< Deuteronomo 24 >

1 Ngati mwamuna wakwatira mkazi amene sakukondwera naye chifukwa wapeza vuto pa mkaziyo, namulembera mkaziyo kalata ya chisudzulo, namupatsa ndi kumutulutsa mʼnyumba mwake,
Uba indoda ithatha umfazi, imgane, kuzakuthi nxa engatholi umusa emehlweni ayo, ngoba ifice kuye into elihlazo, kayimbhalele incwadi yesehlukaniso, ifake esandleni sakhe, imkhuphe endlini yayo.
2 mkaziyo ndi kukakwatiwa ndi mwamuna wina,
Nxa esephumile endlini yayo, angahamba, ayekuba ngowenye indoda.
3 ndipo mwamuna wachiwiriyo nʼkuyipidwa nayenso ndi kumulemberanso kalata ya chisudzulo nʼkumutulutsa mʼnyumba mwake, kapena ngati mwamunayo amwalira,
Uba lindoda elandelayo imzonda, imbhalele incwadi yesehlukaniso, iyifake esandleni sakhe, imkhiphe endlini yayo; loba lindoda elandelayo isifa ebimthethe waba ngumkayo,
4 mwamuna wake woyamba uja, amene anamuleka saloledwanso kumukwatira kachiwiri popeza mkaziyo wadetsedwa. Chimenechi ndi chonyansa pamaso pa Yehova. Musalowetse tchimo mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu.
indoda yakhe yokuqala eyamkhiphayo ingemthathe futhi abe ngumkayo, emva kokuba esengcolisiwe; ngoba kuyisinengiso phambi kweNkosi. Ngakho kawuyikwenza ilizwe lone iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona ukuba yilifa.
5 Mwamuna akangokwatira kumene asamatumizidwe ku nkhondo kapena kupatsidwa ntchito ina iliyonse. Kwa chaka chathunthu akhale ndi ufulu wokhala pa khomo pake kumasangalatsa mkazi wakeyo.
Nxa indoda ithethe umfazi omutsha kayiyikuphuma impi, futhi kayiyikuphathiswa laloba yiwuphi umsebenzi; izakuba sekhaya ikhululekile umnyaka owodwa ukuze ithokozise umkayo emthetheyo.
6 Munthu akakhala nanu ndi ngongole musamutengere mwala wake wa mphero ngati chikole, chifukwa kutero nʼkumutengera moyo kukhala chikole cha ngongole.
Kakungabi khona ozathatha ilitshe lokucholela loba imbokodo ukuze kube yisibambiso; ngoba uthatha impilo ibe yisibambiso.
7 Ngati munthu agwidwa akuba mʼbale wake wa Chiisraeli namamuzunza ngati kapolo kapena kumugulitsa, wogulitsa mnzakeyo ayenera kuphedwa. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
Uba umuntu eficwa eseba umuntu kubafowabo ebantwaneni bakoIsrayeli, amphathe njengesigqili kumbe amthengise, lelosela lizakufa. Ngalokhu uzakhupha ububi phakathi kwakho.
8 Pakagwa matenda a khate, samalitsani kuchita zonse zimene ansembe, amene ndi Alevi, anakulangizani. Mutsatire mosamalitsa zimene ndinawalamula.
Qaphela esifeni sobulephero, ukunanzelelisisa wenze njengakho konke abapristi abangamaLevi abakufundisa khona; njengalokhu ngabalaya, nanzelelani ukukwenza.
9 Kumbukirani zimene Yehova Mulungu wanu anachita kwa Miriamu muli paulendo mutatuluka mu Igupto.
Khumbula lokho iNkosi uNkulunkulu wakho eyakwenza kuMiriyamu endleleni ekuphumeni kwenu eGibhithe.
10 Ukabwereketsa mnzako kanthu kena kalikonse, usalowe mʼnyumba mwake kukatenga chimene wachipereka ngati chikole.
Nxa useboleka umakhelwane wakho ulutho, ungangeni endlini yakhe ukuthi uthathe isibambiso sakhe.
11 Uziyima kunja kwa nyumba kuti munthu amene wamubwereketsa kanthuyo akubweretsere kunja komweko.
Uzakuma phandle, lomuntu omebolekayo akukhuphele isibambiso phandle.
12 Ngati munthuyo ndi wosauka, usamutengere chikolecho mpaka kukagona nacho kwanu.
Njalo uba umuntu engumyanga, ungalali lesibambiso sakhe;
13 Pomalowa dzuwa ukhale utamubwezera mkanjo wakewo kuti akafunde. Pamenepo adzakuthokoza, ndipo amenewa adzawerengedwa ngati machitidwe olungama kwa iweyo pamaso pa Yehova Mulungu wako.
uzabuyisela lokubuyisela isibambiso kuye lapho ilanga litshona, ukuze alale ngesembatho sakhe, akubusise; lalokho kuzakuba yikulunga kuwe phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho.
14 Osamapezera mwayi pa anthu aganyu osauka ndi aumphawi, kaya ndi Mwisraeli kapena mlendo wokhala mu umodzi mwa mizinda yanu.
Ungacindezeli inceku eqhatshiweyo engumyanga leswelayo, ingowabafowenu loba ingowezizweni oselizweni lakini phakathi kwamasango akho.
15 Mumulipire malipiro ake a tsiku dzuwa lisanalowe chifukwa ndi wosauka ndipo akudalira malipirowo. Kupanda kutero adzakudandaulirani kwa Yehova ndipo mudzapezeka ochimwa.
Uzanika iholo layo ngosuku lwayo, lelanga kalingatshoni phezu kwalo, ngoba ingumyanga, ibeke inhliziyo yayo kulo; ukuze ingakhali eNkosini ngawe, njalo kube yisono kuwe.
16 Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.
Oyise kabayikubulawa ngenxa yabantwana, labantwana kabayikubulawa ngenxa yaboyise; ngulowo lalowo uzabulawa ngenxa yesakhe isono.
17 Musachitire mlendo kapena mwana wamasiye zoyipa, kapena kulanda mkazi wamasiye chovala ngati chikole cha ngongole.
Ungaphambuli isahlulelo sowemzini lentandane; ungathathi isembatho somfelokazi sibe yisibambiso;
18 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwombolani kumeneko. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.
kodwa ukhumbule ukuthi wawuyisigqili eGibhithe, leNkosi uNkulunkulu wakho yakuhlenga khona; ngakho ngiyakulaya ukuthi wenze lolulutho.
19 Mukamakolola mʼmunda mwanu ndipo zokolola zina zikasiyidwa, musamabwerere kukazitola. Muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochita zanu zonse.
Nxa uvuna isivuno sakho ensimini yakho, ukhohlwe isithungo ensimini, ungabuyeli ukusithatha; sizakuba ngesowemzini, esentandane lesomfelokazi; ukuze iNkosi uNkulunkulu wakho ikubusise emsebenzini wonke wezandla zakho.
20 Mukathyola zipatso mu mtengo wa olivi, musamabwererenso kachiwiri ku mtengo womwewo. Zotsalazo zilekereni alendo, ana ndi akazi amasiye.
Nxa uvuthuza isihlahla sakho somhlwathi, ungayihlola izingatsha emva kwakho; kuzakuba ngokowemzini lokwentandane lokomfelokazi.
21 Mukakolola mphesa mʼmunda mwanu musamabwereremonso kachiwiri. Zotsalazo muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye.
Nxa usuvunile izithelo zesivini sakho, ungakhothozi emva kwakho; kuzakuba ngokowemzini lokwentandane lokomfelokazi.
22 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.
Uzakhumbula ukuthi wawuyisigqili elizweni leGibhithe; ngakho ngiyakulaya ukwenza lolulutho.

< Deuteronomo 24 >