< Deuteronomo 24 >
1 Ngati mwamuna wakwatira mkazi amene sakukondwera naye chifukwa wapeza vuto pa mkaziyo, namulembera mkaziyo kalata ya chisudzulo, namupatsa ndi kumutulutsa mʼnyumba mwake,
Quand un homme aura pris une femme et l'aura épousée, si elle ne trouve pas grâce à ses yeux, parce qu'il aura trouvé en elle quelque chose de honteux, il lui écrira une lettre de divorce, la lui mettra dans la main, et la renverra de sa maison.
2 mkaziyo ndi kukakwatiwa ndi mwamuna wina,
Et si, étant sortie de sa maison, elle s'en va et devient la femme d'un autre homme,
3 ndipo mwamuna wachiwiriyo nʼkuyipidwa nayenso ndi kumulemberanso kalata ya chisudzulo nʼkumutulutsa mʼnyumba mwake, kapena ngati mwamunayo amwalira,
Si ce dernier mari la hait, lui écrit une lettre de divorce, la lui met dans la main, et la renvoie de sa maison; ou si ce dernier mari, qui l'avait prise pour femme, meurt,
4 mwamuna wake woyamba uja, amene anamuleka saloledwanso kumukwatira kachiwiri popeza mkaziyo wadetsedwa. Chimenechi ndi chonyansa pamaso pa Yehova. Musalowetse tchimo mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu.
Son premier mari, qui l'avait renvoyée, ne pourra pas la reprendre pour femme après qu'elle a été souillée; car ce serait une abomination devant l'Éternel, et tu ne chargeras point de péché le pays que l'Éternel ton Dieu te donne en héritage.
5 Mwamuna akangokwatira kumene asamatumizidwe ku nkhondo kapena kupatsidwa ntchito ina iliyonse. Kwa chaka chathunthu akhale ndi ufulu wokhala pa khomo pake kumasangalatsa mkazi wakeyo.
Quand un homme aura nouvellement pris femme, il n'ira point à la guerre, et on ne lui imposera aucune charge; pendant un an il en sera exempt pour sa famille, et il réjouira la femme qu'il aura prise.
6 Munthu akakhala nanu ndi ngongole musamutengere mwala wake wa mphero ngati chikole, chifukwa kutero nʼkumutengera moyo kukhala chikole cha ngongole.
On ne prendra point pour gage les deux meules, ni la meule de dessus; car ce serait prendre pour gage la vie de son prochain.
7 Ngati munthu agwidwa akuba mʼbale wake wa Chiisraeli namamuzunza ngati kapolo kapena kumugulitsa, wogulitsa mnzakeyo ayenera kuphedwa. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
Quand on trouvera un homme qui aura dérobé quelqu'un de ses frères, des enfants d'Israël, et l'aura fait esclave ou vendu, ce larron mourra; et tu ôteras le méchant du milieu de toi.
8 Pakagwa matenda a khate, samalitsani kuchita zonse zimene ansembe, amene ndi Alevi, anakulangizani. Mutsatire mosamalitsa zimene ndinawalamula.
Prends garde à la plaie de la lèpre, pour bien observer et pour faire tout ce que les sacrificateurs, de la race de Lévi, vous enseigneront; vous prendrez garde à faire comme je leur ai commandé.
9 Kumbukirani zimene Yehova Mulungu wanu anachita kwa Miriamu muli paulendo mutatuluka mu Igupto.
Souviens-toi de ce que l'Éternel ton Dieu fit à Marie dans le chemin, quand vous sortiez d'Égypte.
10 Ukabwereketsa mnzako kanthu kena kalikonse, usalowe mʼnyumba mwake kukatenga chimene wachipereka ngati chikole.
Quand tu prêteras quelque chose à ton prochain, tu n'entreras point dans sa maison pour prendre son gage;
11 Uziyima kunja kwa nyumba kuti munthu amene wamubwereketsa kanthuyo akubweretsere kunja komweko.
Tu te tiendras dehors, et l'homme à qui tu prêtes t'apportera le gage dehors.
12 Ngati munthuyo ndi wosauka, usamutengere chikolecho mpaka kukagona nacho kwanu.
Et si c'est un homme pauvre, tu ne te coucheras point ayant encore son gage.
13 Pomalowa dzuwa ukhale utamubwezera mkanjo wakewo kuti akafunde. Pamenepo adzakuthokoza, ndipo amenewa adzawerengedwa ngati machitidwe olungama kwa iweyo pamaso pa Yehova Mulungu wako.
Tu ne manqueras pas de lui rendre le gage, au coucher du soleil, afin qu'il couche dans son vêtement, et qu'il te bénisse; et cela te sera imputé à justice devant l'Éternel ton Dieu.
14 Osamapezera mwayi pa anthu aganyu osauka ndi aumphawi, kaya ndi Mwisraeli kapena mlendo wokhala mu umodzi mwa mizinda yanu.
Tu ne feras point tort au mercenaire pauvre et indigent, d'entre tes frères ou d'entre les étrangers qui demeurent dans ton pays, dans tes portes.
15 Mumulipire malipiro ake a tsiku dzuwa lisanalowe chifukwa ndi wosauka ndipo akudalira malipirowo. Kupanda kutero adzakudandaulirani kwa Yehova ndipo mudzapezeka ochimwa.
Tu lui donneras son salaire, le jour même, avant que le soleil se couche; car il est pauvre, et son âme s'y attend; de peur qu'il ne crie contre toi à l'Éternel, et qu'il n'y ait du péché en toi.
16 Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.
On ne fera point mourir les pères pour les enfants; on ne fera point non plus mourir les enfants pour les pères; on fera mourir chacun pour son péché.
17 Musachitire mlendo kapena mwana wamasiye zoyipa, kapena kulanda mkazi wamasiye chovala ngati chikole cha ngongole.
Tu ne pervertiras point le droit d'un étranger, ni d'un orphelin, et tu ne prendras point pour gage le vêtement d'une veuve.
18 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwombolani kumeneko. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.
Et tu te souviendras que tu as été esclave en Égypte, et que l'Éternel ton Dieu t'a racheté de là. C'est pourquoi, je te commande de faire ces choses.
19 Mukamakolola mʼmunda mwanu ndipo zokolola zina zikasiyidwa, musamabwerere kukazitola. Muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochita zanu zonse.
Quand tu feras ta moisson dans ton champ, et que tu y auras oublié une poignée d'épis, tu ne retourneras point pour la prendre; elle sera pour l'étranger, pour l'orphelin et pour la veuve, afin que l'Éternel ton Dieu te bénisse dans toutes les œuvres de tes mains.
20 Mukathyola zipatso mu mtengo wa olivi, musamabwererenso kachiwiri ku mtengo womwewo. Zotsalazo zilekereni alendo, ana ndi akazi amasiye.
Quand tu secoueras tes oliviers, tu n'y retourneras point pour examiner branche après branche; ce qui restera sera pour l'étranger, pour l'orphelin et pour la veuve.
21 Mukakolola mphesa mʼmunda mwanu musamabwereremonso kachiwiri. Zotsalazo muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye.
Quand tu vendangeras ta vigne, tu n'y feras pas grappiller après toi; ce qui restera sera pour l'étranger, pour l'orphelin et pour la veuve.
22 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.
Et tu te souviendras que tu as été esclave au pays d'Égypte; c'est pourquoi, je te commande de faire cela.