< Deuteronomo 26 >
1 Mukalowa ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu,
Now when you have come into the land which the Lord is giving you for your heritage, and you have made it yours and are living in it;
2 mutengeko zina mwa zipatso zoyamba pa zonse zimene mudzakola mʼnthaka ya dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndi kuziyika mʼdengu. Mukatero mupite kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzakhazikitsako dzina lake
You are to take a part of the first-fruits of the earth, which you get from the land which the Lord your God is giving you, and put it in a basket, and go to the place marked out by the Lord your God, as the resting-place of his name.
3 ndipo mudzamuwuze wansembe amene ali pa ntchito pa nthawiyo kuti, “Ndikunenetsa lero kwa Yehova Mulungu wanu kuti ndabwera ku dziko limene Yehova analumbirira makolo athu kuti adzatipatsa ife.”
And you are to come to him who is priest at that time, and say to him, I give witness today before the Lord your God, that I have come into the land which the Lord made an oath to our fathers to give us.
4 Wansembe adzatenga dengulo mʼmanja mwanu ndi kuliyika pansi patsogolo pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
Then the priest will take the basket from your hand and put it down in front of the altar of the Lord your God.
5 Ndipo mudzanenetsa pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, “Abambo anga anali Mwaramu woyendayenda, anapita ku Igupto ndi anthu ochepa nakhala kumeneko. Pambuyo pake anakhala mtundu waukulu, wamphamvu ndi wochuluka.
And these are the words which you will say before the Lord your God: My father was a wandering Aramaean, and he went down with a small number of people into Egypt; there he became a great and strong nation:
6 Koma Aigupto anatisautsa natizunza, kumatigwiritsa ntchito yakalavulagaga.
And the Egyptians were cruel to us, crushing us under a hard yoke:
7 Kenaka tinafuwulira Yehova, Mulungu wa makolo athu ndipo Yehova anamva mawu athu ndi kuona kusauka, kuvutika ndi kuponderezedwa kwathu.
And our cry went up to the Lord, the God of our fathers, and the Lord's ear was open to the voice of our cry, and his eyes took note of our grief and the crushing weight of our work:
8 Kotero Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndi mkono wotambasuka ndi zoopsa zazikulu ndi zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa.
And the Lord took us out of Egypt with a strong hand and a stretched-out arm, with works of power and signs and wonders:
9 Iye anatibweretsa ku malo ano natipatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi lino.
And he has been our guide to this place, and has given us this land, a land flowing with milk and honey.
10 Ndipo tsopano ndikubweretsa zipatso zoyamba zimene inu Yehova mwandipatsa.” Ikani dengulo pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kuwerama mopereka ulemu pamaso pake.
So now, I have come here with the first of the fruits of the earth which you, O Lord, have given me. Then you will put it down before the Lord your God and give him worship:
11 Ndipo inu ndi Alevi pamodzi ndi alendo okhala pakati panu mudzakondwera mʼzinthu zonse zabwino zimene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, inu ndi a pa banja panu.
And you will have joy in every good thing which the Lord your God has given to you and to your family; and the Levite, and the man from a strange land who is with you, will take part in your joy.
12 Mukatha kupatula chakhumi pa zonse zimene mwakolola mʼchaka chachitatu chimene ndi chaka chakhumi, muzichipereka kwa wansembe, mlendo, ana ndi akazi amasiye, kuti pamenepo adye mʼmizinda yanu nakhuta.
When you have taken out a tenth from the tenth of all your produce in the third year, which is the year when this has to be done, give it to the Levite, and the man from a strange land, and the child without a father, and the widow, so that they may have food in your towns and be full;
13 Kenaka munene kwa Yehova Mulungu wanu kuti “Ndatulutsamo mʼnyumba mwanga gawo lopatulika ndipo ndalipereka kwa Mlevi, mlendo, ana ndi akazi amasiye, monga mwa zonse zimene munalamula. Sindinapatuke pa zimene munalamula kapena kuyiwala ndi chimodzi chomwe.
And say before the Lord your God, I have taken all the holy things out of my house and have given them to the Levite, and the man from a strange land, and him who has no father, and the widow, as you have given me orders: I have kept in mind all your orders, in nothing have I gone against them:
14 Sindinadye kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndimalira maliro kapena kuchotsapo kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndinali wodetsedwa, kapena kuperekako nsembe kwa akufa kalikonse ka gawoli. Ine ndamvera Yehova Mulungu wanga, ndachita chilichonse chimene inu munandilamula.
No part of these things has been used for food in a time of weeping, or put away when I was unclean, or given for the dead: I have given ear to the voice of the Lord my God, and have done all you have given me orders to do.
15 Yangʼanani pa dziko kuchokera kumwamba, ku malo anu wopatulika, ndi kudalitsa anthu anu Aisraeli ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi limene mwatipatsa ife monga momwe munalonjezera pa malumbiro anu kwa makolo athu.”
So, looking down from your holy place in heaven, send your blessing on your people Israel and on the land which you have given us, as you said in your oath to our fathers, a land flowing with milk and honey.
16 Yehova Mulungu wanu akukulamulani lero lino kuti mutsate malangizo ndi malamulo ake ndipo muwasunge mosamalitsa ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Today the Lord your God gives you orders to keep all these laws and decisions: so then keep and do them with all your heart and all your soul.
17 Mwanena motsimikiza lero lino kuti Yehova ndiye Mulungu wanu ndi kuti mudzayenda mʼnjira zake, kusunga malangizo, malamulo ndi zonse akukulamulani ndi kutinso mudzamumvera.
Today you have given witness that the Lord is your God, and that you will go in his ways and keep his laws and his orders and his decisions and give ear to his voice:
18 Ndipo Yehova wanenetsa lero lino kuti inu ndinu anthu ake, chuma chake chamtengowapatali monga momwe analonjezera, ndipo mukuyenera kusunga malamulo ake onse.
And the Lord has made it clear this day that you are a special people to him, as he gave you his word; and that you are to keep all his orders;
19 Iye wanenetsa kuti adzakuyikani kukhala oyamikika, otchuka ndi olemekezeka koposa mitundu yonse imene anayilenga. Komanso mudzakhala anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu monga momwe analonjezera.
And that he will make you high over all the nations he has made, in praise, in name, and in honour, and that you are to be a holy people to the Lord your God as he has said.