< Deuteronomo 21 >
1 Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha,
If there be found a slain person in the land which the Lord thy God giveth thee to possess it, lying in the field, [and] it be not known who hath slain him:
2 akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira.
Then shall thy elders and thy judges go forth, and they shall measure unto the cities which are round about the one that is slain.
3 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli
And it shall be, that the city which is the nearest unto the slain person, even the elders of that city shall take a heifer, which hath not been wrought with, which hath not drawn in a yoke;
4 ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo.
And the elders of that city shall bring down the heifer unto a rough valley, which is neither tilled nor sown, and they shall break there the neck of the heifer in the valley;
5 Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana.
And the priests the sons of Levi shall come near; for them the Lord thy God hath chosen to minister unto him, and to bless in the name of the Lord; and after their decision shall be done [at] every controversy and every injury;
6 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija,
And all the elders of that city who are nearest unto the slain person shall wash their hands over the heifer, the neck of which is broken in the valley.
7 nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako.
And they shall commence and say, Our hands have not shed this blood, and our eyes have not seen it.
8 Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa.
Grant pardon unto thy people Israel, whom thou hast redeemed, O Lord, and lay not innocent blood in the midst of thy people Israel: and the blood shall be forgiven unto them.
9 Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova.
And thou shalt put away the [guilt of] the innocent blood from the midst of thee, when thou wilt do what is right in the eyes of the Lord.
10 Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo,
When thou goest forth to war against thy enemies, and the Lord thy God delivereth them into thy hands, and thou takest captives of them;
11 ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu.
And thou seest among the captives a woman of handsome form, and hast a desire unto her, that thou wouldst take her to thee for wife:
12 Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake
Then shalt thou bring her home to thy house; and she shall shave her head, and let grow her nails;
13 ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu.
And she shall put off the raiment of her captivity from her, and she shall remain in thy house, and weep for her father and her mother a full month; and after that thou mayest go in unto her, and be her husband, that she may become thy wife.
14 Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu.
And it shall be, if thou have no delight in her, then shalt thou let her go whither she will; but thou shalt nowise sell her for money; thou shalt not make a servant of her, because thou hast humbled her.
15 Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo,
If a man have two wives, one beloved, and the other hated, and they bear him children, both the beloved and the hated; so that the first-born son be hers that is hated:
16 akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda.
Then shall it be, when he divideth as inheritance among his sons what he hath, that he shall not institute the son of the beloved as the first-born before the son of the hated, the firstborn;
17 Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake.
But the first-born, the son of the hated woman, shall he acknowledge, to give him a double portion of all that is found in his possession; for he is the beginning of his strength; to him belongeth the right of the first birth.
18 Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza,
If a man have a stubborn and rebellious son, who hearkeneth not to the voice of his father, or the voice of his mother, and they chastise him, and he will not hearken unto them:
19 abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo
Then shall his father and his mother lay hold on him, and bring him out unto the elders of his city, and unto the gate of his place;
20 akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.”
And they shall say unto the elders of his city, This our son is stubborn and rebellious, he will not hearken to our voice; he is a glutton, and a drunkard.
21 Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha.
And all the men of his city shall stone him with stones, that he die; and thou shalt put away the evil from the midst of thee; and all Israel shall hear, and be afraid.
22 Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo,
And if a man have committed a sin for which there is a punishment of death, and he be to be put to death, and thou hang him on a tree:
23 musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.
Then shall his body not remain all night on the tree, but thou shalt surely bury him on that day; [for he that is hanged is a dishonor of God; ] and thou shalt not defile thy land, which the Lord thy God giveth thee for an inheritance.