< Deuteronomo 23 >
1 Mwamuna aliyense wofulidwa kapena woduka chiwalo chachimuna asalowe nawo mu msonkhano wa Yehova.
He that is crushed or maimed in his privy parts shall not enter into the assembly of the LORD.
2 Aliyense wobadwa mʼbanja losavomerezeka, kapena mdzukulu wake wina aliyense, ngakhale mibado khumi pambuyo pake, asalowe mu msonkhano wa Yehova.
A bastard shall not enter into the assembly of the LORD; even to the tenth generation shall none of his enter into the assembly of the LORD.
3 Mwamoni kapena Mmowabu asalowe mu msonkhano wa anthu a Yehova ngakhale mibado khumi yobwera pambuyo pake.
An Ammonite or a Moabite shall not enter into the assembly of the LORD; even to the tenth generation shall none of them enter into the assembly of the LORD for ever;
4 Pakuti iwowa sanabwere kudzakulonjerani ndi chakudya kapena madzi pamene mumadutsa pochokera ku Igupto, mʼmalo mwake anakalemba ganyu Balaamu mwana wa Beori wochokera ku Petori ku Mesopotamiya kuti akutemberereni.
because they met you not with bread and with water in the way, when ye came forth out of Egypt; and because they hired against thee Balaam the son of Beor from Pethor of Aram-naharaim, to curse thee.
5 Komabe Yehova Mulungu wanu sanamvere Balaamu koma anatembenuza temberero kukhala dalitso kwa inu chifukwa Yehova Mulungu wanu amakukondani.
Nevertheless the LORD thy God would not hearken unto Balaam; but the LORD thy God turned the curse into a blessing unto thee, because the LORD thy God loved thee.
6 Musachite nawo mgwirizano uliwonse wa mtendere pa moyo wanu wonse.
Thou shalt not seek their peace nor their prosperity all thy days for ever.
7 Musapeputse Mwedomu pakuti ndi mʼbale wanu ndithu. Musapeputse Mwigupto chifukwa munali alendo mʼdziko lake.
Thou shalt not abhor an Edomite, for he is thy brother; thou shalt not abhor an Egyptian, because thou wast a stranger in his land.
8 Mʼbado wachitatu wa ana awo akhoza kulowa mu msonkhano wa anthu a Yehova.
The children of the third generation that are born unto them may enter into the assembly of the LORD.
9 Mukamakhala pa msasa pokonzekera adani anu, musayandikane ndi china chilichonse chodetsedwa.
When thou goest forth in camp against thine enemies, then thou shalt keep thee from every evil thing.
10 Wina mwa asilikali anu akadziwonongera ndi umuna usiku, ayenera kuchoka pa msasapo ndipo akhale kunja kwa msasa.
If there be among you any man, that is not clean by reason of that which chanceth him by night, then shall he go abroad out of the camp, he shall not come within the camp.
11 Koma dzuwa likapendeka ayenera kusamba ndipo polowa dzuwa akhoza kubwerera ku msasa.
But it shall be, when evening cometh on, he shall bathe himself in water; and when the sun is down, he may come within the camp.
12 Mukonze malo kunja kwa msasa kumene mukhoza kukadzithandizirako.
Thou shalt have a place also without the camp, whither thou shalt go forth abroad.
13 Pakati pa zida zanu muzikhala ndi china chokumbira, ndipo pokadzithandiza muzikumba kadzenje ndi kukwirira chimbudzi chanu.
And thou shalt have a paddle among thy weapons; and it shall be, when thou sittest down abroad, thou shalt dig therewith, and shalt turn back and cover that which cometh from thee.
14 Pakuti Yehova Mulungu wanu amayendayenda ku msasa wanu kukutchinjirizani ndi kupereka adani anu kwa inu. Nʼchifukwa chake msasa wanu uzikhala wopatulika kuti mwina angaone china chonyansa nabwerera osakuyandikirani.
For the LORD thy God walketh in the midst of thy camp, to deliver thee, and to give up thine enemies before thee; therefore shall thy camp be holy; that He see no unseemly thing in thee, and turn away from thee.
15 Ngati kapolo wathawa mbuye wake nakabisala kwanu, musamuperekenso kwa mbuye wakeyo.
Thou shalt not deliver unto his master a bondman that is escaped from his master unto thee;
16 Mumulole akhale pakati panu, paliponse pamene angakonde, mʼmudzi umene angasankhe ndipo musamupondereze.
he shall dwell with thee, in the midst of thee, in the place which he shall choose within one of thy gates, where it liketh him best; thou shalt not wrong him.
17 Pasapezeke Mwisraeli wamwamuna kapena wamkazi wochita chiwerewere ku Nyumba ya Mulungu.
There shall be no harlot of the daughters of Israel, neither shall there be a sodomite of the sons of Israel.
18 Musabweretse malipiro a wachiwerewere wamkazi kapena wamwamuna Mʼnyumba ya Yehova Mulungu wanu kudzapereka za malumbiro aliwonse, chifukwa Yehova Mulungu wanu amadana ndi zimenezi.
Thou shalt not bring the hire of a harlot, or the price of a dog, into the house of the LORD thy God for any vow; for even both these are an abomination unto the LORD thy God.
19 Musamalipitse mʼbale wanu chiwongoladzanja, kaya pa ndalama, kapena pa chakudya, kapena pa china chilichonse choti nʼkupereketsa chiwongoladzanja.
Thou shalt not lend upon interest to thy brother: interest of money, interest of victuals, interest of any thing that is lent upon interest.
20 Mlendo mukhoza kumulipitsa chiwongoladzanja koma osati mʼbale wanu Mwisraeli, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochitika zanu zonse mʼdziko mukulowamoli.
Unto a foreigner thou mayest lend upon interest; but unto thy brother thou shalt not lend upon interest; that the LORD thy God may bless thee in all that thou puttest thy hand unto, in the land whither thou goest in to possess it.
21 Mukalumbira kupereka kanthu kwa Yehova Mulungu wanu, musamachedwetse kupereka, chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakufunsanibe kanthuko ndipo mudzapezeka wochimwa.
When thou shalt vow a vow unto the LORD thy God, thou shalt not be slack to pay it; for the LORD thy God will surely require it of thee; and it will be sin in thee.
22 Koma ngati mupewa kupanga mapangano simudzapezeka ochimwa.
But if thou shalt forbear to vow, it shall be no sin in thee.
23 Zilizonse zimene mulumbira ndi pakamwa panu muzitsimikiza kuzichita, chifukwa mwalumbira mwaufulu pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi pakamwa panu.
That which is gone out of thy lips thou shalt observe and do; according as thou hast vowed freely unto the LORD thy God, even that which thou hast promised with thy mouth.
24 Mukalowa mʼmunda wamphesa wa mnzanu mukhoza kudya mphesa mmene mungafunire koma musayike zina mʼdengu mwanu.
When thou comest into thy neighbour's vineyard, then thou mayest eat grapes until thou have enough at thine own pleasure; but thou shalt not put any in thy vessel.
25 Mukalowa mʼmunda wa tirigu wa mʼbale wanu, mukhoza kutengako ngala mʼmanja mwanu, koma osasenga tirigu ndi chikwakwa.
When thou comest into thy neighbour's standing corn, then thou mayest pluck ears with thy hand; but thou shalt not move a sickle unto thy neighbour's standing corn.