< Deuteronomo 25 >

1 Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa.
If there be a controversy between men, and they come nigh unto a court of justice, and they judge them; and they justify the righteous, and condemn the wicked:
2 Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake,
Then shall it be, if the guilty man deserve to be beaten, that the judge shall cause him to lie down, and to be beaten before his face, according to the degree of his fault, by a [certain] number.
3 koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu.
Forty stripes may he give him, not more; so that he shall not exceed to have him beaten above these with too many stripes, and thy brother be thus rendered vile before thy eyes.
4 Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.
Thou shalt not muzzle the ox when he thresheth out the corn.
5 Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo.
If brothers dwell together, and one of them die, and have no child: then shall the wife of the dead not be married abroad, unto a stranger; her husband's brother shall go in unto her, and take her to himself for wife, and perform the duty of a husband's brother unto her.
6 Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli.
And it shall be, that the first-born whom she may bear shall succeed in the name of his brother who is dead; so that his name be not blotted out of Israel.
7 Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.”
And if the man have no desire to take his sister-in-law: then shall his sister-in-law go up to the gate unto the elders, and say, My husband's brother refuseth to raise up unto his brother a name in Israel, he will not perform on me the duty of a husband's brother.
8 Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,”
Then shall the elders of his city call him, and speak unto him; and if he persist, and say, I have no desire to take her:
9 mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.”
Then shall his sister-in-law come nigh unto him in the presence of the elders, and pull his shoe from off his foot, and spit out before him, and shall commence and say, Thus shall be done unto that man that will not build up his brother's house.
10 Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato.
And his name shall be called in Israel, The house of the barefooted.
11 Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo,
When men strive together one with the other, and the wife of the one draweth near to deliver her husband out of the hand of him that smiteth him, and putteth forth her hand, and taketh him by the secrets:
12 muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni.
Then shalt thou cut off her hand, thy eye shall not have pity.
13 Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka.
Thou shalt not have in thy bag divers weights, a great and a small.
14 Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono.
Thou shalt not have in thy house divers measures, a great and a small.
15 Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
A perfect and just weight shalt thou have, a perfect and just measure shalt thou have; in order that thy days may be prolonged in the land which the Lord thy God giveth thee;
16 Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi.
For an abomination of the Lord thy God is every one that doth such things, every one that acteth unrighteously.
17 Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto.
Remember what 'Amalek did unto thee, by the way, at your coming forth out of Egypt;
18 Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu.
How he met thee by the way, and smote the hindmost of thee, all that were feeble behind thee, when thou was faint and weary; and he feared not God.
19 Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!
And it shall come to pass, when the Lord thy God giveth thee rest from all thy enemies round about, in the land which the Lord thy God giveth thee for an inheritance to possess it, that thou shalt blot out the remembrance of 'Amalek from under the heavens: thou shalt not forget.

< Deuteronomo 25 >