< Deuteronomo 21 >

1 Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha,
Jeśli w ziemi, którą PAN, twój Bóg, daje ci w posiadanie, zostanie znaleziony zabity człowiek leżący na polu, a nie wiadomo, kto go zabił;
2 akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira.
Wtedy twoi starsi i sędziowie wyjdą i zmierzą odległość do miast [leżących] dokoła zabitego.
3 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli
A starsi tego miasta, które leży najbliżej zabitego, wezmą jałówkę, której jeszcze nie użyto do pracy i która jeszcze nie ciągnęła w jarzmie;
4 ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo.
I zaprowadzą starsi tego miasta jałówkę do kamienistej doliny, gdzie nigdy nie uprawiano ani nie zasiewano, i tam utną kark jałówki w tej dolinie.
5 Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana.
Potem przyjdą kapłani, synowie Lewiego, gdyż ich wybrał PAN, twój Bóg, aby mu służyli i aby błogosławili w imię PANA, a według ich uznania ma być rozstrzygnięty każdy spór i każde zranienie;
6 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija,
I wszyscy starsi tego miasta, które leży najbliżej zabitego, umyją swoje ręce nad jałówką, którą ścięto w dolinie;
7 nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako.
I oświadczą: Nasze ręce nie wylały tej krwi i nasze oczy [tego] nie widziały.
8 Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa.
PANIE, przyjmij przebłaganie za twój lud Izraela, który odkupiłeś, a nie poczytaj twemu ludowi Izraela niewinnej krwi. I będą oczyszczeni od tej krwi.
9 Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova.
W ten sposób usuniesz niewinną krew spośród siebie, gdy uczynisz to, co jest prawe w oczach PANA.
10 Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo,
Gdy też wyruszysz na wojnę przeciwko swoim wrogom i PAN, twój Bóg, wyda ich w twoje ręce, i weźmiesz z nich jeńców;
11 ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu.
I zobaczysz wśród jeńców piękną kobietę, którą sobie upodobasz, i chciałbyś pojąć ją za żonę;
12 Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake
Wtedy przyprowadzisz ją do swego domu, a ona ogoli swoją głowę i obetnie sobie paznokcie;
13 ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu.
I złoży z siebie szatę, w której została pojmana, zostanie w twoim domu i będzie opłakiwać swego ojca i matkę przez cały miesiąc. Potem będziesz z nią obcował i będziesz jej mężem, a ona będzie twoją żoną.
14 Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu.
A jeśli nie będzie ci się podobać, wtedy pozwolisz jej odejść, dokąd zechce; żadną miarą nie sprzedasz jej za pieniądze i nie będziesz nią kupczyć, gdyż ją poniżyłeś.
15 Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo,
Gdyby mężczyzna miał dwie żony, jedną kochaną, a drugą znienawidzoną, i one urodzą mu synów – kochana i znienawidzona – a pierworodny będzie synem znienawidzonej;
16 akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda.
To gdy będzie przydzielał dobra swoim synom w dziedzictwo, nie będzie mógł ustanowić pierworodnym syna kochanej przed pierworodnym synem znienawidzonej;
17 Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake.
Ale za pierworodnego uzna syna znienawidzonej, dając mu podwójną część wszystkiego, co ma, gdyż on [jest] początkiem jego siły, jemu przysługuje prawo pierworództwa.
18 Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza,
Jeśli ktoś ma syna upartego i krnąbrnego, który nie słucha ani głosu swojego ojca, ani głosu swojej matki, a choć go karcą, nie słucha ich;
19 abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo
Wtedy jego ojciec i matka wezmą go i przyprowadzą do starszych swego miasta i do bramy jego miejscowości;
20 akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.”
I powiedzą do starszych miasta: Ten nasz syn jest uparty i krnąbrny, nie słucha naszego głosu, [jest] żarłokiem i pijakiem;
21 Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha.
Wtedy wszyscy mężczyźni tego miasta ukamienują go na śmierć; w ten sposób usuniesz zło spośród siebie, a cały Izrael usłyszy o tym i będzie się bać.
22 Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo,
A jeśli ktoś popełni grzech zasługujący na śmierć i poniesie śmierć, a powiesisz go na drzewie;
23 musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.
Jego trup nie pozostanie na drzewie przez noc, lecz musisz go pochować tego samego dnia, bo ten, kto wisi, [jest] przeklęty przez Boga. Nie będziesz plugawił twojej ziemi, którą PAN, twój Bóg, daje ci w dziedzictwo.

< Deuteronomo 21 >