< Deuteronomo 26 >
1 Mukalowa ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu,
Kuzakuthi-ke lapho usufikile elizweni iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona libe yilifa, udle ilifa lalo, uhlale kulo,
2 mutengeko zina mwa zipatso zoyamba pa zonse zimene mudzakola mʼnthaka ya dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndi kuziyika mʼdengu. Mukatero mupite kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzakhazikitsako dzina lake
uthathe okokuqala kwezithelo zonke zomhlabathi ozakuletha kuvela elizweni lakho iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona, ukufake esitsheni, uye endaweni iNkosi uNkulunkulu wakho ezayikhetha ukuhlalisa ibizo layo khona.
3 ndipo mudzamuwuze wansembe amene ali pa ntchito pa nthawiyo kuti, “Ndikunenetsa lero kwa Yehova Mulungu wanu kuti ndabwera ku dziko limene Yehova analumbirira makolo athu kuti adzatipatsa ife.”
Uzakuya kumpristi ozakuba ekhona ngalezonsuku uthi kuye: Ngiyabika lamuhla eNkosini uNkulunkulu wakho ukuthi sengifikile elizweni iNkosi eyalifungela obaba ukusinika lona.
4 Wansembe adzatenga dengulo mʼmanja mwanu ndi kuliyika pansi patsogolo pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
Njalo umpristi uzathatha isitsha esandleni sakho, asibeke phambi kwelathi leNkosi uNkulunkulu wakho.
5 Ndipo mudzanenetsa pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, “Abambo anga anali Mwaramu woyendayenda, anapita ku Igupto ndi anthu ochepa nakhala kumeneko. Pambuyo pake anakhala mtundu waukulu, wamphamvu ndi wochuluka.
Khona uzaphendula uthi phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho: Ubaba wayengumSiriya obhubhayo, wehlela eGibhithe, wahlala khona njengowezizwe labantu abalutshwana; kodwa lapho waba yisizwe esikhulu esilamandla lesilabanengi.
6 Koma Aigupto anatisautsa natizunza, kumatigwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Kodwa amaGibhithe asiphatha kubi, asihlupha, asethwesa ubugqili obunzima.
7 Kenaka tinafuwulira Yehova, Mulungu wa makolo athu ndipo Yehova anamva mawu athu ndi kuona kusauka, kuvutika ndi kuponderezedwa kwathu.
Sasesikhala eNkosini uNkulunkulu wabobaba; iNkosi yalizwa ilizwi lethu, yabona inhlupheko yethu, lokutshikatshika kwethu, locindezelo lwethu;
8 Kotero Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndi mkono wotambasuka ndi zoopsa zazikulu ndi zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa.
iNkosi yasikhupha eGibhithe ngesandla esilamandla langengalo eyeluliweyo, langokwesabeka okukhulu, langezibonakaliso, langezimangaliso;
9 Iye anatibweretsa ku malo ano natipatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi lino.
yasiletha kulindawo, yasinika lelilizwe, ilizwe eligeleza uchago loluju.
10 Ndipo tsopano ndikubweretsa zipatso zoyamba zimene inu Yehova mwandipatsa.” Ikani dengulo pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kuwerama mopereka ulemu pamaso pake.
Khathesi-ke, khangela, ngilethile ukuqala kwezithelo zomhlabathi, Nkosi, onginike khona. Njalo uzakubeka phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho, ukhonze phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho;
11 Ndipo inu ndi Alevi pamodzi ndi alendo okhala pakati panu mudzakondwera mʼzinthu zonse zabwino zimene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, inu ndi a pa banja panu.
uthokoze ngakho konke okuhle iNkosi uNkulunkulu wakho ekunike khona labendlu yakho, wena lomLevi lowemzini ophakathi kwakho.
12 Mukatha kupatula chakhumi pa zonse zimene mwakolola mʼchaka chachitatu chimene ndi chaka chakhumi, muzichipereka kwa wansembe, mlendo, ana ndi akazi amasiye, kuti pamenepo adye mʼmizinda yanu nakhuta.
Lapho usuqedile ukunika okwetshumi, konke okwetshumi kwezithelo zakho ngomnyaka wesithathu, umnyaka wokunika okwetshumi, usukunike umLevi, owemzini, intandane lomfelokazi ukuze badle phakathi kwamasango akho basuthe,
13 Kenaka munene kwa Yehova Mulungu wanu kuti “Ndatulutsamo mʼnyumba mwanga gawo lopatulika ndipo ndalipereka kwa Mlevi, mlendo, ana ndi akazi amasiye, monga mwa zonse zimene munalamula. Sindinapatuke pa zimene munalamula kapena kuyiwala ndi chimodzi chomwe.
uzakuthi phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho: Sengikhuphile endlini yami into engcwele, lami njalo ngakunika umLevi, lowemzini, intandane, lomfelokazi, njengayo yonke imilayo yakho ongilaye yona; kangeqanga okwemilayo yakho, futhi kangiyikhohlwanga.
14 Sindinadye kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndimalira maliro kapena kuchotsapo kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndinali wodetsedwa, kapena kuperekako nsembe kwa akufa kalikonse ka gawoli. Ine ndamvera Yehova Mulungu wanga, ndachita chilichonse chimene inu munandilamula.
Kangidlanga kukho ekulileni kwami, kangisuselanga kukho ukungcola, kangikunikelanga okwakho kofileyo; ngililalele ilizwi leNkosi uNkulunkulu wami, ngenzile njengakho konke ongilaye khona.
15 Yangʼanani pa dziko kuchokera kumwamba, ku malo anu wopatulika, ndi kudalitsa anthu anu Aisraeli ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi limene mwatipatsa ife monga momwe munalonjezera pa malumbiro anu kwa makolo athu.”
Khangela phansi usendaweni yakho yokuhlala engcwele usemazulwini, ubusise abantu bakho uIsrayeli lomhlaba osinike wona, njengokufunga kwakho kubobaba, ilizwe eligeleza uchago loluju.
16 Yehova Mulungu wanu akukulamulani lero lino kuti mutsate malangizo ndi malamulo ake ndipo muwasunge mosamalitsa ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Lamuhla iNkosi uNkulunkulu wakho iyakulaya ukuthi wenze lezizimiso lezahlulelo; ngakho uzazigcina uzenze ngenhliziyo yakho yonke langomphefumulo wakho wonke.
17 Mwanena motsimikiza lero lino kuti Yehova ndiye Mulungu wanu ndi kuti mudzayenda mʼnjira zake, kusunga malangizo, malamulo ndi zonse akukulamulani ndi kutinso mudzamumvera.
Lamuhla uvumile obala ukuthi iNkosi inguNkulunkulu wakho, lokuthi uzahamba endleleni zayo, ugcine izimiso zayo lemilayo yayo lezahlulelo zayo, ulalele ilizwi layo.
18 Ndipo Yehova wanenetsa lero lino kuti inu ndinu anthu ake, chuma chake chamtengowapatali monga momwe analonjezera, ndipo mukuyenera kusunga malamulo ake onse.
Futhi iNkosi ivumile obala lamuhla ukuthi uzakuba yisizwe sayo esikhethekileyo njengokukuthembisa kwayo, lokuthi ugcine yonke imilayo yayo,
19 Iye wanenetsa kuti adzakuyikani kukhala oyamikika, otchuka ndi olemekezeka koposa mitundu yonse imene anayilenga. Komanso mudzakhala anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu monga momwe analonjezera.
ukuze ikuphakamise phezu kwezizwe zonke ezenzileyo, ekubongweni, lebizweni, lenhlonipheni, lokuthi ube yisizwe esingcwele eNkosini uNkulunkulu wakho njengokutsho kwayo.