< Deuteronomo 20 >

1 Pamene mukupita kokachita nkhondo ndi adani anu, mukaona akavalo kapena magaleta kapena gulu la ankhondo kuposa inuyo musamaope chifukwa Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto adzakhala nanu.
“If you go out to battle against your enemies, and you see horsemen and chariots, and that the multitude of your adversary’s army is greater than your own, you shall not fear them. For the Lord your God, who led you away from the land of Egypt, is with you.
2 Pamene mwatsala pangʼono kuyamba nkhondo, wansembe azibwera kutsogolo ndipo aziyankhula ku gulu lonse lankhondolo.
Then, as the battle now draws near, the priest shall stand before the front ranks, and he shall speak to the people in this manner:
3 Iye aziti, “Tamverani inu Aisraeli, mukupita kukachita nkhondo ndi adani anu lero. Musataye mitima kapena kuchita mantha ayi. Musaopsedwe kapena kunjenjemera pamaso pawo,
‘Listen, O Israel! Today you engage in a battle against your enemies. Do not let your heart be overwhelmed with fear. Do not be apprehensive. Do not yield. You should have no dread of them.
4 pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye amene apite nanu kukakumenyerani nkhondo ndi kugonjetsa adani anu.”
For the Lord your God is in your midst, and he will contend against your enemies on your behalf, so that he may rescue you from peril.’
5 Akuluakulu ankhondo adzati kwa gulu la ankhondolo, “Kodi pali wina amene wangomanga nyumba kumene ndipo sanayitsekulire? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondoko ndipo wina ndi kudzayitsekulira.
Likewise, the officers shall proclaim, throughout every company, in the hearing of the soldiers: ‘What man is there who has built a new house, and has not dedicated it? Let him go and return to his house, lest perhaps he may die in the battle, and another man may dedicate it.
6 Kodi pali wina amene analima munda wamphesa ndipo sanayambe kudyerera? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzadyerera mundawo.
What man is there who has planted a vineyard, and has not yet caused it to be common, so that all may eat from it? Let him go, and return to his house, lest perhaps he may die in the battle, and another man may carry out his office.
7 Kodi pali amene wachita chinkhoswe ndi mkazi ndipo sanamukwatire mkaziyo? Ayambe wabwerera ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzakwatira mkaziyo.”
What man is there, who has betrothed a wife, and has not taken her? Let him go, and return to his house, lest perhaps he may die in battle, and another man may take her.’
8 Ndipo akuluakulu ankhondowo akapitirize kuti, “Kodi pali amene akuchita mantha kapena kutaya mtima? Abwerere ku mudzi kuopa kuti abale ake angatayenso mtima.”
After these things have been declared, they shall add the remainder, and shall say to the people: ‘What man is there who is overwhelmed by fear and is fainthearted? Let him go, and return to his house, lest he cause the hearts of his brothers to fear, just as he himself has been thoroughly stricken with fear.’
9 Akuluakuluwo akatsiriza kuyankhula ndi gulu la ankhondolo, adzasankhe olilamulira.
And when the officers of the army have become silent, and have completed their speech, each one shall prepare his unit to wage war.
10 Pamene mukuyandikira kuphwanya mzinda, muyambe mwafunsa anthu a mu mzindawo ngati afuna zamtendere.
When, at any time, you approach a city to fight against it, you shall first offer peace to it.
11 Akavomera natsekula zipata zawo, anthu wonse mu mzindawo adzagwidwa ukapolo nakugwirirani ntchito.
If they receive it, and open the gates to you, then all the people who are in it shall be saved, and they shall serve you by paying tribute.
12 Koma akakana za mtendere nachita nanu nkhondo, muwuphwanye mzindawo.
But if they are not willing to enter into an agreement, and they begin to act against you in warfare, then you shall besiege it.
13 Yehova Mulungu wanu akakupatsani mzindawo, muwaphe amuna onse.
And when the Lord your God will have delivered it into your hands, you shall strike down anyone who is in it, of the male gender, with the edge of the sword,
14 Akazi, ana, ziweto ndi china chilichonse mu mzindamo, mukhoza kuzitenga kuti zikhale zanu monga katundu wolanda ku nkhondo. Katundu wa adani anuyu amene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, mukhoza kumugwiritsa ntchito.
but not the women and young children, nor the cattle and the other things that are within the city. And you shall divide all the plunder to the soldiers, and you shall eat the spoils from your enemies, which the Lord your God will give to you.
15 Mizinda yonse yakutali osati ya mitundu yapafupi, muzichita nayo chomwechi.
So shall you do to all the cities which are at a great distance from you, those which are not among the cities that you shall receive as a possession.
16 Komabe mʼmizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, musasiyemo chamoyo chilichonse.
But among those cities which shall be given to you, you shall not permit anyone at all to live.
17 Muwawononge kwathunthu Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi monga momwe Yehova Mulungu wanu anakulamulirani.
Instead, you shall put them to death with the edge of the sword, specifically: the Hittite and the Amorite and the Canaanite, the Perizzite and the Hivite and the Jebusite, just as the Lord your God has commanded you.
18 Mukapanda kutero adzakuphunzitsani kuti mutengere zinthu zonyansa zimene amachita popembedza milungu yawo ndipo mudzachimwira Yehova Mulungu wanu.
Otherwise, they may teach you to do all the abominations which they have committed for their own gods. And then you would sin against the Lord your God.
19 Mukalimbana ndi mzinda nthawi yayitali, kuchita nawo nkhondo pofuna kuwugonjetsa, musawononge podula mitengo yake ndi nkhwangwa, osayidula chifukwa zipatso zakezo mukhoza kudya. Kodi mitengo ya ku munda ndi anthu kuti mukalimbane nayo?
When you will have besieged a city for a long time, and you will have encircled it with fortifications, so that you may fight against it, you shall not cut down trees from which one is able to eat, neither shall you cause devastation with axes to the surrounding region. For it is a tree, and not a man. It is not able to increase the number of those who are fighting against you.
20 Komabe mukhoza kudula mitengo imene mukudziwa kuti si ya zipatso ndi kuyigwiritsa ntchito pa nkhondo mpaka mzinda umene mukumenyana nawowo utagwetsedwa.
But if there are any trees which are not fruitful, but are wild, and if these are fit for other uses, then cut them down, and make machines, until you have captured the city that is contending against you.”

< Deuteronomo 20 >