< Deuteronomo 2 >
1 Kenaka tinabwerera ndi kuyamba ulendo wolowera ku chipululu motsatira njira ya ku Nyanja Yofiira, monga mmene Yehova anatilamulira. Kwa nthawi yayitali tinayendayenda cha ku dziko la mapiri la Seiri.
“Then we turned around and went through the desert toward the (Red Sea/Gulf of Aqaba), as Yahweh told us to do, and we wandered in the Edom area for many years.
2 Ndipo Yehova anati kwa ine,
Then Yahweh said to me,
3 “Mwazungulira mokwanira dziko la mapiri, tsopano tembenukirani kumpoto.
‘You have been wandering around this hilly area for a long enough time. Now turn [and travel] toward the north.
4 Apatse anthu malamulo awa: ‘Muli pafupi kudutsa mʼchigawo cha abale anu adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Iwowa adzachita nanu mantha koma musamale kwambiri.
And tell the people that they are about to travel near the land that belongs to the descendants of Esau, who are also descendants of Isaac. They live in the [hilly] Edom region. They will be afraid of you,
5 Musayambane nawo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo ngakhale poti mungoyika phazi. Ndamupatsa Esau dziko lamapiri la Seiri kuti likhale lakelake.
but do not start to fight against them, because I am not going to give you even a tiny bit [HYP] of their land. I have given that land to the descendants of Esau.
6 Inu muyenera kuwalipira ndi siliva pa chakudya chimene mudye ndi madzi amene mumwe.’”
[When you travel near their land], buy food and water from them.’
7 Yehova Mulungu wanu wakudalitsani mʼntchito zonse za manja anu. Iye wakuyangʼanirani pa ulendo wanu wodutsa mʼchipululu chachikulu. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu mʼzaka makumi anayi, ndipo simunasowe kalikonse.
Do not forget that Yahweh our God has blessed you in everything that you [SYN] have done. He knows [what has happened to you while] you have wandered in this huge desert. But he has been with you during those 40 years, and as a result you have had everything that you needed [LIT].
8 Choncho tinapitiriza ulendo modutsa abale athu, adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Tinapatukira njira ya ku Araba imene imachokera ku Elati ndi Ezioni Geberi ndipo tinayenda njira ya ku chipululu cha Mowabu.
So we continued to travel. We avoided going through the hilly area where the descendants of Esau live. We stayed away from the road through the Jordan [River] Valley past Ezion-Geber and Elath [towns], and we turned and traveled northeast toward the desert area where the Moab people-group lives.
9 Ndipo Yehova anati kwa ine, “Musawavutitse Amowabu kapena kuwaputa kuti muchite nawo nkhondo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo. Ndinapereka Ari kwa adzukulu a Loti ngati chuma chawo.”
Yahweh said to me, ‘Do not bother/harass the people of Moab, and do not start to fight against them, because I am not going to give you any of their land. [Do not forget that] they are descendants of [Abraham’s nephew] Lot, and I have given to them Ar [city, their capital, and the other areas in that country].’”
10 (Aemi, anthu amphamvu ndi ochuluka komanso ataliatali ngati Aanaki amakhala kumeneko.
A large group of giants called Emim formerly lived there. They were strong and numerous, and as tall as the giants who were descendants of Anak.
11 Ngati Aanaki, nawonso ankawayesa kuti anali Arefai, koma Amowabu ankawatcha iwo Aemi.
They and the descendants of Anak are also called the Repha giants, but the people of Moab call them Emim.
12 Ahori amakhala ku Seiri koma adzukulu a Esau anawapirikitsa. Iwo anawononga Ahori pamaso pawo nawakhalira pamalo pawo monga Aisraeli anachitira mʼdziko limene Yehova anawapatsa ngati chuma chawo).
The Hor people-group also formerly lived in the Edom area, but the descendants of Esau chased them out. They defeated and killed them and (settled in/occupied) their land, just as the Israeli people later expelled their enemies from the land that Yahweh gave to them.
13 Ndipo Yehova anati, “Tsopano nyamukani ndipo muwoloke Chigwa cha Zeredi.” Choncho tinawoloka chigwacho.
[I also said to the Israeli people], “Then we crossed the Zered Gorge, as Yahweh told us to do.
14 Panapita zaka 38 kuchokera pa nthawi imene tinachoka ku Kadesi Barinea mpaka pamene tinawoloka Chigwa cha Zeredi. Pa nthawi imeneyi nʼkuti mʼbado wonse wa anthu ankhondowo utawonongeka ku msasa monga Yehova anawalumbirira.
It had been thirty-eight years from the time we first left Kadesh-Barnea until we crossed the Zered Gorge. During those years, all the Israeli (fighting men/soldiers) of that generation had died, as Yahweh had vowed would happen.
15 Dzanja la Yehova linatsutsana nawo mpaka wonse anathera ku msasa.
They died because Yahweh opposed them, until he had gotten rid of all of them.
16 Tsono atafa munthu wotsiriza mwa anthu ankhondowo,
After all the men who had been old enough to fight in wars had died [DOU],
18 “Lero mudutsa malire a Mowabu ku Ari podzera ku Ari.
‘Today you all must cross the border into the Moab region, near Ar, [their capital city].
19 Mukafika kwa Aamoni, musawavutitse kapena kuwaputa, popeza sindidzakupatsani gawo lililonse la dziko la Aamoni. Ine ndalipereka dzikoli ngati chuma kwa adzukulu a Loti.”
When you come near the border of the land where the Ammon people-group live, do not bother/harass them or start to fight against them. They are also descendants of Lot, so I am not going to give you any of the land that I have given to them.’”
20 (Ilinso ankaliyesa dziko la Arefai amene ankakhala kumeneko. Koma Aamoni ankawatcha iwo Azamuzumi.
That region is also called the land of the Repha giants, who formerly lived there. The Ammon people-group call them the Zamzum group.
21 Iwo anali anthu amphamvu ndiponso ochuluka, ataliatali ngati Aanaki. Yehova anawawononga ndi kuwachotsa pamaso pa Aamoni, amene anawapirikitsa nawakhalira pa malo pawo.
They were a large and powerful group, who were as tall as the descendants of Anak. But Yahweh got rid of them, and the Ammon people-group expelled them and took their land away from them and started to live there.
22 Yehova anachitanso chimodzimodzi ndi adzukulu a Esau omwe anakhazikika ku Seiri atawononga Ahori powachotsa pamaso pawo. Iwo anawapirikitsa Ahoriwo ndi kuwakhalira pamalo pawo mpaka lero.
Yahweh had done the same thing for the descendants of Esau who live in the hilly area of Edom. He got rid of the Hor people-group, with the result that the Edom people-group took their land from them and started to live there. They still live there.
23 Ndipo za Aavi omwe ankakhala mʼmidzi yofika mpaka ku Gaza, anagonjetsedwa ndi Akafitori wochokera ku Akafitori nakhala pamalo pawo).
People who came from Crete [Island] got rid of the Av group [who previously lived in the land close to the Mediterranean Sea], as far south as Gaza. They took their land from them and started to live there.
24 “Tsopano nyamukani, muwoloke khwawa la Arinoni. Taona ndapereka mʼmanja mwako Sihoni Mwamori mfumu ya Hesiboni ndi dziko lake lonse. Yambapo kutenga chuma chake ndi kumenyana naye nkhondo.
“[After we had gone through the Moab region], Yahweh said to us, ‘Now cross the Arnon [River]. I will help you to defeat [IDM] [the army of] Sihon, the king of the Amor people-group, who lives in Heshbon [city]. So attack their army and start to take their land from them.
25 Lero lomwe lino ndidzayamba kuyika chiopsezo ndi mantha pa mitundu yonse pansi pa thambo kuti akuope. Iwowo adzamva zambiri yako ndipo adzanjenjemera ndi kuwawidwa mtima chifukwa cha iwe.”
Today I will begin to cause everyone, everywhere, to be afraid of you. Everyone who hears about you will tremble and be terrified.’
26 Ine ndinatuma amithenga kuchokera ku chipululu cha Kedemoti kupita kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni kukanena mawu ofuna mtendere ndipo ndinati,
Then I sent messengers to go from the desert to King Sihon at Heshbon. I told them to give this peaceful message to the king:
27 “Tiloleni tidutse mʼdziko mwanu. Ife tidzangodutsa ndi msewu waukulu, ndipo sitidzapatukira kumanja kapena kumanzere.
‘Please allow us to travel through your land. We [promise that we] will stay on the road; we will not turn off to the right or to the left.
28 Mutigulitse chakudya kuti tidye ndi madzi kuti timwe pa mtengo wa siliva. Mungotilola kuti tidutse, tikuyenda pansi
We will pay for any food or water that you allow us to buy. We want only to walk through your country,
29 monga mmene anatichitira adzukulu a Esau okhala ku Seiri ndi Amowabu okhala ku Ari mpaka titawoloka Yorodani kufika ku dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.”
until we cross the Jordan [River] into the land that Yahweh our God is giving to us. Do for us just as the descendants of Esau who live in the Edom area and the Moab people-group did for us when they allowed us to go through their areas.’
30 Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanalole kuti tidutse. Popeza Yehova Mulungu wanu analimbitsa mzimu wake, nawumitsa mtima wake kuti amupereke mʼmanja mwanu monga wachitira lero lino.
But King Sihon would not allow us to go through his country. That was because Yahweh our God caused him to be stubborn [IDM]. The result was that Yahweh enabled us to defeat his army and take his land [IDM], which we still live in.
31 Yehova anati kwa ine, “Taona ndayamba kumupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Tsopano yamba kugonjetsa ndi kulanda dziko lake.”
Yahweh said to me, ‘Listen! I am about to allow you to defeat Sihon’s [army] and to take the people’s land from them. So start to occupy it!’
32 Sihoni ndi ankhondo ake atabwera kudzakumana nafe mwankhondo pa Yahazi,
Then Sihon came out [of the city] with all his army to fight against us at Jahaz [town].
33 Yehova Mulungu anamupereka iye kwa ife ndipo tinankantha, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse lankhondo.
But God enabled us to defeat [DOU] them, and we killed Sihon and his sons and all his soldiers.
34 Pa nthawi imeneyi tinamulanda mizinda yake yonse ndi kuyiwononga kwathunthu, amuna, akazi ndi ana. Palibe amene anapulumuka.
We captured all their cities and destroyed them all. We killed all the men and women and children; we did not allow any of them to remain alive.
35 Koma ziweto ndi zinthu zonse zimene tinalanda mʼmizinda imene tinagonjetsayo, tinazitenga kukhala zathu.
We took the valuable things that were in the cities that we captured and also their cattle.
36 Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo.
Yahweh our God enabled us to capture [IDM] all their towns from Aroer [in the south], which is at the edge of the Arnon River [Valley], to the Gilead [region in the north]. Some of their cities had [walls around them], but we were able to [climb over them].
37 Molingana ndi lamulo la Yehova Mulungu wathu, simunalowerere dziko lililonse la Aamoni, ngakhale dera lonse la ku mtsinje wa Yaboki kapena dera lozungulira dera la ku mizinda ya ku mapiri.
But we did not go near the area where the Ammon people-group live, or the banks of the Jabbok riverbed, or the towns in the hilly area, or any other place where Yahweh our God told us not to go.”