< Deuteronomo 22 >

1 Ngati uwona ngʼombe kapena nkhosa ya mʼbale wako ikusochera, usayilekerere koma uyesetse kuyibwezera kwa iye.
“If you see some Israeli’s ox or sheep that has strayed away, do not act as though you did not see it. Take it back [to its owner].
2 Ngati mʼbale wakoyo sakhala pafupi kapena sukudziwa kuti ndi yandani, uyitengere ku nyumba kwako ndi kuyisamala mpaka mwini wake atayilondola ndipo umubwezere.
But if the owner does not live near you, or if you do not know who the owner is, take the animal to your house. [It can stay with you] until the owner comes, searching for it. Then you must give the animal to him.
3 Uzitero ndithu ngati upeza bulu kapena mkanjo kapena chilichonse chimene chatayika. Osachilekerera.
You must do the same thing if you see a donkey, or a piece of clothing, or anything else that someone has lost. Do not refuse to do what you should do.
4 Ngati wapeza bulu kapena ngʼombe ya mʼbale wako itagwa panjira, usayilekerere. Ithandize kuti idzuke.
“And if you see a fellow Israeli’s donkey or cow that has fallen down on the road, do not act as though you did not see it. Help the owner to lift the animal up [so that it can stand on its feet again].
5 Akazi asavale zovala za amuna, kapena mwamuna kuvala zovala za akazi, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita izi.
“Women must not wear men’s clothes, and men must not wear women’s clothes. Yahweh our God hates people who do things like that.
6 Ukapeza chisa cha mbalame mʼmphepete mwa msewu, kaya ndi mu mtengo kapena pansi, mbalame yayikazi itafungatira ana kapena mazira, usatenge mbalameyo pamodzi ndi ana ake omwe.
“If you happen to find a bird’s nest in a tree or on the ground, and the mother bird is sitting in the nest on its eggs or with the baby birds, do not take the mother bird [and kill it].
7 Anawo mukhoza kutenga koma onetsetsani kuti mayi wawo mwamutaya kuti apite, kuti zinthu zizikuyenderani bwino ndiponso kuti mukhale ndi moyo wautali.
You are permitted to take the baby birds, but you must allow the mother bird to fly away. Do this in order that things will go well for you and that you will live for a long time.
8 Mukamanga nyumba yatsopano, mutchingire khonde lake la pa denga kuti inu musapezeke ndi mlandu wopha munthu ngati wina agwa kuchokera pa khonde la pa dengalo.
“If you build a new house, you must put a (railing/low wall) around the edge of the roof. If you do that, and if someone falls off the roof [and dies], (you will not be guilty of causing that person to die/his death [MTY] will not be your fault).
9 Musadzale mbewu zamitundu iwiri mʼmunda wanu wa mpesa, ngati mutero, si mbewu zanu zokha zimene zidzakhale zodetsedwa, komanso zipatso za mʼmunda wamphesawo.
“Do not plant any crop in the area where your grapevines are growing. If you do, you are not allowed to harvest the crops that you have planted or to harvest the grapes [to make wine from them].
10 Musatipule pogwiritsa ntchito ngʼombe ndi bulu pa goli limodzi.
“Do not hitch together an ox and a donkey [for plowing your fields].
11 Musamavale chovala chopangidwa mophatikiza ubweya ndi thonje.
“Do not wear clothing that is made by weaving together (wool and linen/two different kinds of thread).
12 Muzipanga mphonje mʼngodya za mkanjo umene mumavala.
“[Twist threads together to] make tassels and sew/fasten them on the four bottom corners of your cloak.
13 Ngati munthu akwatira mkazi, ndipo atagona naye nʼkusamufunanso
“Suppose a man marries a young woman and has sex with her and later decides that he does not want her any more,
14 namunyoza ndi kumuyipitsira dzina nʼkumati, “Ine ndinakwatira mkazi uyu, koma pamene ndinakhala naye, sindinachione chizindikiro cha unamwali wake,”
and he says false things about her, and claims that she was not a virgin when he married her.
15 zikatero abambo ndi amayi ake ayenera kubweretsa chitsimikizo chakuti anali namwali kwa akuluakulu a mzinda ku chipata.
If that happens, the young woman’s parents must take the sheet that was on the bed when that man and their daughter were married, which still has bloodstains on it, and show it to the elders of the city at the (gate of/central meeting place in) the city.
16 Abambo ake a mtsikanayo adzanene kwa akuluakuluwo kuti, “Ine ndinamupatsa munthu uyu mwana wanga wamkazi kuti amukwatire, koma sakumufunanso.
Then the father of the young woman must say to the elders, ‘I gave my daughter to this man to be his wife. But now he says that he doesn’t want her any more.
17 Tsopano wamunyoza ndipo wanena kuti, ‘Ine sindinapeze kuti mwana wanu wamkaziyu ndi namwali.’ Koma tsopano onani chitsimikizo ichi cha unamwali wa mwana wanga wamkazi.” Kenaka makolo a mtsikanayo adzaonetse kansalu kwa akuluakulu aja,
And he has falsely said that she was not a virgin when he married her. But look! Here is what proves that my daughter was a virgin! Look at the bloodstains on the sheet where they slept the night that they were married!’ And he will show the sheet to the elders.
18 ndipo akuluakuluwo adzamugwire munthuyo namupatsa chilango.
Then the elders of that city must take that man and whip him.
19 Iwo adzamulipitse ndalama zasiliva zokwana 100 nazipereka kwa abambo a mtsikana, chifukwa munthu uyu wayipitsa dzina la mtsikana wa Chiisraeli. Ayenera kukhalabe mkazi wake ndipo asadzamuleke moyo wake wonse.
They shall require that he pay a fine of 100 pieces of silver and give the money to the father of the young woman, because the man caused an Israeli young woman to be disgraced. Also, that woman must continue to live with him; she is his wife. He is not allowed to divorce her during the rest of his life.
20 Koma ngati zomunenerazo ndi zoona, ndipo kuti chitsimikizo cha unamwali wa mtsikanayo sichinapezeke,
“But if what the man said is true, and there is nothing to prove that she was a virgin when he married her,
21 iyeyu ayenera kumutengera pa khomo pa abambo ake pamene anthu a mu mzinda wake akamuphere ndi miyala. Iyeyo wachita chinthu chochititsa manyazi mu Israeli pochita chiwerewere akanali pa khomo pa abambo ake. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu.
they must take that young woman to the door of her father’s house. Then the men of that city must execute her by throwing stones at her. They must do that because she has done something in Israel that is very disgraceful, by having sex with some man [while she was still living] in her father’s house. By executing her like that, you will get rid of this evil practice among you.
22 Ngati munthu apezeka akugona ndi mkazi wa mwini wake, ayenera kuphedwa munthuyo pamodzi ndi mkazi yemwe wagona nayeyo. Muyenera kuchotsa zoyipa mu Israeli.
“If a man is caught while he is having sex with another man’s wife, both of them must be executed. By doing that, you will get rid of this evil practice in Israel.
23 Ngati munthu mu mzinda akumana ndi mkazi yemwe anachita kale chinkhoswe nagona naye,
“Suppose in some town a man sees a young woman who is engaged/promised to be married to another man, and he is caught having sex with [EUP] her.
24 muwatengere awiriwo ku chipata cha mzinda ndi kuwapha ndi miyala. Aphedwe chifukwa mtsikanayo anali pafupi ndi anthu ndipo sanakuwe kuti ena amuthandize ndipo mwamunayo chifukwa anayipitsa mkazi wa mwini. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
You must take both of them to the (gate of/central meeting place in) that town. There you must execute them both by throwing stones at them. You must execute the young woman because she did not shout for help even though she was in the town. And the man must be executed because he had sex [EUP] with someone who was already engaged/promised to be married. By doing that, you will get rid of this evil practice among you.
25 Koma ngati munthu akumana ndi mkazi kutchire yemwe anachita kale chinkhoswe namugwiririra, mwamuna yekhayo ndiye woyenera kuphedwa.
“But suppose out in the open countryside a man meets a young woman who is engaged/promised to be married, and he rapes her. If that happens, only that man must be executed.
26 Mtsikanayo musamuchite chilichonse, palibe tchimo limene wachita loti ayenera kuphedwa. Mlandu uwu ufanana ndi wa munthu amene alimbana ndi kupha mnzake woyandikana naye,
You must not punish the young woman, because she did not do anything for which she deserves to be executed. This case is like when one man attacks another man [in the countryside] and murders him,
27 pakuti mwamunayo anamupeza mtsikanayo kutchire, ndipo ngakhale mtsikana wachinkhosweyo anakuwa, panalibe anamulanditsa.
because the man who raped her saw her when she was in the open countryside, and even though she called out for help, there was no one there who could rescue her.
28 Ngati munthu apezana ndi namwali woti sanachite chinkhoswe, namugwiririra, munthuyo nʼkupezeka,
“If a man rapes a young woman who is not engaged/promised to be married, if someone sees him while he is doing that,
29 ayenera kuwalipira abambo ake a namwaliyo ndalama za siliva makumi asanu. Iye ayenera kumukwatira mkaziyo chifukwa wamuyipitsa, ndipo sadzamulekanso moyo wake wonse.
that man must pay 50 pieces of silver to the young woman’s father, and he must marry her, because he forced her to have sex with him. He is not allowed to divorce her for the rest of his life.
30 Munthu asakwatire mkazi wa abambo ake pakuti ayenera kuchitira ulemu pogona pa abambo ake.
“man must not disgrace his father by having sex with any of his father’s wives.”

< Deuteronomo 22 >