< Deuteronomo 2 >

1 Kenaka tinabwerera ndi kuyamba ulendo wolowera ku chipululu motsatira njira ya ku Nyanja Yofiira, monga mmene Yehova anatilamulira. Kwa nthawi yayitali tinayendayenda cha ku dziko la mapiri la Seiri.
“And setting out from there, we arrived at the wilderness which leads to the Red Sea, just as the Lord had spoken to me. And we encompassed Mount Seir for a long time.
2 Ndipo Yehova anati kwa ine,
And the Lord said to me:
3 “Mwazungulira mokwanira dziko la mapiri, tsopano tembenukirani kumpoto.
‘You have encompassed this mountain for long enough. Go forth, toward the north.
4 Apatse anthu malamulo awa: ‘Muli pafupi kudutsa mʼchigawo cha abale anu adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Iwowa adzachita nanu mantha koma musamale kwambiri.
And instruct the people, saying: You shall cross through the borders of your brothers, the sons of Esau, who live at Seir, and they will fear you.
5 Musayambane nawo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo ngakhale poti mungoyika phazi. Ndamupatsa Esau dziko lamapiri la Seiri kuti likhale lakelake.
Therefore, take care diligently, lest you be moved against them. For I will not give to you from their land even as much as the step that one foot can tread upon, because I have given Mount Seir to Esau as a possession.
6 Inu muyenera kuwalipira ndi siliva pa chakudya chimene mudye ndi madzi amene mumwe.’”
You shall buy food from them for money, and you shall eat. You shall draw water for money, and you shall drink.
7 Yehova Mulungu wanu wakudalitsani mʼntchito zonse za manja anu. Iye wakuyangʼanirani pa ulendo wanu wodutsa mʼchipululu chachikulu. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu mʼzaka makumi anayi, ndipo simunasowe kalikonse.
The Lord your God has blessed you in every work of your hands. The Lord your God, dwelling with you, knows your journey, how you crossed through this great wilderness over forty years, and how you have been lacking in nothing.’
8 Choncho tinapitiriza ulendo modutsa abale athu, adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Tinapatukira njira ya ku Araba imene imachokera ku Elati ndi Ezioni Geberi ndipo tinayenda njira ya ku chipululu cha Mowabu.
And when we had passed through our brothers, the sons of Esau, who were living at Seir by the way of the plain from Elath and from Eziongeber, we arrived at the way which leads to the desert of Moab.
9 Ndipo Yehova anati kwa ine, “Musawavutitse Amowabu kapena kuwaputa kuti muchite nawo nkhondo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo. Ndinapereka Ari kwa adzukulu a Loti ngati chuma chawo.”
And the Lord said to me: ‘You should not fight against the Moabites, nor should you go to battle against them. For I will not give to you anything from their land, because I have given Ar to the sons of Lot as a possession.’
10 (Aemi, anthu amphamvu ndi ochuluka komanso ataliatali ngati Aanaki amakhala kumeneko.
The Emim were the first of its inhabitants, a people great and strong, and of such great height, like the race of the Anakim.
11 Ngati Aanaki, nawonso ankawayesa kuti anali Arefai, koma Amowabu ankawatcha iwo Aemi.
They were considered to be like giants, and they were like the sons of the Anakim. And, indeed, the Moabites call them: the Emim.
12 Ahori amakhala ku Seiri koma adzukulu a Esau anawapirikitsa. Iwo anawononga Ahori pamaso pawo nawakhalira pamalo pawo monga Aisraeli anachitira mʼdziko limene Yehova anawapatsa ngati chuma chawo).
The Horites also formerly lived at Seir. When these had been driven out and destroyed, the sons of Esau lived there, just as Israel did in the land of his possession, which the Lord gave to him.
13 Ndipo Yehova anati, “Tsopano nyamukani ndipo muwoloke Chigwa cha Zeredi.” Choncho tinawoloka chigwacho.
Then, rising up so as to cross over the torrent Zered, we arrived at the place.
14 Panapita zaka 38 kuchokera pa nthawi imene tinachoka ku Kadesi Barinea mpaka pamene tinawoloka Chigwa cha Zeredi. Pa nthawi imeneyi nʼkuti mʼbado wonse wa anthu ankhondowo utawonongeka ku msasa monga Yehova anawalumbirira.
Then, from the time that we advanced from Kadesh-barnea until we crossed over the torrent Zered, there were thirty-eight years, until the entire generation of the men who were fit for war had been consumed out of the camp, just as the Lord had sworn.
15 Dzanja la Yehova linatsutsana nawo mpaka wonse anathera ku msasa.
For his hand was against them, so that they would pass away from the midst of the camp.
16 Tsono atafa munthu wotsiriza mwa anthu ankhondowo,
Then, after all the fighting men had fallen,
17 Yehova anati kwa ine,
the Lord spoke to me, saying:
18 “Lero mudutsa malire a Mowabu ku Ari podzera ku Ari.
‘Today, you shall cross the borders of Moab, at the city named Ar.
19 Mukafika kwa Aamoni, musawavutitse kapena kuwaputa, popeza sindidzakupatsani gawo lililonse la dziko la Aamoni. Ine ndalipereka dzikoli ngati chuma kwa adzukulu a Loti.”
And when you have arrived in the vicinity of the sons of Ammon, be careful that you do not fight against them, nor should you be moved to battle. For I will not give to you from the land of the sons of Ammon, because I have given it to the sons of Lot as a possession.’
20 (Ilinso ankaliyesa dziko la Arefai amene ankakhala kumeneko. Koma Aamoni ankawatcha iwo Azamuzumi.
It was reputed to be a land of giants. And giants lived there in times past, those whom the Ammonites call the Zamzummim.
21 Iwo anali anthu amphamvu ndiponso ochuluka, ataliatali ngati Aanaki. Yehova anawawononga ndi kuwachotsa pamaso pa Aamoni, amene anawapirikitsa nawakhalira pa malo pawo.
They are a people, great and numerous, and of lofty stature, like the Anakim, whom the Lord wiped away before their face. And he caused them to live there in place of them,
22 Yehova anachitanso chimodzimodzi ndi adzukulu a Esau omwe anakhazikika ku Seiri atawononga Ahori powachotsa pamaso pawo. Iwo anawapirikitsa Ahoriwo ndi kuwakhalira pamalo pawo mpaka lero.
just as he had done for the sons of Esau, who live at Seir, wiping out the Horites and delivering their land to them, which they possess even to the present time.
23 Ndipo za Aavi omwe ankakhala mʼmidzi yofika mpaka ku Gaza, anagonjetsedwa ndi Akafitori wochokera ku Akafitori nakhala pamalo pawo).
Likewise the Hevites, who were living in small villages as far as Gaza, were expelled by the Cappadocians, who went forth from Cappadocia, and they wiped them out and lived in their place.
24 “Tsopano nyamukani, muwoloke khwawa la Arinoni. Taona ndapereka mʼmanja mwako Sihoni Mwamori mfumu ya Hesiboni ndi dziko lake lonse. Yambapo kutenga chuma chake ndi kumenyana naye nkhondo.
‘Rise up and cross the torrent Arnon! Behold, I have delivered Sihon, the king of Heshbon, the Amorite, into your hand, and so, begin to possess his land and to engage in battle against him.
25 Lero lomwe lino ndidzayamba kuyika chiopsezo ndi mantha pa mitundu yonse pansi pa thambo kuti akuope. Iwowo adzamva zambiri yako ndipo adzanjenjemera ndi kuwawidwa mtima chifukwa cha iwe.”
Today I will begin to send the terror and dread of you among the peoples who are living under all of heaven, so that, when they hear your name, they may be afraid, and may tremble in the manner of a woman giving birth, and may be gripped by anguish.’
26 Ine ndinatuma amithenga kuchokera ku chipululu cha Kedemoti kupita kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni kukanena mawu ofuna mtendere ndipo ndinati,
Therefore, I sent messengers from the wilderness of Kedemoth to Sihon, the king of Heshbon, with peaceful words, saying:
27 “Tiloleni tidutse mʼdziko mwanu. Ife tidzangodutsa ndi msewu waukulu, ndipo sitidzapatukira kumanja kapena kumanzere.
‘We will cross through your land. We will advance by the public way. We will not turn aside, neither to the right, nor to the left.
28 Mutigulitse chakudya kuti tidye ndi madzi kuti timwe pa mtengo wa siliva. Mungotilola kuti tidutse, tikuyenda pansi
Sell us food for a price, so that we may eat. Provide us with water for money, and so we will drink. We only ask that you allow us to pass through,
29 monga mmene anatichitira adzukulu a Esau okhala ku Seiri ndi Amowabu okhala ku Ari mpaka titawoloka Yorodani kufika ku dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.”
just as the sons of Esau have done, who live at Seir, and the Moabites, who abide in Ar, until we arrive at the Jordan, and we cross to the land which the Lord our God will give to us.’
30 Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanalole kuti tidutse. Popeza Yehova Mulungu wanu analimbitsa mzimu wake, nawumitsa mtima wake kuti amupereke mʼmanja mwanu monga wachitira lero lino.
And Sihon, the king of Heshbon, was not willing to grant passage to us. For the Lord your God had hardened his spirit, and had fastened his heart, so that he would be delivered into your hands, just as you now see.
31 Yehova anati kwa ine, “Taona ndayamba kumupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Tsopano yamba kugonjetsa ndi kulanda dziko lake.”
And the Lord said to me: ‘Behold, I have begun to deliver Sihon and his land to you. Begin to possess it.’
32 Sihoni ndi ankhondo ake atabwera kudzakumana nafe mwankhondo pa Yahazi,
And Sihon went out to meet us with all his people, to battle at Jahaz.
33 Yehova Mulungu anamupereka iye kwa ife ndipo tinankantha, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse lankhondo.
And the Lord our God delivered him to us. And we struck him down, with his sons and all his people.
34 Pa nthawi imeneyi tinamulanda mizinda yake yonse ndi kuyiwononga kwathunthu, amuna, akazi ndi ana. Palibe amene anapulumuka.
And we seized all his cities at that time, putting to death their inhabitants: men as well as women and children. We left nothing of them,
35 Koma ziweto ndi zinthu zonse zimene tinalanda mʼmizinda imene tinagonjetsayo, tinazitenga kukhala zathu.
except the cattle, which went to the share of those who plundered them. And we seized the spoils of the cities,
36 Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo.
from Aroer, which is above the bank of the torrent Arnon, a town which is situated in a valley, all the way to Gilead. There was not a village or city which escaped from our hands. The Lord our God delivered everything to us,
37 Molingana ndi lamulo la Yehova Mulungu wathu, simunalowerere dziko lililonse la Aamoni, ngakhale dera lonse la ku mtsinje wa Yaboki kapena dera lozungulira dera la ku mizinda ya ku mapiri.
except the land of the sons of Ammon, which we did not approach, and all that is adjacent to the torrent Jabbok, and the cities in the mountains, and all the places which the Lord our God prohibited to us.”

< Deuteronomo 2 >