< Deuteronomo 20 >
1 Pamene mukupita kokachita nkhondo ndi adani anu, mukaona akavalo kapena magaleta kapena gulu la ankhondo kuposa inuyo musamaope chifukwa Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto adzakhala nanu.
Quand tu iras à la guerre contre tes ennemis, et que tu verras des chevaux et des chariots, et un peuple plus grand que toi, n'aie point peur d'eux, car l'Eternel ton Dieu qui t'a fait monter hors du pays d'Egypte, [est] avec toi.
2 Pamene mwatsala pangʼono kuyamba nkhondo, wansembe azibwera kutsogolo ndipo aziyankhula ku gulu lonse lankhondolo.
Et quand il faudra s'approcher pour combattre, le Sacrificateur s'avancera, et parlera au peuple,
3 Iye aziti, “Tamverani inu Aisraeli, mukupita kukachita nkhondo ndi adani anu lero. Musataye mitima kapena kuchita mantha ayi. Musaopsedwe kapena kunjenjemera pamaso pawo,
Et leur dira: Ecoute Israël: Vous vous approchez aujourd'hui pour combattre vos ennemis; que votre cœur ne soit point lâche, ne craignez point, ne soyez point épouvantés, ne soyez point effrayés à cause d'eux.
4 pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye amene apite nanu kukakumenyerani nkhondo ndi kugonjetsa adani anu.”
Car l'Eternel votre Dieu marche avec vous, pour combattre pour vous contre vos ennemis, [et] pour vous conserver.
5 Akuluakulu ankhondo adzati kwa gulu la ankhondolo, “Kodi pali wina amene wangomanga nyumba kumene ndipo sanayitsekulire? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondoko ndipo wina ndi kudzayitsekulira.
Alors les Officiers parleront au peuple, en disant: Qui est celui qui a bâti une maison neuve, et ne l'a point dédiée? qu'il s'en aille, et s'en retourne en sa maison, de peur qu'il ne meure en la bataille, et qu'un autre ne la dédie.
6 Kodi pali wina amene analima munda wamphesa ndipo sanayambe kudyerera? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzadyerera mundawo.
Et qui est celui qui a planté une vigne, et n'en a point encore cueilli le fruit? qu'il s'en aille, et s'en retourne en sa maison, de peur qu'il ne meure en la bataille, et qu'un autre n'en cueille le fruit.
7 Kodi pali amene wachita chinkhoswe ndi mkazi ndipo sanamukwatire mkaziyo? Ayambe wabwerera ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzakwatira mkaziyo.”
Et qui est celui qui a fiancé une femme, et ne l'a point épousée? qu'il s'en aille, et s'en retourne en sa maison, de peur qu'il ne meure en la bataille, et qu'un autre ne l'épouse.
8 Ndipo akuluakulu ankhondowo akapitirize kuti, “Kodi pali amene akuchita mantha kapena kutaya mtima? Abwerere ku mudzi kuopa kuti abale ake angatayenso mtima.”
Et les officiers continueront à parler au peuple, et diront: Si quelqu'un est timide et lâche, qu'il s'en aille, et s'en retourne en sa maison, de peur que le cœur de ses frères ne se fonde comme le sien.
9 Akuluakuluwo akatsiriza kuyankhula ndi gulu la ankhondolo, adzasankhe olilamulira.
Et aussitôt que les officiers auront achevé de parler au peuple, ils rangeront les chefs des bandes à la tête de chaque troupe.
10 Pamene mukuyandikira kuphwanya mzinda, muyambe mwafunsa anthu a mu mzindawo ngati afuna zamtendere.
Quand tu t'approcheras d'une ville pour lui faire la guerre, tu lui présenteras la paix.
11 Akavomera natsekula zipata zawo, anthu wonse mu mzindawo adzagwidwa ukapolo nakugwirirani ntchito.
Et si elle te fait une réponse de paix, et t'ouvre [les portes], tout le peuple qui sera trouvé dedans, te sera tributaire, et sujet.
12 Koma akakana za mtendere nachita nanu nkhondo, muwuphwanye mzindawo.
Mais si elle ne traite pas avec toi, et qu'elle fasse la guerre contre toi, alors tu mettras le siège contr'elle.
13 Yehova Mulungu wanu akakupatsani mzindawo, muwaphe amuna onse.
Et quand l'Eternel ton Dieu l'aura livrée entre tes mains, tu feras passer au fil de l'épée tous les hommes qui s'y trouveront.
14 Akazi, ana, ziweto ndi china chilichonse mu mzindamo, mukhoza kuzitenga kuti zikhale zanu monga katundu wolanda ku nkhondo. Katundu wa adani anuyu amene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, mukhoza kumugwiritsa ntchito.
[Réservant] seulement les femmes, et les petits enfants. Et quant aux bêtes, et tout ce qui sera dans la ville, [savoir] tout son butin, tu le pilleras pour toi; et tu mangeras le butin de tes ennemis, que l'Eternel ton Dieu t'aura donné.
15 Mizinda yonse yakutali osati ya mitundu yapafupi, muzichita nayo chomwechi.
Tu en feras ainsi à toutes les villes qui sont fort éloignées de toi; lesquelles ne [sont] point des villes de ces nations-ci;
16 Komabe mʼmizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, musasiyemo chamoyo chilichonse.
Mais tu ne laisseras vivre personne qui soit des villes de ces peuples que l'Eternel ton Dieu te donne en héritage.
17 Muwawononge kwathunthu Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi monga momwe Yehova Mulungu wanu anakulamulirani.
Car tu ne manqueras point de les détruire à la façon de l'interdit, [savoir] les Héthiens, les Amorrhéens, les Cananéens, les Phérésiens, les Héviens, les Jébusiens, comme l'Eternel ton Dieu te l'a commandé.
18 Mukapanda kutero adzakuphunzitsani kuti mutengere zinthu zonyansa zimene amachita popembedza milungu yawo ndipo mudzachimwira Yehova Mulungu wanu.
Afin qu'ils ne vous apprennent point à faire selon toutes les abominations qu'ils ont faites à leurs dieux, et que vous ne péchiez point contre l'Eternel votre Dieu.
19 Mukalimbana ndi mzinda nthawi yayitali, kuchita nawo nkhondo pofuna kuwugonjetsa, musawononge podula mitengo yake ndi nkhwangwa, osayidula chifukwa zipatso zakezo mukhoza kudya. Kodi mitengo ya ku munda ndi anthu kuti mukalimbane nayo?
Quand tu tiendras une ville assiégée durant plusieurs jours, en la battant pour la prendre, tu ne détruiras point ses arbres à coups de cognée, parce que tu en pourras manger; c'est pourquoi tu ne les couperas point; car l'arbre des champs [est-il] un homme, pour entrer dans la forteresse.
20 Komabe mukhoza kudula mitengo imene mukudziwa kuti si ya zipatso ndi kuyigwiritsa ntchito pa nkhondo mpaka mzinda umene mukumenyana nawowo utagwetsedwa.
Mais seulement tu détruiras et tu couperas les arbres que tu connaîtras n'être point des arbres fruitiers; et tu en bâtiras des forts contre la ville qui te fait la guerre, jusqu'à ce qu'elle soit subjuguée.