< Deuteronomo 21 >
1 Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha,
Si quelqu'un est trouvé tué dans le pays dont l'Éternel, ton Dieu, te donne la possession, couché dans les champs, et que l'on ne sache pas qui l'a frappé,
2 akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira.
tes anciens et tes juges sortiront, et ils mesureront les villes qui entourent celui qui est tué.
3 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli
Les anciens de la ville la plus proche de l'homme tué prendront une génisse du troupeau, qui n'a pas été travaillée et qui n'a pas tiré le joug.
4 ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo.
Les anciens de cette ville feront descendre la génisse dans une vallée où coulent des eaux courantes, qui n'est ni labourée ni ensemencée, et ils briseront le cou de la génisse là, dans la vallée.
5 Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana.
Les prêtres, fils de Lévi, s'approcheront, car c'est eux que Yahvé ton Dieu a choisis pour le servir et pour bénir au nom de Yahvé; et c'est d'après leur parole que seront tranchées toutes les controverses et toutes les contestations.
6 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija,
Tous les anciens de la ville la plus proche de l'homme tué laveront leurs mains sur la génisse dont le cou a été brisé dans la vallée.
7 nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako.
Ils répondront: « Nos mains n'ont pas versé ce sang, et nos yeux ne l'ont pas vu.
8 Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa.
Pardonne, Yahvé, à ton peuple d'Israël, que tu as racheté, et ne permets pas le sang innocent parmi ton peuple d'Israël. » Le sang leur sera pardonné.
9 Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova.
Ainsi, vous effacerez le sang innocent du milieu de vous, lorsque vous ferez ce qui est juste aux yeux de l'Éternel.
10 Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo,
Lorsque tu iras combattre tes ennemis, que Yahvé ton Dieu les livrera entre tes mains et que tu les emmèneras en captivité,
11 ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu.
et que tu verras parmi les captives une belle femme, que tu seras attiré par elle et que tu voudras la prendre pour femme,
12 Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake
tu la ramèneras dans ta maison. Elle se rasera la tête et se coupera les ongles.
13 ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu.
Elle ôtera les vêtements de sa captivité, restera dans ta maison et pleurera son père et sa mère pendant un mois entier. Après cela, tu iras chez elle et tu seras son mari, et elle sera ta femme.
14 Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu.
Si elle ne te plaît pas, tu la laisseras aller où elle voudra, mais tu ne la vendras pas du tout pour de l'argent. Tu ne la traiteras pas comme une esclave, car tu l'as humiliée.
15 Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo,
Si un homme a deux femmes, l'une bien-aimée et l'autre haïe, et qu'elles lui aient enfanté, l'une bien-aimée et l'autre haïe, et que le fils premier-né soit celui de la haïe,
16 akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda.
alors, le jour où il fera hériter ses fils de ce qui lui appartient, il ne donnera pas au fils de la bien-aimée les droits du premier-né avant le fils de la haïe, qui est le premier-né;
17 Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake.
mais il reconnaîtra le premier-né, le fils du haï, en lui donnant une double part de tout ce qu'il possède, car il est le commencement de sa force. Le droit du premier-né lui revient.
18 Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza,
Si un homme a un fils obstiné et rebelle qui n'obéit pas à la voix de son père ou à la voix de sa mère, et qui, bien qu'ils le châtient, ne les écoute pas,
19 abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo
son père et sa mère le saisiront et le conduiront devant les anciens de sa ville et à la porte de son lieu de résidence.
20 akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.”
Ils diront aux anciens de sa ville: « Notre fils est têtu et rebelle. Il n'obéit pas à notre voix. C'est un glouton et un ivrogne ».
21 Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha.
Tous les hommes de sa ville le lapideront jusqu'à ce que mort s'ensuive. Ainsi vous éloignerez le mal du milieu de vous. Tout Israël entendra et craindra.
22 Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo,
Si un homme a commis un péché qui mérite la mort, qu'il soit mis à mort et que tu le pendes à un arbre,
23 musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.
son corps ne restera pas toute la nuit sur l'arbre, mais tu l'enterreras le jour même, car celui qui est pendu est maudit de Dieu. Ne souille pas le pays que Yahvé ton Dieu te donne en héritage.