< Deuteronomo 25 >

1 Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa.
Uba kukhona ukuxabana phakathi kwabantu, baye esahlulelweni, ukuthi babahlulele, bazalungisisa olungileyo, balahle olecala.
2 Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake,
Kuzakuthi-ke uba olecala efanele ukutshaywa, umahluleli uzamlalisa phansi, atshaywe phambi kwakhe, njengokulingene icala lakhe, ngokwenani.
3 koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu.
Angatshaywa imivimvinya engamatshumi amane, angengezeleli, hlezi nxa esedlule ukumtshaya okwedlula le ngemivimvinya eminengi, kuze kuthi umfowenu ayangeke emehlweni akho.
4 Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.
Ungayifaki isayeke inkabi nxa ibhula.
5 Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo.
Uba izelamani zihlala ndawonye, lomunye wazo esifa, engelandodana, umfazi wofileyo kangendeli kowemzini ongaphandle; umfowabo wendoda yakhe uzangena kuye, amthathe abe ngumkakhe, enze kuye imfanelo yomfowabo wendoda.
6 Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli.
Kuzakuthi-ke izibulo alizalayo lizakuma ebizweni lomfowabo ofileyo, ukuze ibizo lakhe lingacitshwa koIsrayeli.
7 Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.”
Uba umuntu engathandi ukuthatha umkamfowabo, umkamfowabo uzakwenyukela esangweni kubadala athi: Umfowabo wendoda yami uyala ukuvusela umfowabo ibizo koIsrayeli; kafuni ukwenza kimi imfanelo yomfowabo wendoda.
8 Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,”
Abadala bomuzi wakhe bazambiza-ke, bakhulume laye. Uba eqinisa esithi: Kangithandi ukumthatha;
9 mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.”
umkamfowabo uzasondela-ke kuye phambi kwamehlo abadala, akhuphe inyathela lakhe enyaweni lwakhe, amkhafulele ebusweni, aphendule, athi: Kuzakwenziwa njalo kulowomuntu ongayakhiyo indlu yomfowabo.
10 Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato.
Lebizo lakhe lizakuthiwa koIsrayeli: Indlu yolenyathela elakhutshwayo.
11 Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo,
Nxa amadoda esilwa, omunye lomunye, kusondele umfazi wenye ukuthi ayikhulule indoda yakhe esandleni soyitshayayo, elule isandla sakhe ayibambe ngamaphambili,
12 muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni.
usiqume isandla sakhe, ilihlo lakho lingabi lasihawu.
13 Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka.
Ungabi lamatshe okulinganisa ehlukeneyo esikhwameni sakho, elikhulu lelincinyane.
14 Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono.
Ungabi lama-efa ehlukeneyo endlini yakho, esikhulu lesincinyane.
15 Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Woba lelitshe lokulinganisa elipheleleyo lelilungileyo, woba le-efa epheleleyo lelungileyo, ukuze insuku zakho zelulwe elizweni iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona.
16 Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi.
Ngoba wonke owenza izinto ezinje, wonke owenza ukungalungi, uyisinengiso eNkosini uNkulunkulu wakho.
17 Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto.
Khumbula lokho uAmaleki akwenza kuwe endleleni ekuphumeni kwenu eGibhithe,
18 Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu.
ukuthi wakuhlangabeza endleleni, watshaya phakathi kwakho ababebuthakathaka emva kwakho, usudiniwe usuphele amandla; kanti kamesabanga uNkulunkulu.
19 Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!
Ngakho kuzakuthi, nxa iNkosi uNkulunkulu wakho isikuphumuzile kuzo zonke izitha zakho inhlangothi zonke, elizweni iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona libe yilifa ukudla ilifa lalo, uzakwesula ukukhunjulwa kukaAmaleki ngaphansi kwamazulu; ungakhohlwa.

< Deuteronomo 25 >