< Deuteronomo 2 >

1 Kenaka tinabwerera ndi kuyamba ulendo wolowera ku chipululu motsatira njira ya ku Nyanja Yofiira, monga mmene Yehova anatilamulira. Kwa nthawi yayitali tinayendayenda cha ku dziko la mapiri la Seiri.
Puis nous nous tournâmes, et nous partîmes pour le désert, par le chemin de la mer Rouge, comme l'Éternel me l'avait dit, et nous encerclâmes la montagne de Séir pendant plusieurs jours.
2 Ndipo Yehova anati kwa ine,
L'Éternel m'a parlé, en disant:
3 “Mwazungulira mokwanira dziko la mapiri, tsopano tembenukirani kumpoto.
« Tu as assez longtemps encerclé cette montagne. Tourne-toi vers le nord.
4 Apatse anthu malamulo awa: ‘Muli pafupi kudutsa mʼchigawo cha abale anu adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Iwowa adzachita nanu mantha koma musamale kwambiri.
Tu donneras cet ordre au peuple: « Vous allez traverser la frontière de vos frères, les enfants d'Ésaü, qui habitent en Séir, et ils auront peur de vous. Soyez donc prudents.
5 Musayambane nawo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo ngakhale poti mungoyika phazi. Ndamupatsa Esau dziko lamapiri la Seiri kuti likhale lakelake.
Ne vous disputez pas avec eux, car je ne vous donnerai aucune de leurs terres, pas même pour que la plante du pied les foule, car j'ai donné la montagne de Séir en propriété à Ésaü.
6 Inu muyenera kuwalipira ndi siliva pa chakudya chimene mudye ndi madzi amene mumwe.’”
Tu achèteras d'eux, à prix d'argent, des aliments que tu pourras manger. Tu leur achèteras aussi de l'eau à prix d'argent, pour que tu puisses boire.'"
7 Yehova Mulungu wanu wakudalitsani mʼntchito zonse za manja anu. Iye wakuyangʼanirani pa ulendo wanu wodutsa mʼchipululu chachikulu. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu mʼzaka makumi anayi, ndipo simunasowe kalikonse.
Car Yahvé ton Dieu t'a béni dans tout le travail de tes mains. Il a connu ta marche dans ce grand désert. Ces quarante années, Yahvé ton Dieu a été avec toi. Tu n'as manqué de rien.
8 Choncho tinapitiriza ulendo modutsa abale athu, adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Tinapatukira njira ya ku Araba imene imachokera ku Elati ndi Ezioni Geberi ndipo tinayenda njira ya ku chipululu cha Mowabu.
Et nous passâmes à côté de nos frères, les fils d'Ésaü, qui habitent en Séir, par le chemin de la plaine d'Elath et d'Ezion Geber. Nous nous tournâmes et passâmes par le chemin du désert de Moab.
9 Ndipo Yehova anati kwa ine, “Musawavutitse Amowabu kapena kuwaputa kuti muchite nawo nkhondo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo. Ndinapereka Ari kwa adzukulu a Loti ngati chuma chawo.”
Yahvé m'a dit: « N'importune pas Moab et ne te bats pas avec lui, car je ne te donnerai aucune de ses terres en propriété, comme j'ai donné Ar en propriété aux enfants de Lot. »
10 (Aemi, anthu amphamvu ndi ochuluka komanso ataliatali ngati Aanaki amakhala kumeneko.
(Les Emim y habitaient auparavant, peuple grand et nombreux, et de taille égale à celle des Anakim.
11 Ngati Aanaki, nawonso ankawayesa kuti anali Arefai, koma Amowabu ankawatcha iwo Aemi.
Ceux-ci aussi sont considérés comme des Rephaïm, comme les Anakim; mais les Moabites les appellent Emim.
12 Ahori amakhala ku Seiri koma adzukulu a Esau anawapirikitsa. Iwo anawononga Ahori pamaso pawo nawakhalira pamalo pawo monga Aisraeli anachitira mʼdziko limene Yehova anawapatsa ngati chuma chawo).
Les Horites habitaient aussi autrefois en Séir, mais les fils d'Ésaü leur succédèrent. Ils les détruisirent devant eux et habitèrent à leur place, comme Israël l'a fait pour le pays qu'il possédait et que Yahvé leur avait donné).
13 Ndipo Yehova anati, “Tsopano nyamukani ndipo muwoloke Chigwa cha Zeredi.” Choncho tinawoloka chigwacho.
« Maintenant, lève-toi et traverse le torrent de Zered. » Nous avons traversé le ruisseau Zered.
14 Panapita zaka 38 kuchokera pa nthawi imene tinachoka ku Kadesi Barinea mpaka pamene tinawoloka Chigwa cha Zeredi. Pa nthawi imeneyi nʼkuti mʼbado wonse wa anthu ankhondowo utawonongeka ku msasa monga Yehova anawalumbirira.
Les jours que nous fîmes depuis Kadès-Barnéa jusqu'au passage du torrent de Zéred furent de trente-huit ans, jusqu'à ce que toute la génération des hommes de guerre eût disparu du milieu du camp, comme l'avait juré l'Éternel.
15 Dzanja la Yehova linatsutsana nawo mpaka wonse anathera ku msasa.
Et la main de l'Éternel fut contre eux, pour les détruire depuis le milieu du camp, jusqu'à ce qu'ils eussent disparu.
16 Tsono atafa munthu wotsiriza mwa anthu ankhondowo,
Lorsque tous les hommes de guerre furent consumés et morts parmi le peuple,
17 Yehova anati kwa ine,
l'Éternel me parla, et dit:
18 “Lero mudutsa malire a Mowabu ku Ari podzera ku Ari.
« Tu passeras aujourd'hui par Ar, la frontière de Moab.
19 Mukafika kwa Aamoni, musawavutitse kapena kuwaputa, popeza sindidzakupatsani gawo lililonse la dziko la Aamoni. Ine ndalipereka dzikoli ngati chuma kwa adzukulu a Loti.”
Quand tu approcheras de la frontière des enfants d'Ammon, ne les importune pas et ne leur cherche pas querelle, car je ne te donnerai aucune possession du pays des enfants d'Ammon, puisque je l'ai donné en possession aux enfants de Lot. »
20 (Ilinso ankaliyesa dziko la Arefai amene ankakhala kumeneko. Koma Aamoni ankawatcha iwo Azamuzumi.
(Cela aussi est considéré comme un pays de Rephaïm. Les Rephaïm y habitaient autrefois, mais les Ammonites les appellent Zamzummim,
21 Iwo anali anthu amphamvu ndiponso ochuluka, ataliatali ngati Aanaki. Yehova anawawononga ndi kuwachotsa pamaso pa Aamoni, amene anawapirikitsa nawakhalira pa malo pawo.
un peuple grand, nombreux et de haute taille, comme les Anakim; mais Yahvé les détruisit de devant Israël, et ils leur succédèrent et habitèrent à leur place,
22 Yehova anachitanso chimodzimodzi ndi adzukulu a Esau omwe anakhazikika ku Seiri atawononga Ahori powachotsa pamaso pawo. Iwo anawapirikitsa Ahoriwo ndi kuwakhalira pamalo pawo mpaka lero.
comme il fit pour les fils d'Ésaü qui habitent en Séir, lorsqu'il détruisit de devant eux les Horites; et ils leur succédèrent et habitèrent à leur place jusqu'à ce jour.
23 Ndipo za Aavi omwe ankakhala mʼmidzi yofika mpaka ku Gaza, anagonjetsedwa ndi Akafitori wochokera ku Akafitori nakhala pamalo pawo).
Puis les Avvim, qui habitaient des villages jusqu'à Gaza: les Caphtorim, sortis de Caphtor, les détruisirent et habitèrent à leur place).
24 “Tsopano nyamukani, muwoloke khwawa la Arinoni. Taona ndapereka mʼmanja mwako Sihoni Mwamori mfumu ya Hesiboni ndi dziko lake lonse. Yambapo kutenga chuma chake ndi kumenyana naye nkhondo.
« Lève-toi, pars, et franchis le torrent de l'Arnon. Voici, j'ai livré entre tes mains Sihon, l'Amoréen, roi de Hesbon, et son pays; commence à le posséder, et livre bataille contre lui.
25 Lero lomwe lino ndidzayamba kuyika chiopsezo ndi mantha pa mitundu yonse pansi pa thambo kuti akuope. Iwowo adzamva zambiri yako ndipo adzanjenjemera ndi kuwawidwa mtima chifukwa cha iwe.”
Aujourd'hui, je commencerai à mettre l'épouvante et la crainte de toi sur les peuples qui sont sous tout le ciel, qui entendront parler de toi, et qui trembleront et seront dans l'angoisse à cause de toi. »
26 Ine ndinatuma amithenga kuchokera ku chipululu cha Kedemoti kupita kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni kukanena mawu ofuna mtendere ndipo ndinati,
Du désert de Kedemoth, j'envoyai des messagers à Sihon, roi de Hesbon, avec des paroles de paix, en disant:
27 “Tiloleni tidutse mʼdziko mwanu. Ife tidzangodutsa ndi msewu waukulu, ndipo sitidzapatukira kumanja kapena kumanzere.
« Laisse-moi passer par ton pays. Je passerai par la route. Je ne me tournerai ni à droite ni à gauche.
28 Mutigulitse chakudya kuti tidye ndi madzi kuti timwe pa mtengo wa siliva. Mungotilola kuti tidutse, tikuyenda pansi
Tu me vendras à prix d'argent de la nourriture, pour que je mange, et tu me donneras à prix d'argent de l'eau, pour que je boive. Laissez-moi seulement passer sur mes pieds,
29 monga mmene anatichitira adzukulu a Esau okhala ku Seiri ndi Amowabu okhala ku Ari mpaka titawoloka Yorodani kufika ku dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.”
comme m'ont traité les enfants d'Ésaü qui habitent en Séir et les Moabites qui habitent à Ar, jusqu'à ce que je passe le Jourdain pour entrer dans le pays que Yahvé notre Dieu nous donne. »
30 Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanalole kuti tidutse. Popeza Yehova Mulungu wanu analimbitsa mzimu wake, nawumitsa mtima wake kuti amupereke mʼmanja mwanu monga wachitira lero lino.
Mais Sihon, roi de Heshbon, ne voulut pas nous laisser passer devant lui, car Yahvé ton Dieu avait endurci son esprit et rendu son cœur obstiné, afin de le livrer entre tes mains, comme c'est le cas aujourd'hui.
31 Yehova anati kwa ine, “Taona ndayamba kumupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Tsopano yamba kugonjetsa ndi kulanda dziko lake.”
Yahvé me dit: « Voici, j'ai commencé à livrer Sihon et son pays devant toi. Commence à le posséder, pour que tu hérites de son pays. »
32 Sihoni ndi ankhondo ake atabwera kudzakumana nafe mwankhondo pa Yahazi,
Alors Sihon sortit contre nous, lui et tout son peuple, pour combattre à Jahaz.
33 Yehova Mulungu anamupereka iye kwa ife ndipo tinankantha, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse lankhondo.
Yahvé notre Dieu le livra devant nous, et nous le frappâmes, lui, ses fils et tout son peuple.
34 Pa nthawi imeneyi tinamulanda mizinda yake yonse ndi kuyiwononga kwathunthu, amuna, akazi ndi ana. Palibe amene anapulumuka.
Nous prîmes alors toutes ses villes, et nous dévouâmes par interdit toutes les villes habitées, avec les femmes et les petits enfants. Nous n'avons laissé personne en vie.
35 Koma ziweto ndi zinthu zonse zimene tinalanda mʼmizinda imene tinagonjetsayo, tinazitenga kukhala zathu.
Nous ne prîmes pour nous que le bétail, avec le butin des villes que nous avions prises.
36 Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo.
Depuis Arœr, qui est au bord du torrent de l'Arnon, et la ville qui est dans la vallée, jusqu'à Galaad, il n'y avait pas de ville trop élevée pour nous. Yahvé notre Dieu a tout livré devant nous.
37 Molingana ndi lamulo la Yehova Mulungu wathu, simunalowerere dziko lililonse la Aamoni, ngakhale dera lonse la ku mtsinje wa Yaboki kapena dera lozungulira dera la ku mizinda ya ku mapiri.
Seulement, au pays des enfants d'Ammon, vous ne vous êtes pas approchés: toutes les rives du fleuve Jabbok, les villes de la montagne, et partout où Yahvé notre Dieu nous l'a interdit.

< Deuteronomo 2 >