< Deuteronomo 20 >
1 Pamene mukupita kokachita nkhondo ndi adani anu, mukaona akavalo kapena magaleta kapena gulu la ankhondo kuposa inuyo musamaope chifukwa Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto adzakhala nanu.
Когато излезеш на бой против неприятелите си, и видиш коне, колесници и люде повече от тебе, да се не убоиш от тях; защото с тебе е Господ твоят Бог, Който те е извел из Египетската земя.
2 Pamene mwatsala pangʼono kuyamba nkhondo, wansembe azibwera kutsogolo ndipo aziyankhula ku gulu lonse lankhondolo.
И като пристъпиш в боя, свещеникът да се приближи и да говори на людете, като им каже:
3 Iye aziti, “Tamverani inu Aisraeli, mukupita kukachita nkhondo ndi adani anu lero. Musataye mitima kapena kuchita mantha ayi. Musaopsedwe kapena kunjenjemera pamaso pawo,
Слушай, Израилю! вие пристъпвате днес да се биете против неприятелите си; да не премалее сърцето ви; не бойте се, нито се смущавайте, нито се ужасявайте от тях;
4 pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye amene apite nanu kukakumenyerani nkhondo ndi kugonjetsa adani anu.”
защото Господ вашият Бог, Той е, Който ходи с вас да се бие за вас против неприятелите ви, за да ви спаси.
5 Akuluakulu ankhondo adzati kwa gulu la ankhondolo, “Kodi pali wina amene wangomanga nyumba kumene ndipo sanayitsekulire? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondoko ndipo wina ndi kudzayitsekulira.
И военачалниците нека говорят на людете, като рекат: Кой е построил нова къща и не я е посветил? - Нека си иде и се върне у дома си, да не би да умре в боя, и друг да я посвети.
6 Kodi pali wina amene analima munda wamphesa ndipo sanayambe kudyerera? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzadyerera mundawo.
И кой е насадил лозе и не е ял от плода му? - Нека си иде и се върне у дома си, да не би да умре в боя и друг да яде плода му.
7 Kodi pali amene wachita chinkhoswe ndi mkazi ndipo sanamukwatire mkaziyo? Ayambe wabwerera ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzakwatira mkaziyo.”
И кой се е сгодил за жена и не я е взел? - Нека си иде и се върне у дома си, да не би да умре в боя, и друг да я вземе.
8 Ndipo akuluakulu ankhondowo akapitirize kuti, “Kodi pali amene akuchita mantha kapena kutaya mtima? Abwerere ku mudzi kuopa kuti abale ake angatayenso mtima.”
Военачалниците да говорят още на людете, като рекат: Кой е страхлив и малодушен? - Нека си иде и се върне у дома си, да не би да премалеят сърцата на братята му, както неговото сърце.
9 Akuluakuluwo akatsiriza kuyankhula ndi gulu la ankhondolo, adzasankhe olilamulira.
И военачалниците, като свършат да говорят на людете, нека поставят полководци над полковете за водители на людете.
10 Pamene mukuyandikira kuphwanya mzinda, muyambe mwafunsa anthu a mu mzindawo ngati afuna zamtendere.
Когато се приближиш при някой град, за да воюваш против него, предложи му мир.
11 Akavomera natsekula zipata zawo, anthu wonse mu mzindawo adzagwidwa ukapolo nakugwirirani ntchito.
Ако ти отговори мирно и ти отвори портите, тогава всичките люде, които се намират в него, да ти станат поданици и да ти работят.
12 Koma akakana za mtendere nachita nanu nkhondo, muwuphwanye mzindawo.
Но ако не направи мир с тебе, но воюва против тебе, тогава да го обсадиш;
13 Yehova Mulungu wanu akakupatsani mzindawo, muwaphe amuna onse.
и когато го предаде Господ твоят Бог в ръцете ти, тогава да поразиш всичките му мъжки с острото на ножа;
14 Akazi, ana, ziweto ndi china chilichonse mu mzindamo, mukhoza kuzitenga kuti zikhale zanu monga katundu wolanda ku nkhondo. Katundu wa adani anuyu amene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, mukhoza kumugwiritsa ntchito.
а жените, децата, добитъкът и всичко що се намира в града, всичкити користи от него да вземеш за себе си; и да ядеш користите от неприятелите си, които Господ твоят Бог ти даде.
15 Mizinda yonse yakutali osati ya mitundu yapafupi, muzichita nayo chomwechi.
Така да постъпваш с всичките градове, които са много далеч от тебе, които не са от градовете на тукашните народи.
16 Komabe mʼmizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, musasiyemo chamoyo chilichonse.
А от градовете на тия люде, които Господ твоят Бог ти дава за наследство, да не оставиш живо нищо, което диша,
17 Muwawononge kwathunthu Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi monga momwe Yehova Mulungu wanu anakulamulirani.
но да ги обречеш на изтребление; хетейците, аморейците, ханаанците, ферезйците, евейците и евусейците, според както Господ твоят Бог ти заповяда;
18 Mukapanda kutero adzakuphunzitsani kuti mutengere zinthu zonyansa zimene amachita popembedza milungu yawo ndipo mudzachimwira Yehova Mulungu wanu.
за да не ви научат да правите според всичките мерзости, които те са правили за боговете си, и така да съгрешите против Господа вашия Бог.
19 Mukalimbana ndi mzinda nthawi yayitali, kuchita nawo nkhondo pofuna kuwugonjetsa, musawononge podula mitengo yake ndi nkhwangwa, osayidula chifukwa zipatso zakezo mukhoza kudya. Kodi mitengo ya ku munda ndi anthu kuti mukalimbane nayo?
Когато обсаждаш някой град за дълго време и воюваш против него, за да го превземеш, да не унищожаваш дърветата му, нито да дигаш на тях секира; да не ги насичаш, защото от тях можеш да се храниш. Човек ли е полското дърво та да се обсажда от тебе?
20 Komabe mukhoza kudula mitengo imene mukudziwa kuti si ya zipatso ndi kuyigwiritsa ntchito pa nkhondo mpaka mzinda umene mukumenyana nawowo utagwetsedwa.
Само дърветата, които знаеш, че не са хранителни дървета, тях можеш да унищожаваш и изсичаш; и с тях да правиш кули против града, който ти се противи, догде бъде превзет.