< Deuteronomo 21 >
1 Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha,
Si, en la terre que le Seigneur te donne pour héritage, on trouve le cadavre d'un homme frappé à mort dans les champs, et si l'on ignore qui a porté le coup,
2 akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira.
Tes anciens et tes juges sortiront et mesureront à quelle distance sont les villes au milieu desquelles on aura trouvé le corps.
3 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli
On verra quelle est la ville la plus proche du cadavre; alors, les anciens de cette ville prendront, parmi les bœufs, une génisse, non encore soumise au joug;
4 ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo.
Puis, ils feront descendre la génisse en un ravin inculte, et, dans ce ravin, ils trancheront les muscles du cou de la génisse,
5 Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana.
Ensuite, viendront les prêtres et les lévites choisis par le Seigneur Dieu pour se tenir auprès de lui et pour bénir en son nom, car c'est à eux qu'il appartient de condamner et d'absoudre.
6 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija,
Tous les anciens de la ville la plus proche du cadavre se laveront les mains sur la tête de la génisse immolée dans le ravin.
7 nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako.
Puis, ils diront: Nos mains n'ont pas versé ce sang, et nos yeux n'ont rien vu.
8 Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa.
Seigneur, soyez propice au peuple d'Israël que vous avez délivré; faites que le sang innocent ne tombe pas sur le peuple d'Israël; et pour eux le cri du sang innocent sera apaisé
9 Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova.
Et tu auras effacé du milieu du peuple la tache du sang innocent, si tu as fait ce qui est bon et agréable devant le Seigneur.
10 Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo,
Si tu vas en guerre contre des ennemis, si le Seigneur te les ayant livrés, tu t'empares de leurs richesses,
11 ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu.
Et si tu vois parmi le butin une femme qui soit belle; si tu la désires et si tu la prends pour femme,
12 Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake
Tu la conduiras en ta demeure, tu lui raseras la tête, tu lui couperas les ongles,
13 ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu.
Tu lui ôteras les vêtements de la captivité; elle restera en ta maison pendant un mois, elle pleurera son père et sa mère; après cela tu t'approcheras d'elle, tu auras commerce avec elle; elle sera ta femme.
14 Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu.
Et si tu ne la veux plus, tu la renverras libre, parce que tu l'auras humiliée, et tu ne la vendras pas à prix d'argent, et tu ne la mépriseras point.
15 Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo,
Si un homme a deux femmes, l'une bien-aimée, l'autre haïe, et qu'elles enfantent, la détestée comme la bien-aimée, et que le fils premier-né soit de la femme haïe;
16 akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda.
Le jour où l'homme fera le partage de ses biens, il ne pourra transmettre le droit d'aînesse au fils de la bien-aimée, au mépris du fils premier-né, provenant de la femme haïe.
17 Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake.
Il reconnaîtra celui-ci comme son premier-né, et lui donnera double part dans tous ses biens, parce qu'il est l'aîné des enfants et que cette double part appartient au droit d'aînesse.
18 Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza,
Si un homme a un fils indocile, querelleur, sourd à la voix de son père et de sa mère; s'ils le réprimandent sans qu'il les écoute,
19 abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo
Son père et sa mère, l'ayant pris avec eux, le conduiront auprès des anciens devant la porte de la ville,
20 akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.”
Et ils diront aux hommes de leur ville: Notre fils que voici est désobéissant et querelleur; sourd à notre voix, il court les festins et s'enivre;
21 Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha.
Alors, les hommes de la ville le lapideront; il mourra et vous aurez déraciné parmi tous le mal, et les autres enfants indociles l'apprenant auront crainte.
22 Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo,
Si un homme coupable d'un crime capital est mis à mort, et que vous l'ayez pendu à une potence,
23 musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.
Que son corps n'y passe point la nuit; enterrez-le le même jour dans une fosse, car tout homme pendu a une potence est maudit de Dieu; ne souillez donc pas la terre que Dieu vous donne en héritage.