makolo athu ndipo Yehova anamva mawu athu ndi kuona kusauka, kuvutika ndi kuponderezedwa kwathu.
Då ropade vi till Herran våra fäders Gud, och Herren hörde vårt rop, och såg vårt elände, ångest och nöd.
8 Kotero Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndi mkono wotambasuka ndi zoopsa zazikulu ndi zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa.
Och Herren förde oss utur Egypten med väldiga hand och uträcktom arm, och med stor förfärelse genom tecken och under;
9 Iye anatibweretsa ku malo ano natipatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi lino.
Och förde oss på detta rummet, och gaf oss detta landet, der mjölk och hannog uti flyter.
10 Ndipo tsopano ndikubweretsa zipatso zoyamba zimene inu Yehova mwandipatsa.” Ikani dengulo pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kuwerama mopereka ulemu pamaso pake.
Och derföre bär jag nu här fram landsens första frukt, som du, Herre, mig gifvit hafver. Och så skall du låta det der för Herranom dinom Gud, och tillbedja för Herranom dinom Gud;
11 Ndipo inu ndi Alevi pamodzi ndi alendo okhala pakati panu mudzakondwera mʼzinthu zonse zabwino zimene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, inu ndi a pa banja panu.
Och vara glad öfver allt det goda, som Herren din Gud hafver gifvit dig, och dino huse, du och Leviten, och främlingen som när dig är.
12 Mukatha kupatula chakhumi pa zonse zimene mwakolola mʼchaka chachitatu chimene ndi chaka chakhumi, muzichipereka kwa wansembe, mlendo, ana ndi akazi amasiye, kuti pamenepo adye mʼmizinda yanu nakhuta.
När du hafver tillhopasamlat allan tionden af din årsväxt i tredje årena, hvilket är ett tiondeår, så skall du gifva Levitenom, främlingenom, dem faderlösa och enkone, att de måga äta i dinom port, och varda mätte;
13 Kenaka munene kwa Yehova Mulungu wanu kuti “Ndatulutsamo mʼnyumba mwanga gawo lopatulika ndipo ndalipereka kwa Mlevi, mlendo, ana ndi akazi amasiye, monga mwa zonse zimene munalamula. Sindinapatuke pa zimene munalamula kapena kuyiwala ndi chimodzi chomwe.
Och skall säga för Herranom dinom Gud: Jag hafver här framburit det som helgadt är af mino huse, och hafver gifvit det Levitenom, främlingenom, dem faderlösa och enkone, efter allt ditt bud, som du mig budit hafver; jag hafver icke gått utöfver ditt bud, eller förgätit det;
14 Sindinadye kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndimalira maliro kapena kuchotsapo kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndinali wodetsedwa, kapena kuperekako nsembe kwa akufa kalikonse ka gawoli. Ine ndamvera Yehova Mulungu wanga, ndachita chilichonse chimene inu munandilamula.
Jag hafver icke ätit deraf i mine sorg; jag hafver intet tagit deraf i orenlighet; jag hafver intet deraf gifvit till de döda; jag hafver varit Herrans mins Guds röst hörig, och hafver gjort allt det du mig budit hafver.
15 Yangʼanani pa dziko kuchokera kumwamba, ku malo anu wopatulika, ndi kudalitsa anthu anu Aisraeli ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi limene mwatipatsa ife monga momwe munalonjezera pa malumbiro anu kwa makolo athu.”
Se här neder af dine helga boning af himmelen, och välsigna ditt folk Israel, och landet som du oss gifvit hafver, såsom du våra fäder svorit hafver, ett land der mjölk och hannog uti flyter.
16 Yehova Mulungu wanu akukulamulani lero lino kuti mutsate malangizo ndi malamulo ake ndipo muwasunge mosamalitsa ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
I dag hafver Herren din Gud budit dig, att du efter all dessa bud och rätter göra skall, så att du håller dem, och gör derefter af allo hjerta, och af allo själ.
17 Mwanena motsimikiza lero lino kuti Yehova ndiye Mulungu wanu ndi kuti mudzayenda mʼnjira zake, kusunga malangizo, malamulo ndi zonse akukulamulani ndi kutinso mudzamumvera.
Herranom hafver du det tillsagt i denna dag, att han skall vara din Gud, och du skall vandra i hans vägar, och hålla hans lag, bud och rätter, och lyda hans röst.
18 Ndipo Yehova wanenetsa lero lino kuti inu ndinu anthu ake, chuma chake chamtengowapatali monga momwe analonjezera, ndipo mukuyenera kusunga malamulo ake onse.
Herren hafver dig tillsagt i dag, att du skall vara hans eget folk, såsom han dig sagt hafver; att du skall hålla all hans bud;
19 Iye wanenetsa kuti adzakuyikani kukhala oyamikika, otchuka ndi olemekezeka koposa mitundu yonse imene anayilenga. Komanso mudzakhala anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu monga momwe analonjezera.
Och han skall göra dig det högsta, och du varder prisad, lofvad och ärad, öfver allt folk som han gjort hafver; på det du skall vara Herranom dinom Gud ett heligt folk, såsom han sagt hafver.

< Deuteronomo 26 >