< Deuteronomo 25 >

1 Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa.
Кад је распра међу људима па дођу на суд да им суде, тада правога нека оправдају, а кривога нека осуде.
2 Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake,
И ако криви заслужује бој, тада судија нека заповеди да га повале и бију пред њим, на број према кривици његовој.
3 koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu.
До четрдесет удараца нека заповеди да му ударе, не више, да се не би поништио брат твој у твојим очима, кад би му се ударило више удараца.
4 Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.
Немој завезати уста волу кад врше.
5 Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo.
Кад браћа живе заједно па умре један од њих без деце, онда жена умрлога да се не уда из куће за другог; брат његов нека отиде к њој и узме је за жену и учини јој дужност деверску.
6 Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli.
И први син ког она роди нека се назове именом брата његовог умрлог, да не погине име његово у Израиљу.
7 Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.”
Ако ли онај човек не би хтео узети снахе своје, онда снаха његова нека дође на врата пред старешине, и каже: Неће девер мој да подигне брату свом семе у Израиљу, неће да ми учини дужности деверске.
8 Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,”
Тада нека га дозову старешине места оног и разговоре се с њим; па ако се он упре и каже: Нећу да је узмем;
9 mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.”
Онда нека приступи к њему снаха његова пред старешинама, и нека му изује обућу с ноге његове и пљуне му у лице, и проговоривши нека каже: Тако ваља да буде човеку који неће да зида куће брата свог.
10 Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato.
И он нека се зове у Израиљу: Дом босога.
11 Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo,
Ако би се свадили људи, један с другим, па би дошла жена једног да отме мужа свог из руке другог који га бије, и пруживши руку своју ухватила би га за мошнице.
12 muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni.
Одсеци јој руку; нека не жали око твоје.
13 Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka.
Немој имати у торби својој двојаку меру, велику и малу.
14 Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono.
Немој имати у кући својој двојаку ефу, велику и малу.
15 Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Мера потпуна и права нека ти је; ефа потпуна и права нека ти је, да би ти се продужили дани твоји у земљи коју ти даје Господ Бог твој.
16 Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi.
Јер је гад пред Господом Богом твојим ко год чини тако, ко год чини криво.
17 Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto.
Опомињи се шта ти је учинио Амалик кад иђосте на путу кад иђасте из Мисира,
18 Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu.
Како те дочека на путу и поби на крају све уморне који иђаху за тобом, кад си био сустао и изнемогао, и не боја се Бога.
19 Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!
Зато кад те Господ Бог твој смири од свих непријатеља твојих унаоколо у земљи коју ти даје Господ Бог твој да је наследиш, тада затри спомен Амалику под небом; не заборави.

< Deuteronomo 25 >