< Deuteronomo 22 >

1 Ngati uwona ngʼombe kapena nkhosa ya mʼbale wako ikusochera, usayilekerere koma uyesetse kuyibwezera kwa iye.
You shall not see your brother's ox or his sheep go astray, and hide yourself from them: you shall surely bring them again to your brother.
2 Ngati mʼbale wakoyo sakhala pafupi kapena sukudziwa kuti ndi yandani, uyitengere ku nyumba kwako ndi kuyisamala mpaka mwini wake atayilondola ndipo umubwezere.
If your brother isn't near to you, or if you do not know him, then you shall bring it home to your house, and it shall be with you until your brother seek after it, and you shall restore it to him.
3 Uzitero ndithu ngati upeza bulu kapena mkanjo kapena chilichonse chimene chatayika. Osachilekerera.
So you shall do with his donkey; and so you shall do with his garment; and so you shall do with every lost thing of your brother's, which he has lost, and you have found: you may not hide yourself.
4 Ngati wapeza bulu kapena ngʼombe ya mʼbale wako itagwa panjira, usayilekerere. Ithandize kuti idzuke.
You shall not see your brother's donkey or his ox fallen down by the way, and hide yourself from them: you shall surely help him to lift them up again.
5 Akazi asavale zovala za amuna, kapena mwamuna kuvala zovala za akazi, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita izi.
A woman shall not wear men's clothing, neither shall a man put on women's clothing; for whoever does these things is an abomination to the LORD your God.
6 Ukapeza chisa cha mbalame mʼmphepete mwa msewu, kaya ndi mu mtengo kapena pansi, mbalame yayikazi itafungatira ana kapena mazira, usatenge mbalameyo pamodzi ndi ana ake omwe.
If a bird's nest chance to be before you in the way, in any tree or on the ground, with young ones or eggs, and the hen sitting on the young, or on the eggs, you shall not take the hen with the young:
7 Anawo mukhoza kutenga koma onetsetsani kuti mayi wawo mwamutaya kuti apite, kuti zinthu zizikuyenderani bwino ndiponso kuti mukhale ndi moyo wautali.
you shall surely let the hen go, but the young you may take to yourself; that it may be well with you, and that you may prolong your days.
8 Mukamanga nyumba yatsopano, mutchingire khonde lake la pa denga kuti inu musapezeke ndi mlandu wopha munthu ngati wina agwa kuchokera pa khonde la pa dengalo.
When you build a new house, then you shall make a battlement for your roof, that you do not bring blood on your house, if any man fall from there.
9 Musadzale mbewu zamitundu iwiri mʼmunda wanu wa mpesa, ngati mutero, si mbewu zanu zokha zimene zidzakhale zodetsedwa, komanso zipatso za mʼmunda wamphesawo.
You shall not sow your vineyard with two kinds of seed, lest the whole fruit be forfeited, the seed which you have sown, and the increase of the vineyard.
10 Musatipule pogwiritsa ntchito ngʼombe ndi bulu pa goli limodzi.
You shall not plow with an ox and a donkey together.
11 Musamavale chovala chopangidwa mophatikiza ubweya ndi thonje.
You shall not wear a mixed stuff, wool and linen together.
12 Muzipanga mphonje mʼngodya za mkanjo umene mumavala.
You shall make yourselves fringes on the four borders of your cloak, with which you cover yourself.
13 Ngati munthu akwatira mkazi, ndipo atagona naye nʼkusamufunanso
If any man takes a wife, and goes in to her, and hates her,
14 namunyoza ndi kumuyipitsira dzina nʼkumati, “Ine ndinakwatira mkazi uyu, koma pamene ndinakhala naye, sindinachione chizindikiro cha unamwali wake,”
and accuses her of shameful things, and brings up an evil name on her, and says, "I took this woman, and when I came near to her, I did not find in her the tokens of virginity";
15 zikatero abambo ndi amayi ake ayenera kubweretsa chitsimikizo chakuti anali namwali kwa akuluakulu a mzinda ku chipata.
then shall the father of the young woman, and her mother, take and bring forth the tokens of the young woman's virginity to the elders of the city in the gate;
16 Abambo ake a mtsikanayo adzanene kwa akuluakuluwo kuti, “Ine ndinamupatsa munthu uyu mwana wanga wamkazi kuti amukwatire, koma sakumufunanso.
and the young woman's father shall tell the elders, "I gave my daughter to this man to wife, and he hates her;
17 Tsopano wamunyoza ndipo wanena kuti, ‘Ine sindinapeze kuti mwana wanu wamkaziyu ndi namwali.’ Koma tsopano onani chitsimikizo ichi cha unamwali wa mwana wanga wamkazi.” Kenaka makolo a mtsikanayo adzaonetse kansalu kwa akuluakulu aja,
and look, he has accused her of shameful things, saying, 'I did not find in your daughter the tokens of virginity;' and yet these are the tokens of my daughter's virginity." They shall spread the cloth before the elders of the city.
18 ndipo akuluakuluwo adzamugwire munthuyo namupatsa chilango.
The elders of that city shall take the man and chastise him;
19 Iwo adzamulipitse ndalama zasiliva zokwana 100 nazipereka kwa abambo a mtsikana, chifukwa munthu uyu wayipitsa dzina la mtsikana wa Chiisraeli. Ayenera kukhalabe mkazi wake ndipo asadzamuleke moyo wake wonse.
and they shall fine him one hundred shekels of silver, and give them to the father of the young woman, because he has brought up an evil name on a virgin of Israel: and she shall be his wife; he may not put her away all his days.
20 Koma ngati zomunenerazo ndi zoona, ndipo kuti chitsimikizo cha unamwali wa mtsikanayo sichinapezeke,
But if this thing be true, that the tokens of virginity were not found in the young woman;
21 iyeyu ayenera kumutengera pa khomo pa abambo ake pamene anthu a mu mzinda wake akamuphere ndi miyala. Iyeyo wachita chinthu chochititsa manyazi mu Israeli pochita chiwerewere akanali pa khomo pa abambo ake. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu.
then they shall bring out the young woman to the door of her father's house, and the men of her city shall stone her to death with stones, because she has done folly in Israel, to play the prostitute in her father's house: so you shall put away the evil from the midst of you.
22 Ngati munthu apezeka akugona ndi mkazi wa mwini wake, ayenera kuphedwa munthuyo pamodzi ndi mkazi yemwe wagona nayeyo. Muyenera kuchotsa zoyipa mu Israeli.
If a man be found lying with a woman married to a husband, then they shall both of them die, the man who lay with the woman, and the woman: so you shall put away the evil from Israel.
23 Ngati munthu mu mzinda akumana ndi mkazi yemwe anachita kale chinkhoswe nagona naye,
If there is a young woman who is a virgin pledged to be married to a husband, and a man find her in the city, and lie with her;
24 muwatengere awiriwo ku chipata cha mzinda ndi kuwapha ndi miyala. Aphedwe chifukwa mtsikanayo anali pafupi ndi anthu ndipo sanakuwe kuti ena amuthandize ndipo mwamunayo chifukwa anayipitsa mkazi wa mwini. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
then you shall bring them both out to the gate of that city, and you shall stone them to death with stones; the woman, because she did not cry, being in the city; and the man, because he has humbled his neighbor's wife: so you shall put away the evil from the midst of you.
25 Koma ngati munthu akumana ndi mkazi kutchire yemwe anachita kale chinkhoswe namugwiririra, mwamuna yekhayo ndiye woyenera kuphedwa.
But if the man find the woman who is pledged to be married in the field, and the man force her, and lie with her; then the man only who lay with her shall die:
26 Mtsikanayo musamuchite chilichonse, palibe tchimo limene wachita loti ayenera kuphedwa. Mlandu uwu ufanana ndi wa munthu amene alimbana ndi kupha mnzake woyandikana naye,
but to the woman you shall do nothing; there is in the woman no sin worthy of death: for as when a man rises against his neighbor, and kills him, even so is this matter;
27 pakuti mwamunayo anamupeza mtsikanayo kutchire, ndipo ngakhale mtsikana wachinkhosweyo anakuwa, panalibe anamulanditsa.
for he found her in the field, the pledged to be married woman cried, and there was none to save her.
28 Ngati munthu apezana ndi namwali woti sanachite chinkhoswe, namugwiririra, munthuyo nʼkupezeka,
If a man find a woman who is a virgin, who is not pledged to be married, and lay hold on her, and lie with her, and they be found;
29 ayenera kuwalipira abambo ake a namwaliyo ndalama za siliva makumi asanu. Iye ayenera kumukwatira mkaziyo chifukwa wamuyipitsa, ndipo sadzamulekanso moyo wake wonse.
then the man who lay with her shall give to the woman's father fifty shekels of silver, and she shall be his wife, because he has humbled her; he may not put her away all his days.
30 Munthu asakwatire mkazi wa abambo ake pakuti ayenera kuchitira ulemu pogona pa abambo ake.
A man shall not take his father's wife, and shall not uncover his father's skirt.

< Deuteronomo 22 >