< Deuteronomo 22 >

1 Ngati uwona ngʼombe kapena nkhosa ya mʼbale wako ikusochera, usayilekerere koma uyesetse kuyibwezera kwa iye.
Kad vidiš kako luta vol ili ovca tvoga brata, nemoj proći mimo njih nego ih otjeraj svome bratu.
2 Ngati mʼbale wakoyo sakhala pafupi kapena sukudziwa kuti ndi yandani, uyitengere ku nyumba kwako ndi kuyisamala mpaka mwini wake atayilondola ndipo umubwezere.
Ako ti brat nije blizu ili ga ne znaš, kući ih svojoj dotjeraj pa neka ostanu kod tebe dokle brat tvoj ne dođe po njih. Tada mu ih vrati.
3 Uzitero ndithu ngati upeza bulu kapena mkanjo kapena chilichonse chimene chatayika. Osachilekerera.
Tako čini s njegovim magarcem, s njegovim ogrtačem i sa svime što brat tvoj izgubi, a ti nađeš. Nije ti dopušteno prolaziti mimo njegovo.
4 Ngati wapeza bulu kapena ngʼombe ya mʼbale wako itagwa panjira, usayilekerere. Ithandize kuti idzuke.
Kad opaziš kako se magarac tvoga brata ili njegov vol svalio na putu, ne kloni se nego mu pomozi da ih podigne.
5 Akazi asavale zovala za amuna, kapena mwamuna kuvala zovala za akazi, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita izi.
Žena ne smije na se stavljati muške odjeće, a muškarac se ne smije oblačiti u ženske haljine. Tko bi to činio bio bi odvratan Jahvi, Bogu svome.
6 Ukapeza chisa cha mbalame mʼmphepete mwa msewu, kaya ndi mu mtengo kapena pansi, mbalame yayikazi itafungatira ana kapena mazira, usatenge mbalameyo pamodzi ndi ana ake omwe.
Ako putem naiđeš na ptičje gnijezdo sa ptićima ili s jajima, na stablu ili na zemlji, a majka bude ležala sa ptićima ili na jajima, nemoj uzimati majke sa ptićima:
7 Anawo mukhoza kutenga koma onetsetsani kuti mayi wawo mwamutaya kuti apite, kuti zinthu zizikuyenderani bwino ndiponso kuti mukhale ndi moyo wautali.
pusti majku na slobodu, a ptiće uzmi. Tako ćeš imati sreću i dug život.
8 Mukamanga nyumba yatsopano, mutchingire khonde lake la pa denga kuti inu musapezeke ndi mlandu wopha munthu ngati wina agwa kuchokera pa khonde la pa dengalo.
Kad gradiš novu kuću, na krovu načini ogradu da svoju kuću, kad bi tko s nje pao, ne okaljaš krvlju.
9 Musadzale mbewu zamitundu iwiri mʼmunda wanu wa mpesa, ngati mutero, si mbewu zanu zokha zimene zidzakhale zodetsedwa, komanso zipatso za mʼmunda wamphesawo.
Po svome vinogradu nemoj sijati drugog usjeva da ne bi bila posvećena čitava ljetina: i plod sjemena i rod vinograda.
10 Musatipule pogwiritsa ntchito ngʼombe ndi bulu pa goli limodzi.
Ne upreži u plug vola i magarca zajedno.
11 Musamavale chovala chopangidwa mophatikiza ubweya ndi thonje.
Ne oblači se u tkaninu otkanu od vune i lana zajedno.
12 Muzipanga mphonje mʼngodya za mkanjo umene mumavala.
Na četiri roglja ogrtača kojim se zaogrćeš napravi rese.
13 Ngati munthu akwatira mkazi, ndipo atagona naye nʼkusamufunanso
Ako koji čovjek uzme ženu i uđe k njoj, ali je potom zamrzi,
14 namunyoza ndi kumuyipitsira dzina nʼkumati, “Ine ndinakwatira mkazi uyu, koma pamene ndinakhala naye, sindinachione chizindikiro cha unamwali wake,”
pripiše joj ružnoće i ozloglasi je govoreći: 'Oženih se njome, ali kad joj priđoh, ne nađoh u nje znakova djevičanstva' -
15 zikatero abambo ndi amayi ake ayenera kubweretsa chitsimikizo chakuti anali namwali kwa akuluakulu a mzinda ku chipata.
neka tada djevojčin otac i majka uzmu dokaz djevojčina djevičanstva te ga iznesu pred gradske starješine na vrata.
16 Abambo ake a mtsikanayo adzanene kwa akuluakuluwo kuti, “Ine ndinamupatsa munthu uyu mwana wanga wamkazi kuti amukwatire, koma sakumufunanso.
Potom neka progovori starješinama djevojčin otac: 'Ovome sam čovjeku dao svoju kćer za ženu, ali mu je omrzla.
17 Tsopano wamunyoza ndipo wanena kuti, ‘Ine sindinapeze kuti mwana wanu wamkaziyu ndi namwali.’ Koma tsopano onani chitsimikizo ichi cha unamwali wa mwana wanga wamkazi.” Kenaka makolo a mtsikanayo adzaonetse kansalu kwa akuluakulu aja,
Stoga joj pripisuje svašta ružno i tvrdi: nisam u tvoje kćeri našao znakove djevičanstva. Ali evo djevičanskih znakova moje kćeri!' I neka razastru plahtu pred gradskim starješinama.
18 ndipo akuluakuluwo adzamugwire munthuyo namupatsa chilango.
Neka tada starješine onoga grada uzmu muža pa ga kazne;
19 Iwo adzamulipitse ndalama zasiliva zokwana 100 nazipereka kwa abambo a mtsikana, chifukwa munthu uyu wayipitsa dzina la mtsikana wa Chiisraeli. Ayenera kukhalabe mkazi wake ndipo asadzamuleke moyo wake wonse.
neka ga, zato što je pronio ružan glas o jednoj izraelskoj djevici, udare globom od stotinu srebrnika pa ih dadnu ocu mlade žene. I neka mu ona i dalje bude ženom da je ne može pustiti dok je živ.
20 Koma ngati zomunenerazo ndi zoona, ndipo kuti chitsimikizo cha unamwali wa mtsikanayo sichinapezeke,
Ali ako optužba - da se na mladoj ženi nije našlo djevičanstvo - bude istinita,
21 iyeyu ayenera kumutengera pa khomo pa abambo ake pamene anthu a mu mzinda wake akamuphere ndi miyala. Iyeyo wachita chinthu chochititsa manyazi mu Israeli pochita chiwerewere akanali pa khomo pa abambo ake. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu.
neka djevojku izvedu na kućna vrata njezina oca pa neka je ljudi njezina grada kamenjem zasiplju dok ne umre, jer je počinila besramnost u Izraelu odajući se bludu u očevu domu. Tako ćeš iskorijeniti zlo iz svoje sredine.
22 Ngati munthu apezeka akugona ndi mkazi wa mwini wake, ayenera kuphedwa munthuyo pamodzi ndi mkazi yemwe wagona nayeyo. Muyenera kuchotsa zoyipa mu Israeli.
Ako se koji čovjek zateče gdje leži sa ženom udatom za drugoga, neka oboje - i čovjek koji je ležao sa ženom i sama žena - budu smaknuti. Tako ćeš iskorijeniti zlo iz Izraela.
23 Ngati munthu mu mzinda akumana ndi mkazi yemwe anachita kale chinkhoswe nagona naye,
Ako mladu djevicu zaručenu za nekoga u gradu sretne drugi čovjek i s njom legne,
24 muwatengere awiriwo ku chipata cha mzinda ndi kuwapha ndi miyala. Aphedwe chifukwa mtsikanayo anali pafupi ndi anthu ndipo sanakuwe kuti ena amuthandize ndipo mwamunayo chifukwa anayipitsa mkazi wa mwini. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
oboje ih dovedite vratima toga grada pa ih kamenjem zasipljite dok ne umru: djevojku što nije zvala u pomoć u gradu, a čovjeka što je oskvrnuo ženu bližnjega svoga. Tako ćeš iskorijeniti zlo iz svoje sredine.
25 Koma ngati munthu akumana ndi mkazi kutchire yemwe anachita kale chinkhoswe namugwiririra, mwamuna yekhayo ndiye woyenera kuphedwa.
Ako čovjek u polju naiđe na zaručenu djevojku i silom legne s njom, onda neka se pogubi samo taj što je s njom legao;
26 Mtsikanayo musamuchite chilichonse, palibe tchimo limene wachita loti ayenera kuphedwa. Mlandu uwu ufanana ndi wa munthu amene alimbana ndi kupha mnzake woyandikana naye,
a djevojci nemoj ništa: nema na njoj krivnje kojom bi zasluživala smrt. Jer to je kao da navali tko na bližnjega svoga i ubije ga.
27 pakuti mwamunayo anamupeza mtsikanayo kutchire, ndipo ngakhale mtsikana wachinkhosweyo anakuwa, panalibe anamulanditsa.
On ju je zatekao u polju; i premda je zaručena djevojka zapomagala, nije bilo nikoga da joj priskoči u pomoć.
28 Ngati munthu apezana ndi namwali woti sanachite chinkhoswe, namugwiririra, munthuyo nʼkupezeka,
Ako čovjek naiđe na mladu djevicu koja nije zaručena te je pograbi i s njom legne, pa budu uhvaćeni na djelu,
29 ayenera kuwalipira abambo ake a namwaliyo ndalama za siliva makumi asanu. Iye ayenera kumukwatira mkaziyo chifukwa wamuyipitsa, ndipo sadzamulekanso moyo wake wonse.
tada čovjek koji je s njom ležao neka djevojčinu ocu dade pedeset srebrnika. A budući da ju je oskvrnuo, neka je uzme za ženu da je ne može pustiti dok je živ.
30 Munthu asakwatire mkazi wa abambo ake pakuti ayenera kuchitira ulemu pogona pa abambo ake.
Neka se nitko ne ženi ženom oca svoga i neka ne odgrće očeva pokrivača.

< Deuteronomo 22 >